< Yesaya 32 >

1 Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo, ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
Mana, ⱨǝⱪⱪaniyliⱪ bilǝn ⱨɵkümranliⱪ ⱪilƣuqi bir padixaⱨ qiⱪidu; Əmirlǝr bolsa toƣra ⱨɵküm qiⱪirip idarǝ ⱪilidu.
2 Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe, adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu, ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
Ⱨǝm xamalƣa dalda bolƣudǝk, Boranƣa panaⱨ bolƣudǝk, Ⱪaƣjiraⱪ jayƣa eriⱪ-sulardǝk, Qangⱪap kǝtkǝn zeminƣa ⱪoram taxning sayisidǝk bolƣan bir adǝm qiⱪidu.
3 Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka, ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
Xuning bilǝn kɵrgüqilǝrning kɵzliri ⱨeq torlaxmaydu, Anglaydiƣanlarning ⱪuliⱪi eniⱪ tingxaydu;
4 Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa, ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
Bǝngbaxning kɵngli bilimni tonup yetidu, Kekǝqning tili tez ⱨǝm eniⱪ sɵzlǝydu.
5 Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
Pǝsǝndilǝr ǝmdi pǝzilǝtlik dǝp atalmaydu, Piⱪsiⱪ iplaslar ǝmdi mǝrd dǝp atalmaydu,
6 Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru, amaganiza kuchita zoyipa: Iye amachita zoyipira Mulungu, ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova; anjala sawapatsa chakudya ndipo aludzu sawapatsa madzi.
Qünki pǝsǝndǝ adǝm pǝslikni sɵzlǝydu, Uning kɵngli buzuⱪqiliⱪ tǝyyarlaydu, Iplasliⱪ ⱪilixⱪa, Pǝrwǝrdigarƣa daƣ kǝltürüxkǝ, Aqlarning ⱪorsiⱪini aq ⱪalduruxⱪa, Qangⱪiƣanlarning iqimlikini yoⱪitiwetixkǝ niyǝtlinidu.
7 Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso, iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa. Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
Bǝrⱨǝⱪ, iplas adǝmning tǝdbirliri ⱪǝbiⱨtur; U ⱪǝstlǝrni pǝmlǝp olturidu, Mɵminlǝrni yalƣan gǝp bilǝn, Yoⱪsulning dǝwasida gǝp ⱪilip uni wǝyran ⱪilixni pǝmlǝp olturidu.
8 Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino, Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
Pǝzilǝtlik adǝmning ⱪilƣan niyǝtliri bǝrⱨǝⱪ pǝzilǝtliktur; U pǝzilǝttǝ muⱪim turidu.
9 Khalani maso, inu akazi amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji ndipo imvani mawu anga. Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
Ornunglardin turup, i hatirjǝm ayallar, awazimni anglanglar! I ǝndixisiz ⱪizlar, sɵzlirimgǝ ⱪulaⱪ selinglar!
10 Pakapita chaka ndi masiku pangʼono inu akazi amatama mudzanjenjemera; chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika ndipo zipatso sizidzaoneka.
Bir yil ɵtǝ-ɵtmǝyla, i biƣǝm ayallar, Parakǝndǝ ⱪilinisilǝr! Qünki üzüm ⱨosuli bikarƣa ketidu, Mewǝ yiƣix yoⱪ bolidu.
11 Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu; ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu. Vulani zovala zanu, ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
I hatirjǝm ayallar, titrǝnglar! I ǝndixisiz ⱪizlar, patiparaⱪ bolunglar! Kiyiminglarni seliwetinglar, ɵzünglarni yalang ⱪilinglar, qatriⱪinglarƣa bɵz baƣlanglar!
12 Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde, ndi mphesa yawonongeka.
Güzǝl etiz-baƣlar üqün, Mewilik üzüm talliri üqün mǝydǝnglarƣa urup ⱨǝsrǝt qekinglar!
13 Mʼdziko la anthu anga mwamera minga ndi mkandankhuku. Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
Üstidǝ tikǝn-yantaⱪlar ɵsidiƣan ɵz hǝlⱪimning zemini üqün, Xad-huram ɵylǝr, warang-qurung ⱪilip oynaydiƣan bu xǝⱨǝr üqün ⱪayƣurunglar!
14 Nyumba yaufumu idzasiyidwa, mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu; malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya. Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
Qünki orda taxlinidu, Adǝmlǝr bilǝn liⱪ tolƣan xǝⱨǝr adǝmzatsiz bolidu, Istiⱨkam wǝ kɵzǝt munarliri uzun zamanƣiqǝ pǝⱪǝtla yawayi exǝklǝr zoⱪ alidiƣan, Ⱪoy padiliri ozuⱪlinidiƣan boz yǝrlǝr bolidu.
15 Yehova adzatipatsa mzimu wake, ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde, ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
Taki Roⱨ bizgǝ yuⱪiridin tɵkülgüqǝ, Dalalar mewilik baƣ-etizlar bolƣuqǝ, Mewilik baƣ-etizlar ormanzar dǝp ⱨesablanƣuqǝ xu peti bolidu.
16 Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
Xu qaƣda adalǝt dalani, Ⱨǝⱪⱪaniyliⱪ mewilik baƣ-etizlarni makan ⱪilidu.
17 Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo; zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
Ⱨǝⱪⱪaniyliⱪtin qiⱪidiƣini hatirjǝmlik bolidu, Hatirjǝmlikning nǝtijisi bolsa mǝnggügǝ bolidiƣan aram-tinqliⱪ wǝ aman-esǝnlik bolidu.
18 Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere, mʼnyumba zodalirika, ndi malo osatekeseka a mpumulo.
Xuning bilǝn mening hǝlⱪim hatirjǝm makanlarda, Ixǝnqlik turalƣularda wǝ tinq aramgaⱨlarda turidu.
19 Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
Orman kesilip yiⱪitilƣanda mɵldür yaƣsimu, Xǝⱨǝr pütünlǝy yǝr bilǝn yǝksan ⱪiliwetilsimu,
20 inutu mudzakhala odalitsika ndithu. Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse, ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.
Su boyida uruⱪ teriƣuqilar, Kala wǝ exǝklǝrni kǝng dalaƣa ⱪoyuwetidiƣanlar bǝhtliktur!

< Yesaya 32 >