< Yesaya 34 >
1 Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve: tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse: Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
Come near, ye nations, to hear; and ye people, hearken: let the earth hear, and all that filleth it; the world, and all things that spring forth of it.
2 Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse; wapsera mtima magulu awo onse ankhondo. Iye adzawawononga kotheratu, nawapereka kuti aphedwe.
For the indignation of the Lord is [enkindled] over all the nations, and his fury over all their army: he hath devoted them, he hath given them up to the slaughter:
3 Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja, mitembo yawo idzawola ndi kununkha; mapiri adzafiira ndi magazi awo.
And their slain also shall be cast out, and as regardeth their carcasses their stench shall ascend upward, and the mountains shall be melted through their blood.
4 Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala; nyenyezi zonse zidzayoyoka ngati masamba ofota a mphesa, ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.
And all the host of heaven shall be dissolved, and the heavens shall be rolled together like a book: and all their host shall wither, as the leaf withereth from the vine, and as withering fruit from the fig-tree.
5 Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba; taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu, anthu amene ndawawononga kotheratu.”
For my sword is sated in heaven: behold, it shall come down upon Edom, and upon the people I have devoted to punishment.
6 Lupanga la Yehova lakhuta magazi, lakutidwa ndi mafuta; magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi, mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna. Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
The sword of the Lord is full of blood, it is enriched with fat, with the blood of lambs and goats, with the fat of the kidneys of rams; for the Lord hath a sacrifice in Bozrah, and a great slaughter in the land of Edom.
7 Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati, ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe. Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha, ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.
And wild oxen shall sink down with them, and steers with bullocks; and their land shall be sated with blood, and their dust enriched with fat.
8 Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira ndi kulanga adani a Ziyoni.
For it is the day of vengeance unto the Lord, and the year of recompense for the controversy of Zion.
9 Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula, ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule; dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
And its brooks shall be changed into pitch, and its dust into sulfur, and its land shall become burning pitch.
10 Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana; utsi wake udzafuka kosalekeza. Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado; palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
Night and day shall it not be quenched; for ever shall ascend the smoke thereof: from generation to generation shall it lie waste; no one shall for ever and ever pass through it.
11 Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu; amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo. Mulungu adzatambalitsa pa Edomu chingwe choyezera cha chisokonezo ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
But pelican and hedgehog shall take possession of it; night-owl also and raven shall dwell in it: and he shall stretch out over it the line of destruction, and the weights of desolation.
12 Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko; akalonga ake onse adzachotsedwa.
Their nobles—no one is there they could call [to] the kingdom, and all its princes shall be no more.
13 Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa, khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake. Ankhandwe azidzadya mʼmenemo; malo okhalamo akadzidzi.
And thorns shall spring up in its palaces, nettles and brambles in its fortresses: and it shall be a habitation of monsters, and a court for ostriches.
14 Avumbwe adzakumana ndi afisi, ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana. Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa ndi kupeza malo opumulirako.
And the martens shall meet with the jackals, and one goat shall call to his fellow; only the screech-owl shall rest there, and find for herself a place of repose.
15 Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira, adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake; akamtema adzasonkhananso kumeneko, awiriawiri.
There shall nestle the arrow-snake, and lay eggs, and hatch, and gather its young under its shadow: only vultures shall assemble there, every one with her mate.
16 Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga: mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa; sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake. Pakuti Yehova walamula kuti zitero, ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
Inquire out of the book of the Lord, and read: not one of these shall be absent, not one shall miss her mate; for my mouth it is that hath ordained it, and its breath it is that hath gathered them.
17 Yehova wagawa dziko lawo; wapatsa chilichonse chigawo chake. Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.
And he hath cast the lot for them, and his hand hath divided it out unto them by the measuring line: for ever shall they possess it, from generation to generation shall they dwell therein.