< Yesaya 33 >
1 Tsoka kwa iwe, iwe wowonongawe, amene sunawonongedwepo! Tsoka kwa iwe, iwe mthirakuwiri, iwe amene sunanyengedwepo! Iwe ukadzaleka kuwononga, udzawonongedwa, ukadzasiya umʼthirakuwiri, adzakuwononga, ndipo ukadzaleka kuchita zachinyengo adzakunyenga.
Alaot ka, tiglaglag nga wala pa gayod malaglag! Alaot ang maluibon nga wala gayod luibi! Sa paghunong mo na sa pagpanglaglag, pagalaglagon ka usab. Sa paghunong mo sa pagpangluib, luiban ka nila.
2 Inu Yehova, mutikomere mtima ife; tikulakalaka Inu. Tsiku ndi tsiku mutitchinjirize ndi mkono wanu, ndipo mutipulumutse pa nthawi ya masautso.
Yahweh, kaluy-i kami; mohulat kami kanimo; himoa nga ikaw ang among bukton sa matag buntag, among kaluwasan panahon sa kalisod.
3 Mukatulutsa liwu lanu longa bingu mitundu ya anthu imathawa; pamene Inu mwadzambatuka mitundu ya anthu imabalalika.
Mokalagiw ang katawhan sa makusog nga dahunog; sa imong pag-abot, magkatibulaag ang kanasoran.
4 Zofunkha za ku nkhondo za mitundu ina Aisraeli adzazisonkhanitsa ngati mmene limachitira dzombe. Iwo adzalumphira zofunkhazo monga mmene limachitira dzombe.
Ang imong kalugmok gitigom sama sa pagtigom sa mga dulon; sama nga manglukso ang mga dulon, manglukso usab ang mga kalalakin-an niini.
5 Yehova wakwezeka kwambiri pakuti amakhala pamwamba pa zonse adzadzaza Ziyoni ndi chilungamo ndi chipulumutso.
Bayawon si Yahweh. Nagpuyo siya sa kinatas-an nga dapit. Pun-on niya ang Zion sa hustisya ug pagkamatarong.
6 Iye adzakupatsani mtendere pa nthawi yanu, adzakupatsani chipulumutso chochuluka, nzeru zambiri ndi chidziwitso chochuluka; kuopa Yehova ngati madalitso.
Siya ang kasaligan sa inyong kapanahonan, madagayaon sa kaluwasan, kaalam, ug kahibalo; ang pagkahadlok kang Yahweh mao ang iyang bahandi.
7 Taonani, anthu awo amphamvu akulira mofuwula mʼmisewu; akazembe okhazikitsa mtendere akulira kwambiri.
Tan-awa, nanghilak diha sa kadalanan ang mga gipadala nila; midangoyngoy pag-ayo ang mga gipadala nga naglaom ug kalinaw.
8 Mʼmisewu yayikulu mulibe anthu, mʼmisewu mulibe anthu a paulendo. Mdaniyo ndi wosasunga pangano. Iye amanyoza mboni. Palibe kulemekezana.
Gibiyaan ang mga kadalanan; wala na gayoy magpapanaw. Naguba ang mga kasabotan, gitamay ang mga saksi, ug wala na tahora ang mga katawhan.
9 Dziko likulira ndipo likunka likutha. Nkhalango ya Lebanoni ikuchita manyazi, yafota. Chigwa cha chonde cha Saroni chasanduka chachidalala. Masamba a mitengo ya ku Basani ndi Karimeli akuyoyoka.
Nagbangotan ang yuta ug nalawos kini; naulaw ang Lebanon ug nalawos kini; nahisama ang Sharon sa patag nga kamingawan; ug giuyog sa Bashan ug sa Carmel ang ilang mga dahon.
10 Yehova akunena kuti, “Tsopano ndidzadzambatuka ndipo ndidzaonetsa mphamvu zanga, ndipo ndidzakwezedwa.
Miingon si Yahweh, “karon motindog na ako”; “Karon pagabayawon na ako; karon ipataas na ako.
11 Zolingalira zanu nʼzachabechabe ngati udzu wamanyowa. Mpweya wamoto udzakupserezani.
Nanamkon ka ug tahop, ug nagpahimugso ug dagami; ang imong gininhawa sama sa kalayo nga molamoy kanimo.
12 Anthu a mitundu ina adzatenthedwa ngati miyala ya njereza; ndi ngati minga yodulidwa.”
Mangasunog ang katawhan hangtod mahimong apog, sama sa mga sampinit nga gipamutol ug gisunog.
13 Inu amene muli kutali, imvani zimene ndachita; inu amene muli pafupi, dziwani mphamvu zanga
Kamo nga anaa sa layo, paminawa kung unsa ang akong nabuhat; ug, kamo nga ania sa duol, ilha ang akong gahom.”
14 Mu mzinda wa Ziyoni anthu ochimwa agwidwa ndi mantha; anthu osapembedza Mulungu akunjenjemera: Iwo akunena kuti, “Ndani wa ife angathe kukhala mʼmoto wonyeketsa? Ndani wa ife angathe kukhala moto wosatha?”
Nangahadlok ang mga makakasala sa Zion; ang pagkurog maoy nagdakop sa mga dili diosnon. Kinsa man kanato ang mopanaw uban ang walay kataposang nagdilaab nga kalayo?
15 Angathe kuti ndi amene amachita zolungama ndi kuyankhula zoona, amene amakana phindu lolipeza monyenga ndipo salola manja ake kulandira ziphuphu, amene amatseka makutu ake kuti angamve mawu opangana kupha anzawo ndipo amatsinzina kuti angaone zoyipa.
Siya nga naglakaw sa pagkamatarong ug nagsulti nga matinud-anon; siya nga nagtamay sa ginansiya sa pagpangdaugdaog, siya nga nagdumili sa pagkuha sa suborno, siya nga wala naglaraw sa pagpatay, ug wala motan-aw sa daotan—
16 Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja, kothawira kwake kudzakhala mʼmalinga a mʼmapiri. Azidzalandira chakudya chake ndipo madzi sadzamusowa.
himoon niya ang iyang balay sa hataas nga dapit; ang dapit nga iyang salipdanan mahimong mga kota nga mga bato; dili siya makabsan ug pagkaon ug tubig.
17 Nthawi imeneyo maso a ana adzaona mfumu ya maonekedwe wokongola ndi kuona dziko lotambasukira kutali.
Makita ninyo ang kaanyag sa hari; ilang pagasud-ongon ang halapad nga yuta.
18 Mu mtima mwanu muzidzalingalira zoopsa zinachitika kale zija: “Ali kuti mkulu wa Asilikali uja? Ali kuti wokhometsa misonkho uja? Ali kuti mkulu woyangʼanira nsanja?”
Mahinumdoman sa imong kasingkasing ang kalisang; hain na man ang manunulat, hain na man kadtong tigdumala sa salapi? Hain na man kadtong nag-ihap sa tore?
19 Simudzawaonanso anthu odzikuza aja, anthu aja achiyankhulo chosadziwika, chachilendo ndi chosamveka.
Dili na gayod ninyo makita ang mga masinupakong tawo, ang katawhan nga lahi ang pinulongan, nga dili ninyo masabtan.
20 Taonani Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zachipembedzo chathu; maso anu adzaona Yerusalemu, mzinda wamtendere, tenti imene sidzachotsedwa, zikhomo zake sizidzazulidwa, kapena zingwe zake kuduka.
Tan-awa ang Zion, ang siyudad sa atong mga kasaulogan; makita ninyo ang Jerusalem ingon nga malinawong pinuy-anan, ang tolda nga dili mabalhin, kansang mga ugsok dili gayod maibot ug kansang mga higot dili mabugto.
21 Kumeneko Yehova adzaonetsa ulemerero wake ndipo mzindawo udzakhala kasupe wa mitsinje yayikulu. Ngalawa za zopalasa sizidzapitamo, sitima zapamadzi zikuluzikulu sizidzayendamo.
Hinuon, mag-uban kanato si Yahweh diha sa pagkahalangdon, nga anaa sa lapad nga mga suba ug mga sapa. Walay sakayan nga panggubat nga adunay pangbugsay ang moagi niini, ug walay dakong sakayan nga molawig.
22 Pakuti Yehova ndi woweruza wathu, Yehova ndiye wotilamulira, Yehova ndiye mfumu yathu; ndipo ndiye amene adzatipulumutse.
Tungod kay si Yahweh ang atong maghuhukom, si Yahweh ang atong tighatag ug balaod, si Yahweh ang atong hari; luwason niya kita.
23 Zingwe za sitima zapamadzi za adani athu zamasuka, sizikutha kulimbitsa mlongoti wake, matanga ake sakutheka kutambasuka. Ngakhale tidzagawana zofunkha zochuluka kwambiri ndipo ngakhale olumala adzatenga zofunkhazo.
Ang inyong banting dili hugot; dili gayod nila makuptan ang poste nga anaa sa tunga sa sakayan; dili nila mabukhad ang layag; sa dihang bahinon ang dakong inilog, bisan ang bakol maguyod sa inilog.
24 Palibe ndi mmodzi yemwe wokhala mʼZiyoni adzanene kuti, “Ndikudwala” ndipo anthu onse okhala mʼmenemo machimo awo adzakhululukidwa.
Dili moingon ang mga lumolupyo, “Nagsakit ako;” ang katawhan nga namuyo didto pasayloon sa ilang kasal-anan.