< Yesaya 34 >

1 Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve: tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse: Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
ای امت‌ها نزدیک آیید تا بشنوید! و‌ای قوم‌ها اصغا نمایید! جهان و پری آن بشنوند. ربع مسکون و هرچه از آن صادر باشد.۱
2 Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse; wapsera mtima magulu awo onse ankhondo. Iye adzawawononga kotheratu, nawapereka kuti aphedwe.
زیرا که غضب خداوند بر تمامی امت‌ها و خشم وی بر جمیع لشکرهای ایشان است پس ایشان رابه هلاکت سپرده، بقتل تسلیم نموده است.۲
3 Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja, mitembo yawo idzawola ndi kununkha; mapiri adzafiira ndi magazi awo.
وکشتگان ایشان دور افکنده می‌شوند و عفونت لاشهای ایشان برمی آید. و از خون ایشان کوههاگداخته می‌گردد.۳
4 Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala; nyenyezi zonse zidzayoyoka ngati masamba ofota a mphesa, ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.
و تمامی لشکر آسمان از هم خواهند پاشید و آسمان مثل طومار پیچیده خواهد شد. و تمامی لشکر آن پژمرده خواهندگشت، بطوریکه برگ از مو بریزد و مثل میوه نارس از درخت انجیر.۴
5 Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba; taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu, anthu amene ndawawononga kotheratu.”
زیرا که شمشیر من درآسمان سیراب شده است. و اینک بر ادوم و برقوم مغضوب من برای داوری نازل می‌شود.۵
6 Lupanga la Yehova lakhuta magazi, lakutidwa ndi mafuta; magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi, mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna. Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
شمشیر خداوند پر خون شده و از پیه فربه گردیده است یعنی از خون بره‌ها و بزها و از پیه گرده قوچها. زیرا خداوند را در بصره قربانی است و ذبح عظیمی در زمین ادوم.۶
7 Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati, ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe. Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha, ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.
و گاوان وحشی باآنها خواهند افتاد و گوساله‌ها با گاوان نر. و زمین ایشان از خون سیراب شده، خاک ایشان از پیه فربه خواهد شد.۷
8 Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira ndi kulanga adani a Ziyoni.
زیرا خداوند را روز انتقام و سال عقوبت به جهت دعوی صهیون خواهد بود.۸
9 Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula, ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule; dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
و نهرهای آن به قیر و غبار آن به کبریت مبدل خواهد شد وزمینش قیر سوزنده خواهد گشت.۹
10 Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana; utsi wake udzafuka kosalekeza. Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado; palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
شب و روزخاموش نشده، دودش تا به ابد خواهد برآمد. نسلا بعد نسل خراب خواهد ماند که کسی تاابدالاباد در آن گذر نکند.۱۰
11 Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu; amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo. Mulungu adzatambalitsa pa Edomu chingwe choyezera cha chisokonezo ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
بلکه مرغ سقا وخارپشت آن را تصرف خواهند کرد و بوم وغراب در آن ساکن خواهند شد و ریسمان خرابی و شاقول ویرانی را بر آن خواهد کشید.۱۱
12 Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko; akalonga ake onse adzachotsedwa.
و ازاشراف آن کسی در آنجا نخواهد بود که او را به پادشاهی بخوانند و جمیع روسایش نیست خواهند شد.۱۲
13 Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa, khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake. Ankhandwe azidzadya mʼmenemo; malo okhalamo akadzidzi.
و در قصرهایش خارها خواهدرویید و در قلعه هایش خسک و شتر خار و مسکن گرگ و خانه شترمرغ خواهد شد.۱۳
14 Avumbwe adzakumana ndi afisi, ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana. Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa ndi kupeza malo opumulirako.
و وحوش بیابان با شغال خواهند برخورد و غول به رفیق خود ندا خواهد داد و عفریت نیز در آنجا ماواگزیده، برای خود آرامگاهی خواهد یافت.۱۴
15 Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira, adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake; akamtema adzasonkhananso kumeneko, awiriawiri.
درآنجا تیرمار آشیانه ساخته، تخم خواهد نهاد و برآن نشسته، بچه های خود را زیر سایه خود جمع خواهد کرد و در آنجا کرکسها با یکدیگر جمع خواهند شد.۱۵
16 Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga: mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa; sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake. Pakuti Yehova walamula kuti zitero, ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
از کتاب خداوند تفتیش نموده، مطالعه کنید. یکی از اینها گم نخواهد شد و یکی جفت خود را مفقود نخواهد یافت زیرا که دهان او این را امر فرموده و روح او اینها را جمع کرده است.۱۶
17 Yehova wagawa dziko lawo; wapatsa chilichonse chigawo chake. Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.
و او برای آنها قرعه انداخته و دست اوآن را به جهت آنها با ریسمان تقسیم نموده است. و تا ابدالاباد متصرف آن خواهند شد و نسلا بعدنسل در آن سکونت خواهند داشت.۱۷

< Yesaya 34 >