< Yesaya 35 >

1 Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala; dziko lowuma lidzakondwa ndi kuchita maluwa.
Le désert et la terre aride se réjouiront; la steppe sera dans l’allégresse, et fleurira comme le narcisse;
2 Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe. Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni, maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni. Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova, ukulu wa Mulungu wathu.
il se couvrira de fleurs et tressaillira, il poussera des cris de joie. La gloire du Liban lui sera donnée, avec la magnificence du Carmel et de Saron. Ils verront la gloire de Yahweh, la magnificence de notre Dieu!
3 Limbitsani manja ofowoka, limbitsani mawondo agwedegwede;
Fortifiez les mains défaillantes, et affermissez les genoux qui chancellent!
4 nenani kwa a mitima yamantha kuti; “Limbani mtima, musachite mantha; Mulungu wanu akubwera, akubwera kudzalipsira; ndi kudzabwezera chilango adani anu; akubwera kudzakupulumutsani.”
Dites à ceux qui ont le cœur troublé: « Prenez courage, ne craignez point: Voici votre Dieu; la vengeance vient, une revanche divine, il vient lui-même et vous sauvera. »
5 Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
Alors s’ouvriront les yeux des aveugles, alors s’ouvriront les oreilles des sourds.
6 Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala, ndipo osayankhula adzayimba mokondwera. Akasupe adzatumphuka mʼchipululu ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
Le boiteux bondira comme un cerf, et la langue du muet éclatera de joie. Car des eaux jailliront dans le désert, et des ruisseaux dans la steppe,
7 mchenga wotentha udzasanduka dziwe, nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe. Pamene panali mbuto ya ankhandwe padzamera udzu ndi bango.
Le sol brûlé se changera en un lac, et la terre altérée en sources d’eaux; le repaire où gîtaient les chacals deviendra un parc de roseaux et de joncs.
8 Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu; ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika. Anthu odetsedwa sadzayendamo mʼmenemo; zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
Il y aura là une route, une voie, qu’on appellera la voie sainte; nul impur n’y passera; elle n’est que pour eux seuls; ceux qui la suivront, les simples mêmes, ne s’égareront pas.
9 Kumeneko sikudzakhala mkango, ngakhale nyama yolusa sidzafikako; sidzapezeka konse kumeneko. Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
Là il n’y aura pas de lion; aucune bête féroce n’y mettra le pied; on ne l’y trouvera pas. Les délivrés y marcheront,
10 Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera. Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba; kumeneko adzakondwa mpaka muyaya. Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe, ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.
et les rachetés de Yahweh reviendront; ils viendront en Sion avec des cris de joie; une allégresse éternelle couronnera leur tête; la joie et l’allégresse les envahiront, la douleur et le gémissement s’enfuiront.

< Yesaya 35 >