< Yesaya 36 >

1 Chaka cha khumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya ku Yuda, nayilanda.
Un notikās ķēniņa Hizkijas četrpadsmitā gadā, tad Sanheribs, Asīrijas ķēniņš, cēlās pret visām stiprām Jūda pilsētām un tās uzņēma.
2 Kenaka mfumu ya ku Asiriya inatuma kazembe wake wankhondo pamodzi ndi gulu lalikulu lankhondo kuchokera ku Lakisi kupita kwa mfumu Hezekiya ku Yerusalemu. Tsono kazembeyo anayima pafupi ndi ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe lakumtunda pa msewu wopita ku malo a munda wa mmisiri wochapa zovala.
Un Asīrijas ķēniņš sūtīja Rabzaku no Laķisa uz Jeruzālemi pie ķēniņa Hizkijas ar varen lielu karaspēku, un viņš stāvēja pie augšēja dīķa grāvjiem, vadmalnieka tīruma ceļa malā.
3 Panali anthu atatu. Woyamba anali Eliyakimu mwana wa Hilikiya komanso ndiye woyangʼanira nyumba ya mfumu. Wachiwiri anali Sebina amene anali mlembi wa bwalo; ndipo wachitatu anali Yowa mwana wa Asafu komanso anali wolemba zochitika. Anthu awa anatuluka kukakumana ndi kazembe wa ankhondo uja.
Tad pie viņa izgāja nama uzraugs Elijaķims, Hilķijas dēls, un skrīveris Šebna, un kanclers Joaks, Asafa dēls.
4 Kazembe wa ankhondo anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?
Un Rabzakus uz tiem sacīja: sakāt jel Hizkijam: Tā saka tas lielais ķēniņš, Asīrijas ķēniņš: Kas tas tāds patvērums, uz ko tu paļaujies?
5 Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
Es saku: tas ir tukšs vārds, ka diezgan esot padoma un spēka uz karu; uz ko tad tu paļaujies, ka tu no manis esi atkritis?
6 Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.
Redzi, tu paļaujies uz to salūzušo niedri, uz Ēģipti. Kas uz to atspiežas, tam tā ies rokā un to pārdurs. Tāds ir faraons, Ēģiptes ķēniņš, visiem, kas uz viņu paļaujas.
7 Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, ‘Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu,’ kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake, Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe ili?’
Bet ja tu uz mani saki: Mēs paļaujamies uz To Kungu, savu Dievu, - vai tas nav tas pats, kam kalnus un altārus Hizkija ir nopostījis un sacījis uz Jūdu un Jeruzālemi: priekš šī altāra še jums būs pielūgt?
8 “Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: Ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
Nu tad, noderi jel ar manu kungu, Asīrijas ķēniņu, un es tev došu divtūkstoš zirgus, ja tev ir jātnieki, ko tiem likt virsū.
9 Iwe ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo.
Kā tad tu varēsi atsist atpakaļ vienu pašu virsnieku no mana kunga vismazākiem kalpiem? Bet tu paļaujies uz Ēģipti, ratu un jātnieku dēļ.
10 Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga dziko lino popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.”
Vai tad nu es bez Tā Kunga esmu cēlies pret šo zemi, to izpostīt? Tas Kungs uz mani sacījis: Celies pret šo zemi un izposti to!
11 Pamenepo Eliyakimu, Sebina ndi Yowa anawuza kazembeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
Tad Elijaķims un Šebna un Joāks sacīja uz Rabzaku: Runā jel ar saviem kalpiem sīriski, mēs to gan protam, un nerunā ar mums jūdiski priekš šo ļaužu ausīm, kas ir uz mūra.
12 Koma kazembeyo anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
Bet Rabzakus sacīja: Vai mans kungs mani sūtījis pie tava kunga un pie tevis, šos vārdus runāt, vai ne pie tiem vīriem, kas sēž uz mūra, kam līdz ar jums būs jāēd savi sūdi un jādzer savi mīzali?
13 Tsono kazembeyo anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
Un Rabzakus nostājās un sauca ar stipru balsi jūdiski un sacīja: klausāties tā lielā ķēniņa, Asīrijas ķēniņa, vārdus!
14 Zimene mfumu ikunena ndi izi: Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni!
Tā saka ķēniņš: Lai Hizkija jūs neapmāna, jo viņš jūs nevarēs izglābt.
15 Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
Lai arī Hizkija jums nedara cerību uz To Kungu, sacīdams: tiešām, Tas Kungs mūs izglābs, šī pilsēta netaps dota Asīrijas ķēniņa rokā!
16 “Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
Neklausāties uz Hizkiju. Jo tā saka Asīrijas ķēniņš: Deriet ar mani mieru un nākat pie manis ārā, tad ikviens ēdīs no sava vīna koka un ikviens no sava vīģes koka, un ikviens dzers ūdeni no savas akas,
17 mpaka mfumuyo itabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanulo, dziko limene lili ndi tirigu ndi vinyo watsopano, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
Kamēr es nākšu, un jūs aizvedīšu tādā zemē, kā jūsu zeme, zeme, kur ir labība un vīns, zeme, kur ir maize un vīna dārzi.
18 “Inu musalole kuti Hezekiya akusocheretseni pamene iye akuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’ Kodi alipo mulungu wa anthu a mtundu wina amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
Lai Hizkija jūs nepieviļ, sacīdams: Tas Kungs mūs izglābs! Vai gan pagānu dievi ikviens savu zemi izglābuši no Asīrijas ķēniņa rokas?
19 Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
Kur ir Hamatas un Arpadas dievi, kur ir Sefarvaimas dievi? Vai tie gan Samariju izglābuši no manas rokas?
20 Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
Kurš no visiem šo zemju dieviem savu zemi izglābis no manas rokas? Kā tad Tas Kungs Jeruzālemi izglābs no manas rokas?
21 Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
Bet tie cieta klusu un viņam neatbildēja neviena vārda, jo ķēniņš bija pavēlējis un sacījis: Jums nebūs viņam atbildēt.
22 Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu; Sebina mlembi wa bwalo; ndi Yowa, mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza zonse zimene anayankhula kazembe uja.
Tad nama uzraugs Elijaķims, Hilķijas dēls, un skrīveris Šebna un kanclers Joaks, Asafa dēls, nāca pie Hizkijas ar saplēstām drēbēm un viņam stāstīja Rabzakus vārdus.

< Yesaya 36 >