< Yesaya 34 >

1 Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve: tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse: Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
Approchez, nations, et écoutez; peuples, soyez attentifs: que la terre écoute, ainsi que sa plénitude, le globe et tout ce qu’il produit.
2 Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse; wapsera mtima magulu awo onse ankhondo. Iye adzawawononga kotheratu, nawapereka kuti aphedwe.
Parce que l’indignation du Seigneur est sur toutes les nations, et sa fureur sur leur milice entière; il les a tués et les a livrés au carnage.
3 Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja, mitembo yawo idzawola ndi kununkha; mapiri adzafiira ndi magazi awo.
Ceux qui leur ont été tués seront jetés dehors, et de leurs cadavres s’élèvera une odeur fétide, et des montagnes se liquéfieront par leur sang.
4 Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala; nyenyezi zonse zidzayoyoka ngati masamba ofota a mphesa, ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.
Et toute la milice des cieux se liquéfiera; et les cieux se rouleront comme un livre; et toute leur milice tombera comme tombe une feuille d’une vigne et d’un figuier.
5 Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba; taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu, anthu amene ndawawononga kotheratu.”
Parce que mon glaive s’est enivré de sang dans le ciel; voici qu’il descendra sur l’Idumée, et sur un peuple que j’ai voué à la mort, pour le juger.
6 Lupanga la Yehova lakhuta magazi, lakutidwa ndi mafuta; magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi, mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna. Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
Le glaive du Seigneur est plein de sang, il est couvert de graisse; du sang des agneaux et des boucs, du sang des béliers les plus gras; car il y a une victime du Seigneur à Bosra, et un grand carnage dans la terre d’Edom.
7 Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati, ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe. Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha, ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.
Et des licornes descendront avec eux, et des taureaux avec les puissants d’entre eux: leur terre sera enivrée de sang, et leur sol de la graisse des gras;
8 Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira ndi kulanga adani a Ziyoni.
Parce que c’est le jour de la vengeance du Seigneur, l’année des rétributions dans le jugement de Sion.
9 Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula, ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule; dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
Et ses torrents seront convertis en poix, et son sol en soufre, et sa terre deviendra une poix brûlante.
10 Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana; utsi wake udzafuka kosalekeza. Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado; palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
Ni nuit ni jour le feu ne s’éteindra, à jamais s’élèvera sa fumée; de génération en génération elle sera désolée; dans les siècles des siècles personne n’y passera.
11 Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu; amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo. Mulungu adzatambalitsa pa Edomu chingwe choyezera cha chisokonezo ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
Et l’onocrotale et le hérisson la posséderont; l’ibis et le corbeau y habiteront; et le cordeau sera étendu sur elle, afin qu’elle soit réduite au néant, et le niveau pour sa ruine.
12 Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko; akalonga ake onse adzachotsedwa.
Ses nobles ne seront pas là; ils invoqueront un roi, et tous ses princes seront anéantis.
13 Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa, khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake. Ankhandwe azidzadya mʼmenemo; malo okhalamo akadzidzi.
Et les épines et les orties croîtront dans ses maisons, et le paliure dans ses forteresses; et elle sera le repaire des dragons et le pâturage des autruches.
14 Avumbwe adzakumana ndi afisi, ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana. Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa ndi kupeza malo opumulirako.
Les démons y rencontreront les onocentaures, et le bouc criera, l’un à l’autre; là s’est couchée la lamie, et elle y a trouvé son repos.
15 Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira, adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake; akamtema adzasonkhananso kumeneko, awiriawiri.
Le hérisson a eu une tanière, et a nourri ses petits, et il a creusé tout autour, et il les a réchauffés sous son ombre; là se sont assemblés les milans, l’un près de l’autre.
16 Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga: mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa; sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake. Pakuti Yehova walamula kuti zitero, ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
Recherchez dans le livre du Seigneur, et lisez; une seule de ces choses n’a pas manqué; l’un n’a pas cherché l’autre; parce que ce qui procède de ma bouche, c’est lui qui l’a commandé, et que son esprit lui-même a rassemblé ces choses.
17 Yehova wagawa dziko lawo; wapatsa chilichonse chigawo chake. Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.
Et lui-même a jeté pour eux le sort, et sa main a divisé leur part au cordeau; jusqu’à l’éternité ils la posséderont, et dans toutes les générations ils y habiteront.

< Yesaya 34 >