< Yesaya 33 >

1 Tsoka kwa iwe, iwe wowonongawe, amene sunawonongedwepo! Tsoka kwa iwe, iwe mthirakuwiri, iwe amene sunanyengedwepo! Iwe ukadzaleka kuwononga, udzawonongedwa, ukadzasiya umʼthirakuwiri, adzakuwononga, ndipo ukadzaleka kuchita zachinyengo adzakunyenga.
Unune malit un joma osetieko ji, to pok otieku! Unune malit un joma osendhogo ji, to un pok ondhogu! Ka uweyo tieko ji to notieku; bende ka uweyo ndhogo ji to nondhogu.
2 Inu Yehova, mutikomere mtima ife; tikulakalaka Inu. Tsiku ndi tsiku mutitchinjirize ndi mkono wanu, ndipo mutipulumutse pa nthawi ya masautso.
Yaye Jehova Nyasaye, yie ikechwa; nimar chunywa dwari. Miwae teko okinyi ka okinyi, kendo bednwa kar resruok, e kinde mag chandruok.
3 Mukatulutsa liwu lanu longa bingu mitundu ya anthu imathawa; pamene Inu mwadzambatuka mitundu ya anthu imabalalika.
Ka dwondi omor to ji ringo; ka ia malo to ogendini ke.
4 Zofunkha za ku nkhondo za mitundu ina Aisraeli adzazisonkhanitsa ngati mmene limachitira dzombe. Iwo adzalumphira zofunkhazo monga mmene limachitira dzombe.
Yaye un ogendini, mwandu noyaki mana ka kama nyithi bonyo omonjo; kendo ji noyak mwandugi, mana kaka bonyo monjo piny.
5 Yehova wakwezeka kwambiri pakuti amakhala pamwamba pa zonse adzadzaza Ziyoni ndi chilungamo ndi chipulumutso.
Nying Jehova Nyasaye otingʼ malo, nimar odak e polo; obiro pongʼo Sayun gi tim makare kod adiera.
6 Iye adzakupatsani mtendere pa nthawi yanu, adzakupatsani chipulumutso chochuluka, nzeru zambiri ndi chidziwitso chochuluka; kuopa Yehova ngati madalitso.
Enobed mise mar adier e ndalou, kar mwandu mar resruok gi rieko kod ngʼeyo; luoro Jehova Nyasaye e rayaw mar mwanduni.
7 Taonani, anthu awo amphamvu akulira mofuwula mʼmisewu; akazembe okhazikitsa mtendere akulira kwambiri.
To neuru kaka thuondige ywak malit e wangʼ yore; joote ma oseor mondo odwar kwe ywak malit.
8 Mʼmisewu yayikulu mulibe anthu, mʼmisewu mulibe anthu a paulendo. Mdaniyo ndi wosasunga pangano. Iye amanyoza mboni. Palibe kulemekezana.
Yore osedongʼ nono, kendo onge jowuoth e yo. Winjruok osekethi mi joma nobedo joneno ok dew, kendo onge ngʼama omi luor.
9 Dziko likulira ndipo likunka likutha. Nkhalango ya Lebanoni ikuchita manyazi, yafota. Chigwa cha chonde cha Saroni chasanduka chachidalala. Masamba a mitengo ya ku Basani ndi Karimeli akuyoyoka.
Piny ywak kendo dok chien, Lebanon ni e wichkuot kendo okethore, Sharon olokore ongoro ka Araba, kendo Bashan gi Karmel oyaki modongʼ nono.
10 Yehova akunena kuti, “Tsopano ndidzadzambatuka ndipo ndidzaonetsa mphamvu zanga, ndipo ndidzakwezedwa.
Jehova Nyasaye wacho niya, “Koro abiro aa malo, mondo anyisu duongʼna gi tekona.
11 Zolingalira zanu nʼzachabechabe ngati udzu wamanyowa. Mpweya wamoto udzakupserezani.
Ubiro mako ich to unywolo yamo; muya muyweyo en mach ma tiekou.
12 Anthu a mitundu ina adzatenthedwa ngati miyala ya njereza; ndi ngati minga yodulidwa.”
Ogendini nowangʼ, mi lokre pidhe mag buru, kendo mana kaka kudho mobet e bungu enowangʼ gi mach!”
13 Inu amene muli kutali, imvani zimene ndachita; inu amene muli pafupi, dziwani mphamvu zanga
Un mudak mabor, winjuru gima asetimo, un mudak machiegni ngʼeuru tekona!
14 Mu mzinda wa Ziyoni anthu ochimwa agwidwa ndi mantha; anthu osapembedza Mulungu akunjenjemera: Iwo akunena kuti, “Ndani wa ife angathe kukhala mʼmoto wonyeketsa? Ndani wa ife angathe kukhala moto wosatha?”
Joricho man Sayun, kihondko osemako; kibaji ogoyo joma okia nyasaye, mi gisepenjore kendgi niya, “En ngʼa kuomwa manyalo dak kod mach mawengʼo magerni? Koso en ngʼa kuomwa manyalo dak kod mach maliel maonge gikone?”
15 Angathe kuti ndi amene amachita zolungama ndi kuyankhula zoona, amene amakana phindu lolipeza monyenga ndipo salola manja ake kulandira ziphuphu, amene amatseka makutu ake kuti angamve mawu opangana kupha anzawo ndipo amatsinzina kuti angaone zoyipa.
Ngʼatno mawuotho e ratiro kendo wacho gima adiera, ma tamore yudo ohala e yor mecho kendo ok oyie kawo asoya, ngʼatno ma ok chik ite e chenro mar neko, kendo odino wengene e neno timbe mamono,
16 Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja, kothawira kwake kudzakhala mʼmalinga a mʼmapiri. Azidzalandira chakudya chake ndipo madzi sadzamusowa.
ma e ngʼama nodagi kuonde motingʼore gi malo, ma kare mar pondo nobedi got mochiel gohinga motegno. Chiembe ibiro chiw, kendo pi ok nodwon-ne.
17 Nthawi imeneyo maso a ana adzaona mfumu ya maonekedwe wokongola ndi kuona dziko lotambasukira kutali.
Wengeni biro neno ruoth kober kendo iningʼi piny molandore malach.
18 Mu mtima mwanu muzidzalingalira zoopsa zinachitika kale zija: “Ali kuti mkulu wa Asilikali uja? Ali kuti wokhometsa misonkho uja? Ali kuti mkulu woyangʼanira nsanja?”
E pachi inipar masiche machon: “Ere jatelo maduongʼ cha? Ere ngʼatno mane okawo osuru? Ere jatelo mochungʼne kuonde ngʼicho man malo?”
19 Simudzawaonanso anthu odzikuza aja, anthu aja achiyankhulo chosadziwika, chachilendo ndi chosamveka.
Ok inichak ine jonjorego kendo, jogo ma wechegi oyombore, kendo mawacho dhok matek winjo.
20 Taonani Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zachipembedzo chathu; maso anu adzaona Yerusalemu, mzinda wamtendere, tenti imene sidzachotsedwa, zikhomo zake sizidzazulidwa, kapena zingwe zake kuduka.
Ka irango Sayun, dala maduongʼ mar sewniwa moyier; ibiro neno Jerusalem kama kwe nitie, hema ma ok bi muki; loje mage ok nopudhi, kata tondene ok nochodi.
21 Kumeneko Yehova adzaonetsa ulemerero wake ndipo mzindawo udzakhala kasupe wa mitsinje yayikulu. Ngalawa za zopalasa sizidzapitamo, sitima zapamadzi zikuluzikulu sizidzayendamo.
Kanyo Jehova Nyasaye biro bedonwa Jal Maratego. Kanyo nochalnwa ka aore kod mago matindo. Yiedhi man-gi tanga ok nokwangʼ kanyo, meli maduongʼ ok nokwangʼ e aore.
22 Pakuti Yehova ndi woweruza wathu, Yehova ndiye wotilamulira, Yehova ndiye mfumu yathu; ndipo ndiye amene adzatipulumutse.
Nimar Jehova Nyasaye e jangʼadnwa bura, Jehova Nyasaye e jaketonwa chik, kendo Jehova Nyasaye e ruodhwa; en ema obiro resowa.
23 Zingwe za sitima zapamadzi za adani athu zamasuka, sizikutha kulimbitsa mlongoti wake, matanga ake sakutheka kutambasuka. Ngakhale tidzagawana zofunkha zochuluka kwambiri ndipo ngakhale olumala adzatenga zofunkhazo.
Tondegi mag meli obwodhore: Tanga ok otwe motegno, ok ginyal kwangʼ maber. Eka gik moyaki ibiro pogi kendo kata mana joma rongʼonde noyud pok.
24 Palibe ndi mmodzi yemwe wokhala mʼZiyoni adzanene kuti, “Ndikudwala” ndipo anthu onse okhala mʼmenemo machimo awo adzakhululukidwa.
Onge ngʼama odak Sayun manowachi niya, “Atuo,” kendo richo mag joma odak kanyo nowenegi.

< Yesaya 33 >