< Yesaya 35 >
1 Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala; dziko lowuma lidzakondwa ndi kuchita maluwa.
Inkangala lelizwe elomileyo kuzathokoza; inkangala izajabula iqhakaze. Njengeluba
2 Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe. Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni, maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni. Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova, ukulu wa Mulungu wathu.
izakhahlela, ithokoze kakhulu, ihlabele isithi. Inkazimulo yaseLebhanoni izanikezwa kuyo ubuhle beKhameli leSharoni, kuzabona inkazimulo kaThixo lobukhosi bukaNkulunkulu wethu.
3 Limbitsani manja ofowoka, limbitsani mawondo agwedegwede;
Qinisani izandla ezibuthakathaka, liqinise lamadolo axegayo;
4 nenani kwa a mitima yamantha kuti; “Limbani mtima, musachite mantha; Mulungu wanu akubwera, akubwera kudzalipsira; ndi kudzabwezera chilango adani anu; akubwera kudzakupulumutsani.”
tshonini kulabo abalezinhliziyo ezilokwesaba lithi: “Qinani, lingesabi; uNkulunkulu wenu uzakuza, uzakuza ezophindisela, ajezise ngokulunga uzakuza ukuba alikhulule.”
5 Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
Lapho-ke amehlo eziphofu azavuleka, lezindlebe zezacuthe zivuleke.
6 Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala, ndipo osayankhula adzayimba mokondwera. Akasupe adzatumphuka mʼchipululu ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
Lapho-ke abaqhulayo bazakweqa njengempala, izimungulu zihlabele ngokuthokoza. Amanzi azampompoza ogwaduleni, izifula zigeleze enkangala.
7 mchenga wotentha udzasanduka dziwe, nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe. Pamene panali mbuto ya ankhandwe padzamera udzu ndi bango.
Itshebetshebe elitshisayo lizakuba yisiziba, umhlabathi owomileyo ube yimithombo echaphaka amanzi. Ezindaweni amakhanka ake ahlala kuzo, utshani lemihlanga lebhuma kuzakhula khona.
8 Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu; ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika. Anthu odetsedwa sadzayendamo mʼmenemo; zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
Njalo kuzakuba lomgwaqo omkhulu: uzathiwa yiNdlela yobuNgcwele, izakuba ngeyalabo abahamba ngokuqonda. Abangcolileyo kabayikuhamba kuwo; uzakuba ngowalabo abahamba kuleyoNdlela lezithutha ezonayo kaziyikuhambahamba kuwo.
9 Kumeneko sikudzakhala mkango, ngakhale nyama yolusa sidzafikako; sidzapezeka konse kumeneko. Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
Akuyikuba lesilwane khona, loba esinye isilo esilolaka; sivuke kuwo kaziyikutholwa khona. Kodwa abahlengiweyo yibo kuphela abazahamba lapho,
10 Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera. Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba; kumeneko adzakondwa mpaka muyaya. Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe, ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.
njalo labahlengiweyo bakaThixo bazabuyela. Bazangena eZiyoni behlabelela, intokozo engapheliyo izakuba ngumqhele emakhanda abo. Bazakuba lokuthula lenjabulo, usizi lokububula kuzaphela.