< Yesaya 33 >

1 Tsoka kwa iwe, iwe wowonongawe, amene sunawonongedwepo! Tsoka kwa iwe, iwe mthirakuwiri, iwe amene sunanyengedwepo! Iwe ukadzaleka kuwononga, udzawonongedwa, ukadzasiya umʼthirakuwiri, adzakuwononga, ndipo ukadzaleka kuchita zachinyengo adzakunyenga.
Вай де тине, пустииторуле, каре тотушь н-ай фост пустиит, каре жефуешть, ши н-ай фост жефуит ынкэ! Дупэ че вей сфырши де пустиит, вей фи пустиит ши ту, дупэ че вей испрэви де жефуит, вей фи жефуит ши ту.
2 Inu Yehova, mutikomere mtima ife; tikulakalaka Inu. Tsiku ndi tsiku mutitchinjirize ndi mkono wanu, ndipo mutipulumutse pa nthawi ya masautso.
Доамне, ай милэ де ной! Ной нэдэждуим ын Тине. Фий ажуторул ностру ын фиекаре диминяцэ ши избэвиря ноастрэ ла време де невое!
3 Mukatulutsa liwu lanu longa bingu mitundu ya anthu imathawa; pamene Inu mwadzambatuka mitundu ya anthu imabalalika.
Кынд рэсунэ гласул Тэу, попоареле фуг; кынд Те сколь Ту, нямуриле се ымпрэштие.
4 Zofunkha za ku nkhondo za mitundu ina Aisraeli adzazisonkhanitsa ngati mmene limachitira dzombe. Iwo adzalumphira zofunkhazo monga mmene limachitira dzombe.
Ши прада воастрэ ва фи стрынсэ кум стрынӂе мушица; сар песте еа кум сар лэкустеле.
5 Yehova wakwezeka kwambiri pakuti amakhala pamwamba pa zonse adzadzaza Ziyoni ndi chilungamo ndi chipulumutso.
Домнул есте ынэлцат ши локуеште ын ынэлциме. Ел умпле Сионул де непэртинире ши дрептате.
6 Iye adzakupatsani mtendere pa nthawi yanu, adzakupatsani chipulumutso chochuluka, nzeru zambiri ndi chidziwitso chochuluka; kuopa Yehova ngati madalitso.
Зилеле тале сунт статорниче, ынцелепчуня ши причеперя сунт ун извор де мынтуире; фрика де Домнул, ятэ комоара Сионулуй.
7 Taonani, anthu awo amphamvu akulira mofuwula mʼmisewu; akazembe okhazikitsa mtendere akulira kwambiri.
Ятэ, витежий стригэ афарэ, солий пэчий плынг ку амар.
8 Mʼmisewu yayikulu mulibe anthu, mʼmisewu mulibe anthu a paulendo. Mdaniyo ndi wosasunga pangano. Iye amanyoza mboni. Palibe kulemekezana.
Друмуриле сунт пустий; нимень ну май умблэ пе друмурь. Асур а рупт легэмынтул, диспрецуеште четэциле, ну се уйтэ ла нимень.
9 Dziko likulira ndipo likunka likutha. Nkhalango ya Lebanoni ikuchita manyazi, yafota. Chigwa cha chonde cha Saroni chasanduka chachidalala. Masamba a mitengo ya ku Basani ndi Karimeli akuyoyoka.
Цара желеште ши есте ынтристатэ; Либанул есте плин де рушине, тынжеште; Саронул есте ка ун пустиу; Басанул ши Кармелул ышь скутурэ фрунза.
10 Yehova akunena kuti, “Tsopano ndidzadzambatuka ndipo ndidzaonetsa mphamvu zanga, ndipo ndidzakwezedwa.
„Акум Мэ вой скула”, зиче Домнул, „акум Мэ вой ынэлца, акум Мэ вой ридика.
11 Zolingalira zanu nʼzachabechabe ngati udzu wamanyowa. Mpweya wamoto udzakupserezani.
Аць зэмислит фын ши наштець пае де мириште; суфларя воастрэ де мыние ымпотрива Иерусалимулуй есте ун фок каре пе вой ыншивэ вэ ва арде де тот.
12 Anthu a mitundu ina adzatenthedwa ngati miyala ya njereza; ndi ngati minga yodulidwa.”
Попоареле вор фи ка ниште куптоаре де вар, ка ниште спинь тэяць каре ард ын фок.
13 Inu amene muli kutali, imvani zimene ndachita; inu amene muli pafupi, dziwani mphamvu zanga
Вой, чей де департе, аскултаць че ам фэкут! Ши вой, чей де апроапе, ведець путеря Мя!”
14 Mu mzinda wa Ziyoni anthu ochimwa agwidwa ndi mantha; anthu osapembedza Mulungu akunjenjemera: Iwo akunena kuti, “Ndani wa ife angathe kukhala mʼmoto wonyeketsa? Ndani wa ife angathe kukhala moto wosatha?”
Пэкэтоший сунт ынгрозиць ын Сион, ун тремур а апукат пе чей нелеӂюиць, каре зик: „Чине дин ной ва путя сэ рэмынэ лынгэ ун фок мистуитор? Чине дин ной ва путя сэ рэмынэ лынгэ ниште флэкэрь вешниче?”
15 Angathe kuti ndi amene amachita zolungama ndi kuyankhula zoona, amene amakana phindu lolipeza monyenga ndipo salola manja ake kulandira ziphuphu, amene amatseka makutu ake kuti angamve mawu opangana kupha anzawo ndipo amatsinzina kuti angaone zoyipa.
Чел че умблэ ын неприхэнире ши ворбеште фэрэ виклешуг, чел че несокотеште ун кыштиг скос прин стоарчере, чел че ышь траӂе мыниле ынапой ка сэ ну примяскэ митэ, чел че ышь аступэ урекя сэ н-аудэ кувинте сетоасе де сынӂе ши ышь лягэ окий ка сэ ну вадэ рэул,
16 Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja, kothawira kwake kudzakhala mʼmalinga a mʼmapiri. Azidzalandira chakudya chake ndipo madzi sadzamusowa.
ачела ва локуи ын локуриле ыналте; стынчь ынтэрите вор фи локул луй де скэпаре; и се ва да пыне, ши апа ну-й ва липси.
17 Nthawi imeneyo maso a ana adzaona mfumu ya maonekedwe wokongola ndi kuona dziko lotambasukira kutali.
Окий тэй вор ведя пе Ымпэрат ын стрэлучиря Луй, вор приви цара ын тоатэ ынтиндеря ей.
18 Mu mtima mwanu muzidzalingalira zoopsa zinachitika kale zija: “Ali kuti mkulu wa Asilikali uja? Ali kuti wokhometsa misonkho uja? Ali kuti mkulu woyangʼanira nsanja?”
Инима та ышь ва адуче аминте де гроаза трекутэ ши ва зиче: „Унде есте логофэтул? Унде есте вистиерникул? Унде есте чел че вегя асупра турнурилор?”
19 Simudzawaonanso anthu odzikuza aja, anthu aja achiyankhulo chosadziwika, chachilendo ndi chosamveka.
Атунч ну вей май ведя пе попорул ачела ындрэзнец, пе попорул ку ворбиря ынкылчитэ де н-о путяй ынцелеӂе, ку лимба гынгавэ де н-о путяй причепе.
20 Taonani Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zachipembedzo chathu; maso anu adzaona Yerusalemu, mzinda wamtendere, tenti imene sidzachotsedwa, zikhomo zake sizidzazulidwa, kapena zingwe zake kuduka.
Привеште Сионул, четатя сэрбэторилор ноастре! Окий тэй вор ведя Иерусалимул ка локуинцэ лиништитэ, ка ун корт каре ну ва май фи мутат, ай кэруй цэрушь ну вор май фи скошь ничодатэ ши але кэруй фуний ну вор май фи дезлегате.
21 Kumeneko Yehova adzaonetsa ulemerero wake ndipo mzindawo udzakhala kasupe wa mitsinje yayikulu. Ngalawa za zopalasa sizidzapitamo, sitima zapamadzi zikuluzikulu sizidzayendamo.
Да, аколо ку адевэрат Домнул есте минунат пентру ной: Ел не цине лок де рыурь, де пырае лате, унде тотушь ну пэтрунд корэбий ку лопець ши ну трече ничун вас путерник.
22 Pakuti Yehova ndi woweruza wathu, Yehova ndiye wotilamulira, Yehova ndiye mfumu yathu; ndipo ndiye amene adzatipulumutse.
Кэч Домнул есте Жудекэторул ностру, Домнул есте Леӂюиторул ностру, Домнул есте Ымпэратул ностру: Ел не мынтуеште!
23 Zingwe za sitima zapamadzi za adani athu zamasuka, sizikutha kulimbitsa mlongoti wake, matanga ake sakutheka kutambasuka. Ngakhale tidzagawana zofunkha zochuluka kwambiri ndipo ngakhale olumala adzatenga zofunkhazo.
Фунииле тале с-ау слэбит, аша кэ ну май пот стрынӂе пичорул катаргулуй ши ну май пот ынтинде пынзеле. Атунч се ымпарте прада, каре-й аша де маре, кэ пынэ ши олоӂий яу парте ла еа.
24 Palibe ndi mmodzi yemwe wokhala mʼZiyoni adzanene kuti, “Ndikudwala” ndipo anthu onse okhala mʼmenemo machimo awo adzakhululukidwa.
Ничун локуитор ну зиче: „Сунт болнав!” Попорул Иерусалимулуй капэтэ ертаря фэрэделеӂилор луй.

< Yesaya 33 >