< Yesaya 35 >

1 Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala; dziko lowuma lidzakondwa ndi kuchita maluwa.
Que le désert et le sol brûlé se réjouissent! Que la plaine aride exulte et fleurisse comme la rose!
2 Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe. Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni, maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni. Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova, ukulu wa Mulungu wathu.
Qu’ils se couvrent de fleurs, que leur joie délirante se traduise par des chants, que la gloire du Liban leur soit prêtée, l’éclat du Carmel et du Saron! Ils vont voir la gloire de l’Eternel, la splendeur de notre Dieu.
3 Limbitsani manja ofowoka, limbitsani mawondo agwedegwede;
Fortifiez les mains défaillantes, affermissez les genoux vacillants.
4 nenani kwa a mitima yamantha kuti; “Limbani mtima, musachite mantha; Mulungu wanu akubwera, akubwera kudzalipsira; ndi kudzabwezera chilango adani anu; akubwera kudzakupulumutsani.”
Dites à ceux dont le cœur chancelle: "Prenez courage, ne craignez pas! Voici votre Dieu; la vengeance vient; elles viennent, les représailles de Dieu! Il va vous secourir!"
5 Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
Alors s’ouvriront les yeux des aveugles, et les oreilles des sourds seront débouchées.
6 Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala, ndipo osayankhula adzayimba mokondwera. Akasupe adzatumphuka mʼchipululu ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
Alors le boiteux bondira comme le chamois, la langue du muet entonnera des chants; car des sources d’eau jaillissent dans le désert, des rivières dans la plaine aride.
7 mchenga wotentha udzasanduka dziwe, nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe. Pamene panali mbuto ya ankhandwe padzamera udzu ndi bango.
Le mirage deviendra une nappe d’eau et le pays de la soif aura ses fontaines. La demeure où gîtent les bêtes sauvages sera une région couverte de roseaux et de joncs.
8 Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu; ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika. Anthu odetsedwa sadzayendamo mʼmenemo; zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
Là s’ouvrira une chaussée, une route qui sera appelée la route sacrée; aucun impur n’y passera: elle leur est réservée, à eux. Ceux qui la suivront, même les imprudents, ne pourront s’égarer.
9 Kumeneko sikudzakhala mkango, ngakhale nyama yolusa sidzafikako; sidzapezeka konse kumeneko. Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
Sur cette route, pas de lion à craindre, nulle bête féroce ne l’abordera: il ne s’en trouvera pas. Seuls les affranchis y marcheront.
10 Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera. Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba; kumeneko adzakondwa mpaka muyaya. Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe, ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.
Les rachetés de l’Eternel reviendront ainsi et rentreront dans Sion en chantant; une joie éternelle sur leur tête! Ils auront retrouvé contentement et allégresse: adieu peines et soupirs!

< Yesaya 35 >