< Yesaya 36 >

1 Chaka cha khumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya ku Yuda, nayilanda.
Og det skete i Kong Ezekias's fjortende Aar, at Senakerib, Kongen af Assyrien, drog op imod alle Judas faste Stæder og indtog dem.
2 Kenaka mfumu ya ku Asiriya inatuma kazembe wake wankhondo pamodzi ndi gulu lalikulu lankhondo kuchokera ku Lakisi kupita kwa mfumu Hezekiya ku Yerusalemu. Tsono kazembeyo anayima pafupi ndi ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe lakumtunda pa msewu wopita ku malo a munda wa mmisiri wochapa zovala.
Og Kongen af Assyrien sendte Rabsake fra Lakis til Jerusalem til Kong Ezekias med en svar Hær; og han stod ved den øverste Dams Vandledning, som er ved den alfare Vej til Blegerens Ager.
3 Panali anthu atatu. Woyamba anali Eliyakimu mwana wa Hilikiya komanso ndiye woyangʼanira nyumba ya mfumu. Wachiwiri anali Sebina amene anali mlembi wa bwalo; ndipo wachitatu anali Yowa mwana wa Asafu komanso anali wolemba zochitika. Anthu awa anatuluka kukakumana ndi kazembe wa ankhondo uja.
Da gik Eliakim, Hilkias Søn, som var Hofmester, og Sebna, Kansleren, og Joa, Asafs Søn, Historieskriveren, ud til ham.
4 Kazembe wa ankhondo anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?
Og Rabsake sagde til dem: Siger til Ezekias: Saa siger den store Konge, Kongen af Assyrien: Hvad er det for en Tillid, som du forlader dig paa?
5 Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
Jeg siger — dog det er ikkun Læbers Ord — at der er Klogskab og Styrke til Krigen; nu, paa hvem forlader du dig, eftersom du er affalden fra mig?
6 Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.
Se, du forlader dig paa denne brudte Rørkæp, paa Ægypten; støtter nogen sig paa den, da gaar den ind i hans Haand og borer den igennem; saaledes er Farao, Kongen i Ægypten, for alle dem, som forlade sig paa ham.
7 Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, ‘Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu,’ kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake, Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe ili?’
Og om du vil sige til mig: Vi forlade os paa Herren vor Gud, er det da ikke ham, hvis Høje og hvis Altre Ezekias har borttaget, idet han sagde til Juda og til Jerusalem: For dette Alter skulle I tilbede?
8 “Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: Ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
Og nu, indgaa Væddemaal med min Herre, Kongen af Assyrien, saa vil jeg give dig to Tusinde Heste, om du kan skaffe dig Ryttere til dem.
9 Iwe ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo.
Hvorledes vilde du da drive en Fyrstes Magt tilbage, hørte han end til min Herres ringeste Tjenere? men du forlader dig paa Ægypten, for Vognes og for Rytteres Skyld.
10 Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga dziko lino popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.”
Og nu, mon jeg vel uden Herren er dragen op imod dette Land for at ødelægge det? Herren sagde til mig: Drag op imod dette Land og ødelæg det!
11 Pamenepo Eliyakimu, Sebina ndi Yowa anawuza kazembeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
Da sagde Eliakim og Sebna og Joa til Rabsake: Kære, tal til dine Tjenere paa Syrisk, thi vi forstaa det; og tal ikke til os paa jødisk for Folkets Øren, som er paa Muren.
12 Koma kazembeyo anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
Men Rabsake sagde: Har min Herre sendt mig til din Herre eller til dig for at tale disse Ord? mon ikke til de Mænd, som sidde paa Muren, og som skulle komme til at æde deres eget Skarn og drikke deres eget Vand med eder?
13 Tsono kazembeyo anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
Saa stod Rabsake og raabte med høj Røst paa jødisk og sagde: Hører den store Konges Ord, Kongens af Assyrien!
14 Zimene mfumu ikunena ndi izi: Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni!
Saa sagde Kongen: Lader ikke Ezekias bedrage eder! thi han formaar ikke at redde eder.
15 Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
Og lader ikke Ezekias faa eder til at forlade eder paa Herren, idet han siger: Herren skal visselig fri os; denne Stad skal ikke gives i Kongen af Assyriens Haand.
16 “Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
Lyder ikke Ezekias ad; thi saa sagde Kongen af Assyrien: Slutter Fred med mig, og gaar ud til mig og æder, hver af sit Vintræ og hver af sit Figentræ, og drikker hver Vand af sin Brønd,
17 mpaka mfumuyo itabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanulo, dziko limene lili ndi tirigu ndi vinyo watsopano, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
indtil jeg kommer og henter eder til et Land som eders Land, et Land, i hvilket der er Korn og Vin, et Land, i hvilket der er Brød og Vingaarde.
18 “Inu musalole kuti Hezekiya akusocheretseni pamene iye akuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’ Kodi alipo mulungu wa anthu a mtundu wina amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
Lader ikke Ezekias tilskynde eder, idet han siger: Herren skal fri os; have Hedningernes Guder vel friet hver sit Land af Kongen af Assyriens Haand?
19 Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
Hvo ere de Guder af Hamat og Arfad? hvo ere de Guder af Sefarvajm? og mon de have reddet Samaria af min Haand?
20 Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
Hvo iblandt alle disse Landes Guder er der, som have friet deres Land af min Haand, og Herren skulde redde Jerusalem af min Haand?
21 Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
Og de tav og svarede ham ikke et Ord; thi det var Kongens Befaling, som havde sagt: Svar ham intet!
22 Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu; Sebina mlembi wa bwalo; ndi Yowa, mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza zonse zimene anayankhula kazembe uja.
Da kom Eliakim, Hilkias Søn, som var Hofmester, og Sebna, Kansleren, og Joa, Asafs Søn, Historieskriveren, til Ezekias med sønderrevne Klæder; og de gave ham Rabsakes Ord til Kende.

< Yesaya 36 >