< Yesaya 34 >

1 Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve: tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse: Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
Neiye, ye hethene men, and here; and ye puplis, perseyue; the erthe, and the fulnesse therof, the world, and al buriownyng therof, here ye.
2 Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse; wapsera mtima magulu awo onse ankhondo. Iye adzawawononga kotheratu, nawapereka kuti aphedwe.
For whi indignacioun of the Lord is on alle folkis, and strong veniaunce on al the chyualrie of hem; he killide hem, and yaf hem in to sleyng.
3 Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja, mitembo yawo idzawola ndi kununkha; mapiri adzafiira ndi magazi awo.
The slayn men of hem schulen be cast forth, and stynk schal stie of the careyns of hem; hillis schulen flete of the blood of hem.
4 Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala; nyenyezi zonse zidzayoyoka ngati masamba ofota a mphesa, ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.
And al the chyualrie of heuenys schal faile, and heuenys schulen be foldid togidere as a book, and al the knyythod of tho schal flete doun, as the leef of a vyner and of a fige tre fallith doun.
5 Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba; taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu, anthu amene ndawawononga kotheratu.”
For my swerd is fillid in heuene; lo! it schal come doun on Ydumee, and on the puple of my sleyng, to doom.
6 Lupanga la Yehova lakhuta magazi, lakutidwa ndi mafuta; magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi, mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna. Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
The swerd of the Lord is fillid of blood, it is maad fat of the ynner fatnesse of the blood of lambren and of buckis of geet, of the blood of rammes ful of merow; for whi the slayn sacrifice of the Lord is in Bosra, and greet sleyng is in the lond of Edom.
7 Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati, ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe. Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha, ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.
And vnycornes schulen go doun with hem, and bolis with hem that ben myyti; the lond of hem schal be fillid with blood, and the erthe of hem with ynnere fatnesse of fatte beestis;
8 Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira ndi kulanga adani a Ziyoni.
for it is a dai of veniaunce of the Lord, a yeer of yeldyng of the dom of Sion.
9 Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula, ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule; dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
And the strondis therof schulen be turned in to pitche, and the erthe therof in to brymstoon; and the lond therof schal be in to brennyng pitch, niyt and dai.
10 Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana; utsi wake udzafuka kosalekeza. Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado; palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
It schal not be quenchid withouten ende, the smoke therof schal stie fro generacioun in to generacioun, and it schal be desolat in to worldis of worldis; noon schal passe therbi.
11 Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu; amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo. Mulungu adzatambalitsa pa Edomu chingwe choyezera cha chisokonezo ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
And onocrotalus, and an irchoun schulen welde it; and a capret, and a crowe schulen dwelle therynne; and a mesure schal be stretchid forth theronne, that it be dryuun to nouyt, and an hangynge plomet in to desolacyoun.
12 Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko; akalonga ake onse adzachotsedwa.
The noble men therof schulen not be there; rathere thei schulen clepe the kyng in to help, and alle the princes therof schulen be in to nouyt.
13 Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa, khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake. Ankhandwe azidzadya mʼmenemo; malo okhalamo akadzidzi.
And thornes and nettlis schulen growe in the housis therof, and a tasil in the strengthis therof; and it schal be the couche of dragouns, and the lesewe of ostrichis.
14 Avumbwe adzakumana ndi afisi, ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana. Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa ndi kupeza malo opumulirako.
And fendis, and wondurful beestis, lijk men in the hiyere part and lijk assis in the nethir part, and an heeri schulen meete; oon schal crie to an other.
15 Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira, adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake; akamtema adzasonkhananso kumeneko, awiriawiri.
Lamya schal ligge there, and foond rest there to hir silf; there an irchoun hadde dichis, and nurschide out whelpis, and diggide aboute, and fostride in the schadewe therof; there kitis weren gaderid togidere, oon to another.
16 Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga: mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa; sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake. Pakuti Yehova walamula kuti zitero, ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
Seke ye diligentli in the book of the Lord, and rede ye; oon of tho thingis failide not, oon souyte not another; for he comaundide that thing, that goith forth of my mouth, and his spirit he gaderide tho togidere.
17 Yehova wagawa dziko lawo; wapatsa chilichonse chigawo chake. Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.
And he sente to hem eritage, and his hond departide it in mesure; til in to withouten ende tho schulen welde that lond, in generacioun and in to generacioun tho schulen dwelle ther ynne.

< Yesaya 34 >