< Yesaya 34 >

1 Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve: tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse: Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!
Namtom rhoek loh hnatun hamla ha mop lah. Namtu rhoek loh hnatung uh saeh lamtah diklai neh lunglai boeih neh a cadil cahma rhoek boeih loh yaa saeh.
2 Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse; wapsera mtima magulu awo onse ankhondo. Iye adzawawononga kotheratu, nawapereka kuti aphedwe.
BOEIPA kah a thinhul te namtom boeih taengah, a kosi te amih kah caempuei boeih taengla pawk. Amih te a thup vetih maeh la a voeih ni.
3 Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja, mitembo yawo idzawola ndi kununkha; mapiri adzafiira ndi magazi awo.
Amih a ngawn te a voeih vaengah a rhok kah a bothae te rhim ni. Amih thii loh tlang a yut sak ni.
4 Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala; nyenyezi zonse zidzayoyoka ngati masamba ofota a mphesa, ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.
Vaan dong caempuei boeih te muei vetih vaan cabu bangla kolong uh ni. Amih kah caempuei boeih te misur hnah a hoo bangla, thaibu a hoo bangla hoo ni.
5 Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba; taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu, anthu amene ndawawononga kotheratu.”
Ka cunghang loh vaan ah hmilhmal tih Edom a cuk thil. Pilnam te kamah kah yaehtaboeih loh laitloeknah neh a pha coeng.
6 Lupanga la Yehova lakhuta magazi, lakutidwa ndi mafuta; magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi, mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna. Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.
BOEIPA kah cunghang tah a thii hah coeng. Bozrah kah BOEIPA hmueih neh Edom khohmuen kah maeh len kongah maehtha neh, tuca thii neh, kikong neh tutal kuel kah a tha loh a men sak.
7 Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati, ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe. Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha, ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.
Cung neh vaito lueng khaw amih taengla suntla ni. Te vaengah a khohmuen te thii neh hmilhmal vetih a laipi khaw maehtha bangla men ni.
8 Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira ndi kulanga adani a Ziyoni.
BOEIPA taengah phulohnah khohnin neh, Zion kah tuituknah te a sah kum khaw om.
9 Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula, ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule; dziko lake lidzasanduka phula lamoto!
A soklong te kunhnai la, a laipi te kat la poeh ni. A khohmuen te kunhnai rhawm la poeh ni.
10 Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana; utsi wake udzafuka kosalekeza. Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado; palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.
Khoyin khothaih kumhal duela thi mahpawh. A khu khaw cadilcahma lamkah cadilcahma patoeng taengla cet ni. A yoeyah kah a yoeyah la khap uh vetih te long te paan uh voel mahpawh.
11 Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu; amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo. Mulungu adzatambalitsa pa Edomu chingwe choyezera cha chisokonezo ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.
Khosoek saelbu, kharhoeng neh saelbu loh a pang vetih vangak loh kho a sak thil ni. Rhilam te hinghong la, lungto he a hong la a toe uh.
12 Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko; akalonga ake onse adzachotsedwa.
A hlangcoelh rhoek khaw a ram ah hah a khueh uh vetih a mangpa rhoek khaw a honghi la boeih om ni.
13 Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa, khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake. Ankhandwe azidzadya mʼmenemo; malo okhalamo akadzidzi.
A impuei te dohui hling loh, a hmuencak te mutlo hling loh a yam thil ni. Te vaengah pongui kah tolkhoeng la, tuirhuk vanu kah a bu la poeh ni.
14 Avumbwe adzakumana ndi afisi, ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana. Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa ndi kupeza malo opumulirako.
Te vaengah kohong neh sa-ui hum vetih maae loh a hui a khue ni. Vathae khaw pahoi paa vetih amah ham ngolbuel a hmuh ni.
15 Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira, adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake; akamtema adzasonkhananso kumeneko, awiriawiri.
Te ah valah loh bu a tuk vetih oi ni. A khae phoeiah tah a hlipkhup ah a ku thil ni. Te ah te valae rhoek khaw tingtun uh vetih a la te a paa cu ni.
16 Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga: mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa; sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake. Pakuti Yehova walamula kuti zitero, ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.
BOEIPA kah cabu dongah cae uh lamtah tae uh lah. Amih kah pakhat khaw hmaai mahpawh. A la pakhat khaw a paa vawt uh mahpawh. Ka ka loh a uen coeng dongah amih te BOEIPA kah a mueihla loh a coi ni.
17 Yehova wagawa dziko lawo; wapatsa chilichonse chigawo chake. Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.
Amah loh amih ham hmulung a nan pah. A kut loh amih ham rhilam a suem pah te kumhal duela a pang uh ni. Cadilcahma phoeikah cadilcahma loh a khuiah kho a sak uh ni.

< Yesaya 34 >