< Yesaya 32 >

1 Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo, ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
Атунч ымпэратул ва ымпэрэци ку дрептате ши воевозий вор кырмуи ку непэртинире.
2 Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe, adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu, ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
Фиекаре ва фи ка ун адэпост ымпотрива вынтулуй ши ка ун лок де скэпаре ымпотрива фуртуний, ка ниште рыурь де апэ ынтр-ун лок ускат, ка умбра уней стынчь марь ынтр-ун пэмынт арс де сете.
3 Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka, ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
Окий челор че вэд ну вор май фи легаць ши урекиле челор че ауд вор луа аминте.
4 Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa, ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
Инима челор ушуратичь ва причепе ши ва ынцелеӂе ши лимба гынгавилор ва ворби юте ши деслушит.
5 Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
Небунул ну се ва май нуми алес ла суфлет, нич мишелул ну се ва май нуми ку инимэ ларгэ.
6 Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru, amaganiza kuchita zoyipa: Iye amachita zoyipira Mulungu, ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova; anjala sawapatsa chakudya ndipo aludzu sawapatsa madzi.
Кэч небунул спуне небуний ши инима луй гындеште рэу, ка сэ лукрезе ын кип нелеӂюит ши сэ спунэ неадевэрурь ымпотрива Домнулуй, ка сэ ласе лихнит суфлетул челуй флэмынд ши сэ я бэутура челуй ынсетат.
7 Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso, iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa. Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
Армеле мишелулуй сунт нимичитоаре; ел фаче планурь виновате ка сэ пярдэ пе чел ненорочит прин кувинте минчиноасе, кяр кынд причина сэракулуй есте дряптэ.
8 Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino, Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
Дар чел алес ла суфлет фаче планурь алесе ши стэруеште ын плануриле луй алесе.
9 Khalani maso, inu akazi amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji ndipo imvani mawu anga. Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
Фемей фэрэ грижэ, скулаци-вэ ши аскултаць гласул меу! Фийче непэсэтоаре, луаць аминте ла кувынтул меу!
10 Pakapita chaka ndi masiku pangʼono inu akazi amatama mudzanjenjemera; chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika ndipo zipatso sizidzaoneka.
Ынтр-ун ан ши кытева зиле, вець тремура, непэсэтоарелор, кэч се ва дуче кулесул виилор ши стрынӂеря поамелор ну ва май вени.
11 Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu; ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu. Vulani zovala zanu, ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
Ынгрозици-вэ, вой, челе фэрэ грижэ! Тремураць, непэсэтоарелор! Дезбрэкаци-вэ, дезголици-вэ ши ынчинӂеци-вэ коапселе ку хайне де жале!
12 Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde, ndi mphesa yawonongeka.
Батеци-вэ пептул, адукынду-вэ аминте де фрумусеця кымпиилор ши де родничия виилор.
13 Mʼdziko la anthu anga mwamera minga ndi mkandankhuku. Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
Пе пэмынтул попорулуй меу креск спинь ши мэрэчинь, кяр ши ын тоате каселе де плэчере але четэций челей веселе.
14 Nyumba yaufumu idzasiyidwa, mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu; malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya. Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
Каса ымпэрэтяскэ есте пэрэситэ, четатя гэлэӂиоасэ есте лэсатэ; дялул ши турнул вор служи пе вечие ка пештерь; мэгарий сэлбатичь се вор жука ын еле ши турмеле вор паште
15 Yehova adzatipatsa mzimu wake, ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde, ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
пынэ кынд се ва турна Духул де сус песте ной; атунч пустиул се ва префаче ын пэмынт ши пометул ва фи привит ка о пэдуре.
16 Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
Атунч непэртиниря ва локуи ын пустиу ши неприхэниря ышь ва авя локуинца ын помет.
17 Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo; zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
Лукраря неприхэнирий ва фи пачя; роаделе неприхэнирий: одихна ши лиништя пе вечие.
18 Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere, mʼnyumba zodalirika, ndi malo osatekeseka a mpumulo.
Попорул меу ва локуи ын локуинца пэчий, ын касе фэрэ грижэ ши ын адэпостурь лиништите.
19 Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
Дар пэдуря ва фи прэбушитэ суб гриндинэ, ши четатя, плекатэ адынк.
20 inutu mudzakhala odalitsika ndithu. Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse, ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.
Фериче де вой, каре семэнаць претутиндень де-а лунгул апелор ши каре даць друмул претутиндень боулуй ши мэгарулуй!

< Yesaya 32 >