< Yesaya 33 >
1 Tsoka kwa iwe, iwe wowonongawe, amene sunawonongedwepo! Tsoka kwa iwe, iwe mthirakuwiri, iwe amene sunanyengedwepo! Iwe ukadzaleka kuwononga, udzawonongedwa, ukadzasiya umʼthirakuwiri, adzakuwononga, ndipo ukadzaleka kuchita zachinyengo adzakunyenga.
Wo to thee, that robbest; whether and thou schalt not be robbid? and that dispisist, whether and thou schalt not be dispisid? Whanne thou hast endid robbyng, thou schalt be robbid; and whanne thou maad weri ceessist to dispise, thou schalt be dispisid.
2 Inu Yehova, mutikomere mtima ife; tikulakalaka Inu. Tsiku ndi tsiku mutitchinjirize ndi mkono wanu, ndipo mutipulumutse pa nthawi ya masautso.
Lord, haue thou merci on vs, for we abiden thee; be thou oure arm in the morewtid, and oure helthe in the tyme of tribulacioun.
3 Mukatulutsa liwu lanu longa bingu mitundu ya anthu imathawa; pamene Inu mwadzambatuka mitundu ya anthu imabalalika.
Puplis fledden fro the vois of the aungel; hethene men ben scaterid of thin enhaunsyng.
4 Zofunkha za ku nkhondo za mitundu ina Aisraeli adzazisonkhanitsa ngati mmene limachitira dzombe. Iwo adzalumphira zofunkhazo monga mmene limachitira dzombe.
And youre spuylis schulen be gaderid togidere, as a bruke is gaderid togidere, as whanne dichis ben ful therof.
5 Yehova wakwezeka kwambiri pakuti amakhala pamwamba pa zonse adzadzaza Ziyoni ndi chilungamo ndi chipulumutso.
The Lord is magnefied, for he dwellide an hiy, he fillid Sion with doom and riytfulnesse.
6 Iye adzakupatsani mtendere pa nthawi yanu, adzakupatsani chipulumutso chochuluka, nzeru zambiri ndi chidziwitso chochuluka; kuopa Yehova ngati madalitso.
And feith schal be in thi tymes; the ritchessis of helthe is wisdom and kunnynge; the drede of the Lord, thilke is the tresour of hym.
7 Taonani, anthu awo amphamvu akulira mofuwula mʼmisewu; akazembe okhazikitsa mtendere akulira kwambiri.
Lo! seeris withoutenforth schulen crye, aungels of pees schulen wepe bittirli.
8 Mʼmisewu yayikulu mulibe anthu, mʼmisewu mulibe anthu a paulendo. Mdaniyo ndi wosasunga pangano. Iye amanyoza mboni. Palibe kulemekezana.
Weies ben distried, a goere bi the path ceesside; the couenaunt is maad voide, he castide doun citees, he arettide not men.
9 Dziko likulira ndipo likunka likutha. Nkhalango ya Lebanoni ikuchita manyazi, yafota. Chigwa cha chonde cha Saroni chasanduka chachidalala. Masamba a mitengo ya ku Basani ndi Karimeli akuyoyoka.
The lond morenyde, and was sijk; the Liban was schent, and was foul; and Saron is maad as desert, and Basan is schakun, and Carmele.
10 Yehova akunena kuti, “Tsopano ndidzadzambatuka ndipo ndidzaonetsa mphamvu zanga, ndipo ndidzakwezedwa.
Now Y schal ryse, seith the Lord, now I schal be enhaunsid, and now I schal be reisid vp.
11 Zolingalira zanu nʼzachabechabe ngati udzu wamanyowa. Mpweya wamoto udzakupserezani.
Ye schulen conseyue heete, ye schulen brynge forth stobil; youre spirit as fier schal deuoure you.
12 Anthu a mitundu ina adzatenthedwa ngati miyala ya njereza; ndi ngati minga yodulidwa.”
And puplis schulen be as aischis of the brennyng; thornes gaderid togidere schulen be brent in fier.
13 Inu amene muli kutali, imvani zimene ndachita; inu amene muli pafupi, dziwani mphamvu zanga
Ye that ben fer, here what thingis Y haue do; and, ye neiyboris, knowe my strengthe.
14 Mu mzinda wa Ziyoni anthu ochimwa agwidwa ndi mantha; anthu osapembedza Mulungu akunjenjemera: Iwo akunena kuti, “Ndani wa ife angathe kukhala mʼmoto wonyeketsa? Ndani wa ife angathe kukhala moto wosatha?”
Synneris ben al to-brokun in Syon, tremblyng weldide ipocritis; who of you mai dwelle with fier deuowringe? who of you schal dwelle with euerlastinge brennyngis?
15 Angathe kuti ndi amene amachita zolungama ndi kuyankhula zoona, amene amakana phindu lolipeza monyenga ndipo salola manja ake kulandira ziphuphu, amene amatseka makutu ake kuti angamve mawu opangana kupha anzawo ndipo amatsinzina kuti angaone zoyipa.
He that goith in riytfulnessis, and spekith treuthe; he that castith awei aueryce of fals calenge, and schakith awei his hondis fro al yifte; he that stoppith his eeris, that he heere not blood, and closith his iyen, that he se not yuel.
16 Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja, kothawira kwake kudzakhala mʼmalinga a mʼmapiri. Azidzalandira chakudya chake ndipo madzi sadzamusowa.
This man schal dwelle in hiy thingis, the strengthis of stoonys ben the hiynesse of hym; breed is youun to hym, hise watris ben feithful.
17 Nthawi imeneyo maso a ana adzaona mfumu ya maonekedwe wokongola ndi kuona dziko lotambasukira kutali.
Thei schulen se the kyng in his fairnesse; the iyen of hym schulen biholde the londe fro fer.
18 Mu mtima mwanu muzidzalingalira zoopsa zinachitika kale zija: “Ali kuti mkulu wa Asilikali uja? Ali kuti wokhometsa misonkho uja? Ali kuti mkulu woyangʼanira nsanja?”
Eliachym, thin herte schal bithenke drede; where is the lettrid man? Where is he that weieth the wordis of the lawe? where is the techere of litle children?
19 Simudzawaonanso anthu odzikuza aja, anthu aja achiyankhulo chosadziwika, chachilendo ndi chosamveka.
Thou schalt not se a puple vnwijs, a puple of hiy word, so that thou maist not vndurstonde the fair speking of his tunge, in which puple is no wisdom.
20 Taonani Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zachipembedzo chathu; maso anu adzaona Yerusalemu, mzinda wamtendere, tenti imene sidzachotsedwa, zikhomo zake sizidzazulidwa, kapena zingwe zake kuduka.
Biholde thou Sion, the citee of youre solempnyte; thin iyen schulen se Jerusalem, a riche citee, a tabernacle that mai not be borun ouer, nether the nailis therof schulen be takun awei withouten ende; and alle the cordis therof schulen not be brokun.
21 Kumeneko Yehova adzaonetsa ulemerero wake ndipo mzindawo udzakhala kasupe wa mitsinje yayikulu. Ngalawa za zopalasa sizidzapitamo, sitima zapamadzi zikuluzikulu sizidzayendamo.
For oneli the worschipful doere oure Lord God is there; the place of floodis is strondis ful large and opyn; the schip of roweris schal not entre bi it, nethir a greet schip schal passe ouer it.
22 Pakuti Yehova ndi woweruza wathu, Yehova ndiye wotilamulira, Yehova ndiye mfumu yathu; ndipo ndiye amene adzatipulumutse.
For whi the Lord is oure iuge, the Lord is oure lawe yyuere, the Lord is oure kyng; he schal saue vs.
23 Zingwe za sitima zapamadzi za adani athu zamasuka, sizikutha kulimbitsa mlongoti wake, matanga ake sakutheka kutambasuka. Ngakhale tidzagawana zofunkha zochuluka kwambiri ndipo ngakhale olumala adzatenga zofunkhazo.
Thi roopis ben slakid, but tho schulen not auaile; thi mast schal be so, that thou mow not alarge a signe. Thanne the spuylis of many preyes schulen be departid, crokid men schulen rauysche raueyn.
24 Palibe ndi mmodzi yemwe wokhala mʼZiyoni adzanene kuti, “Ndikudwala” ndipo anthu onse okhala mʼmenemo machimo awo adzakhululukidwa.
And a neiybore schal seie, Y was not sijk; the puple that dwellith in that Jerusalem, wickidnesse schal be takun awei fro it.