< Yesaya 33 >

1 Tsoka kwa iwe, iwe wowonongawe, amene sunawonongedwepo! Tsoka kwa iwe, iwe mthirakuwiri, iwe amene sunanyengedwepo! Iwe ukadzaleka kuwononga, udzawonongedwa, ukadzasiya umʼthirakuwiri, adzakuwononga, ndipo ukadzaleka kuchita zachinyengo adzakunyenga.
Горко на тебе, който разоряваш, а не си бил разорен, Който постъпваш коварно; а с тебе на се постъпили коварно! Когато престанеш да разоряваш ще бъдеш разорен, И когато спреш да постъпваш коварно, ще постъпват коварно с тебе.
2 Inu Yehova, mutikomere mtima ife; tikulakalaka Inu. Tsiku ndi tsiku mutitchinjirize ndi mkono wanu, ndipo mutipulumutse pa nthawi ya masautso.
Господи, смили се за нас; Тебе чакаме; Бъди ни мишца всяка заран, И избавление за нас в усилно време.
3 Mukatulutsa liwu lanu longa bingu mitundu ya anthu imathawa; pamene Inu mwadzambatuka mitundu ya anthu imabalalika.
От шума на метежа племената побягнаха; От Твоето издигане народите се разпръснаха.
4 Zofunkha za ku nkhondo za mitundu ina Aisraeli adzazisonkhanitsa ngati mmene limachitira dzombe. Iwo adzalumphira zofunkhazo monga mmene limachitira dzombe.
И користта ще се събере от вас както гъсениците събират; Ще скокнат върху нея, както скача скакалец
5 Yehova wakwezeka kwambiri pakuti amakhala pamwamba pa zonse adzadzaza Ziyoni ndi chilungamo ndi chipulumutso.
Господ е превъзвишен, защото обитава на високо; Той е изпълнил Сион с правосъдие и правда.
6 Iye adzakupatsani mtendere pa nthawi yanu, adzakupatsani chipulumutso chochuluka, nzeru zambiri ndi chidziwitso chochuluka; kuopa Yehova ngati madalitso.
А чрез мъдрост и знание и изобилно спасение Ще бъдат утвърдени времената ти: Страхът от Господа е Неговото съкровище.
7 Taonani, anthu awo amphamvu akulira mofuwula mʼmisewu; akazembe okhazikitsa mtendere akulira kwambiri.
Ето, юнаците им викат навън; Посланиците на мира плачат горчиво
8 Mʼmisewu yayikulu mulibe anthu, mʼmisewu mulibe anthu a paulendo. Mdaniyo ndi wosasunga pangano. Iye amanyoza mboni. Palibe kulemekezana.
Друмовете запустяха; Няма вече пътници; Той наруши договора, презря градовете, Не счита човека за нищо.
9 Dziko likulira ndipo likunka likutha. Nkhalango ya Lebanoni ikuchita manyazi, yafota. Chigwa cha chonde cha Saroni chasanduka chachidalala. Masamba a mitengo ya ku Basani ndi Karimeli akuyoyoka.
Земята жалее и изнемощява; Ливан е посрамен и вехне; Сарон прилича на пустиня; Листата на Васан и Кармил окапаха.
10 Yehova akunena kuti, “Tsopano ndidzadzambatuka ndipo ndidzaonetsa mphamvu zanga, ndipo ndidzakwezedwa.
Сега ще стана, казва Господ; Сега ще се възвиша, сега ще се възвелича.
11 Zolingalira zanu nʼzachabechabe ngati udzu wamanyowa. Mpweya wamoto udzakupserezani.
Слама ще заченете, и плява ще родите; Дишането ви като огън ще ви пояде,
12 Anthu a mitundu ina adzatenthedwa ngati miyala ya njereza; ndi ngati minga yodulidwa.”
И племената ще бъдат вар що гори, Като отсечени тръни, които изгарят в огън.
13 Inu amene muli kutali, imvani zimene ndachita; inu amene muli pafupi, dziwani mphamvu zanga
Слушайте, вие далечни, що съм сторил; И вие близки признайте силата Ми.
14 Mu mzinda wa Ziyoni anthu ochimwa agwidwa ndi mantha; anthu osapembedza Mulungu akunjenjemera: Iwo akunena kuti, “Ndani wa ife angathe kukhala mʼmoto wonyeketsa? Ndani wa ife angathe kukhala moto wosatha?”
Грешните в Сион се боят; Трепет обзема безбожните; и казват: Кой от вас ще обитава при поглъщащ огън? Кой от вас ще обитава при вечни пламъци?
15 Angathe kuti ndi amene amachita zolungama ndi kuyankhula zoona, amene amakana phindu lolipeza monyenga ndipo salola manja ake kulandira ziphuphu, amene amatseka makutu ake kuti angamve mawu opangana kupha anzawo ndipo amatsinzina kuti angaone zoyipa.
Който ходи праведно и говори справедливо, Който презира печалбата от насилствата, Който отърсва ръцете си от дароприемство, Който запушва ушите си, за да не чуе за кръвопролитие, И който затуля очите си, за да не види злото,
16 Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja, kothawira kwake kudzakhala mʼmalinga a mʼmapiri. Azidzalandira chakudya chake ndipo madzi sadzamusowa.
Той ще обитава на високо; крепостите на канарите ще бъдат мястото на защитата му; Хлябът му ще му се даде, водата му няма да липсва.
17 Nthawi imeneyo maso a ana adzaona mfumu ya maonekedwe wokongola ndi kuona dziko lotambasukira kutali.
Очите ти ще видят царя в красотата му, Ще видят широкоразпространена земя.
18 Mu mtima mwanu muzidzalingalira zoopsa zinachitika kale zija: “Ali kuti mkulu wa Asilikali uja? Ali kuti wokhometsa misonkho uja? Ali kuti mkulu woyangʼanira nsanja?”
Сърцето ти ще си спомня за миналия ужас, казвайки: Где е този, който броеше кулите?
19 Simudzawaonanso anthu odzikuza aja, anthu aja achiyankhulo chosadziwika, chachilendo ndi chosamveka.
Няма вече да видиш свирепите люде, Люде с дълбок глас, който не проумяваш, С чужд език, който не разбираш.
20 Taonani Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zachipembedzo chathu; maso anu adzaona Yerusalemu, mzinda wamtendere, tenti imene sidzachotsedwa, zikhomo zake sizidzazulidwa, kapena zingwe zake kuduka.
Погледни на Сион, града на празниците ни; Очите ти ще видят Ерусалим безмълвно заселище, Щатър, който няма да се мести, Чиито колове никога не ще бъдат извадени, И нито едно от въжетата му скъсано.
21 Kumeneko Yehova adzaonetsa ulemerero wake ndipo mzindawo udzakhala kasupe wa mitsinje yayikulu. Ngalawa za zopalasa sizidzapitamo, sitima zapamadzi zikuluzikulu sizidzayendamo.
Но там Господ ще бъде с нас във величието Си, Като място на широки реки и потоци, Гдето няма да върви ладия с весла, Нито ще мине великолепен кораб.
22 Pakuti Yehova ndi woweruza wathu, Yehova ndiye wotilamulira, Yehova ndiye mfumu yathu; ndipo ndiye amene adzatipulumutse.
Защото Господ е наш съдия, Господ е наш законодател, Господ е наш цар, Той ще ни спаси.
23 Zingwe za sitima zapamadzi za adani athu zamasuka, sizikutha kulimbitsa mlongoti wake, matanga ake sakutheka kutambasuka. Ngakhale tidzagawana zofunkha zochuluka kwambiri ndipo ngakhale olumala adzatenga zofunkhazo.
Въжетата ти ослабнаха, Не можеха да крепят мачтата ти, Не можеха да разпрострат платната; И тогава големи користи се разделиха, Хромите разграбиха плячката.
24 Palibe ndi mmodzi yemwe wokhala mʼZiyoni adzanene kuti, “Ndikudwala” ndipo anthu onse okhala mʼmenemo machimo awo adzakhululukidwa.
И жителят няма да рече: Болен съм; На людете, които живеят в него, ще се прости беззаконието им.

< Yesaya 33 >