< Yesaya 34 >

1 Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve: tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse: Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
Sondelani, zizwe, ukuze lizwe; lani bantu, lilalele; umhlaba kawuzwe, lokugcwala kwawo; ilizwe, lakho konke okuvela kilo.
2 Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse; wapsera mtima magulu awo onse ankhondo. Iye adzawawononga kotheratu, nawapereka kuti aphedwe.
Ngoba intukuthelo yeNkosi iphezu kwazo zonke izizwe, lolaka phezu kwawo wonke amabutho azo; izitshabalalisile, izinikele ekubulaweni.
3 Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja, mitembo yawo idzawola ndi kununkha; mapiri adzafiira ndi magazi awo.
Ababuleweyo bazo labo bazaphoselwa phandle, levumba labo lizakwenyuka ezidunjini zabo, lezintaba zizancibilika ngegazi labo.
4 Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala; nyenyezi zonse zidzayoyoka ngati masamba ofota a mphesa, ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.
Lalo lonke ibutho lamazulu lizabola; lamazulu agoqwe njengomqulu; lalo lonke ibutho labo liwele phansi, njengehlamvu liwohloka evinini, lanjengomkhiwa owohlokayo esihlahleni somkhiwa.
5 Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba; taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu, anthu amene ndawawononga kotheratu.”
Ngoba inkemba yami izacwila emazulwini; khangela, izakwehlela phezu kukaEdoma laphezu kwabantu bokutshabalalisa kwami ngesigwebo.
6 Lupanga la Yehova lakhuta magazi, lakutidwa ndi mafuta; magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi, mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna. Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
Inkemba yeNkosi igcwele igazi, inoniswe ngamafutha, ngegazi lamawundlu lelezimbuzi, ngamahwahwa ezinso zezinqama; ngoba iNkosi ilomhlatshelo eBhozira, lokubulala okukhulu elizweni leEdoma.
7 Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati, ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe. Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha, ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.
Lezinyathi zizakwehla kanye lazo, lamajongosi kanye lezinkunzi. Njalo ilizwe labo lizacwila egazini, lothuli lwabo lunoniswe ngamahwahwa.
8 Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira ndi kulanga adani a Ziyoni.
Ngoba kulusuku lwempindiselo yeNkosi, umnyaka wokubuyiselwa kwempikisano yeZiyoni.
9 Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula, ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule; dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
Lezifula zabo zizaphendulwa zibe yingcino, lothuli lwabo lube yisibabule; lelizwe labo lizakuba yingcino etshayo.
10 Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana; utsi wake udzafuka kosalekeza. Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado; palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
Kaliyikucitshwa ubusuku lemini; intuthu yalo izakwenyuka laphakade; kusukela esizukulwaneni kusiya kusizukulwana lizakuba yinkangala; kakho ozadabula phakathi kwalo kuze kube nini lanini.
11 Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu; amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo. Mulungu adzatambalitsa pa Edomu chingwe choyezera cha chisokonezo ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
Kodwa iwunkwe lenhloni kuzakudla ilifa lalo; isikhova laso lewabayi kuzahlala kulo. Njalo izakwelula phezu kwalo intambo yencithakalo, lamatshe onxiwa.
12 Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko; akalonga ake onse adzachotsedwa.
Bazabizela izikhulu zalo embusweni, kodwa kakho ozakuba khona, leziphathamandla zalo zonke zizakuba yinto engelutho.
13 Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa, khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake. Ankhandwe azidzadya mʼmenemo; malo okhalamo akadzidzi.
Lameva azakhula ezigodlweni zalo, imbabazane lokhula oluhlabayo ezinqabeni zalo; njalo libe yindawo yokuhlala yemigobho, umuzi wamadodakazi ezintshe.
14 Avumbwe adzakumana ndi afisi, ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana. Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa ndi kupeza malo opumulirako.
Izilo zenkangala lazo zizahlangana lezilo ezihlaba umkhulungwane, legogo lizakhalela umngane walo; lesikhova esikhalayo sizaphumula khona, sizitholele indawo yokuphumula.
15 Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira, adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake; akamtema adzasonkhananso kumeneko, awiriawiri.
Lapho isikhova esikhulu sizakwakha isidleke, sibekele, sichamisele, sifukamele ngaphansi komthunzi waso; amanqe lawo azabuthana lapho, yilelo lalelo lomngane walo.
16 Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga: mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa; sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake. Pakuti Yehova walamula kuti zitero, ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
Dingani egwalweni lweNkosi, lifunde; kakukho lokukodwa kwalokhu okuzasilela, kakukho okuzaswela umngane wakho; ngoba umlomo wami ngokwawo ulayile, lomoya wayo ngokwawo ukubuthanisile.
17 Yehova wagawa dziko lawo; wapatsa chilichonse chigawo chake. Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.
Ngoba yona ibenzele inkatho yokuphosa, lesandla sayo sibehlukanisele ngentambo; lizakuba yilifa labo kuze kube phakade, kusukela kusizukulwana kuze kube sesizukulwaneni bazahlala kulo.

< Yesaya 34 >