< Yesaya 35 >
1 Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala; dziko lowuma lidzakondwa ndi kuchita maluwa.
Çöl ve kurak toprak sevinecek, Bozkır coşup çiğdem gibi çiçeklenecek.
2 Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe. Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni, maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni. Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova, ukulu wa Mulungu wathu.
Her yanı çiçeklenip sevinçle coşacak, Sevincini haykıracak. Lübnan'ın yüceliği, Karmel ve Şaron'un görkemi ona verilecek. İnsanlar RAB'bin yüceliğini, Tanrımız'ın görkemini görecek.
3 Limbitsani manja ofowoka, limbitsani mawondo agwedegwede;
Gevşek elleri güçlendirin, Pekiştirin çözülen dizleri.
4 nenani kwa a mitima yamantha kuti; “Limbani mtima, musachite mantha; Mulungu wanu akubwera, akubwera kudzalipsira; ndi kudzabwezera chilango adani anu; akubwera kudzakupulumutsani.”
Yüreği kaygılı olanlara, “Güçlü olun, korkmayın” deyin, “İşte Tanrınız geliyor! Öç almaya, karşılık vermeye geliyor. Sizi O kurtaracak.”
5 Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
O zaman körlerin gözleri, Sağırların kulakları açılacak;
6 Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala, ndipo osayankhula adzayimba mokondwera. Akasupe adzatumphuka mʼchipululu ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
Topallar geyik gibi sıçrayacak, Sevinçle haykıracak dilsizlerin dili. Çünkü çölde sular fışkıracak, Irmaklar akacak bozkırda.
7 mchenga wotentha udzasanduka dziwe, nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe. Pamene panali mbuto ya ankhandwe padzamera udzu ndi bango.
Kızgın kum havuza, Susuz toprak pınara dönüşecek. Çakalların yattığı yerlerde Kamış, saz ve ot bitecek.
8 Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu; ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika. Anthu odetsedwa sadzayendamo mʼmenemo; zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
Orada bir yol, bir anayol olacak, “Kutsal yol” diye anılacak, Murdar kişiler geçemeyecek oradan. O yol kurtulmuş olanların yoludur. O yolda yürüyenler, bön kişiler de olsa yoldan sapmayacak.
9 Kumeneko sikudzakhala mkango, ngakhale nyama yolusa sidzafikako; sidzapezeka konse kumeneko. Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
Aslan olmayacak orada, Yırtıcı hayvan o yola çıkmayacak; Orada bulunmayacaklar. Ancak kurtulmuş olanlar yürüyecek o yolda.
10 Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera. Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba; kumeneko adzakondwa mpaka muyaya. Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe, ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.
RAB'bin kurtardıkları dönecek, Sevinçle haykırarak Siyon'a varacaklar. Yüzlerinde sonsuz sevinç olacak. Onların olacak coşku ve sevinç, Üzüntü ve inilti kaçacak.