< Yesaya 32 >
1 Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo, ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
Khangelani, inkosi izabusa ngokulunga lababusi bazabusa ngemfanelo.
2 Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe, adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu, ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
Umuntu ngamunye uzakuba njengesihonqo sokuvikela umoya, lesiphephelo sokucatshela isiphepho, njengezihotsha zamanzi enkangala njengomthunzi wedwala elikhulu elizweni elomileyo.
3 Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka, ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
Lapho-ke amehlo alabo ababonayo kawasayikuvaleka, lezindlebe zalabo abezwayo zizalalela.
4 Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa, ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
Ingqondo yowalazelayo izakwazi, iqedisise, ogagasayo ulimi lwakhe luzatshwaphuluka luzwakale kuhle.
5 Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
Isithutha kasisayikuthiwa ngumhlonitshwa, lesigangi kasiyikuhlonitshwa.
6 Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru, amaganiza kuchita zoyipa: Iye amachita zoyipira Mulungu, ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova; anjala sawapatsa chakudya ndipo aludzu sawapatsa madzi.
Ngoba isithutha sikhuluma ubuwula, ingqondo yaso isebenza ububi: Senza imisebenzi yenkohlakalo, siqambe amanga ngoThixo; abalambayo kasibaniki lutho, abomileyo sibancitsha amanzi okunatha.
7 Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso, iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa. Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
Izindlela zesigangi zimbi, senza amacebo amabi ukuba sichithe abayanga ngamanga, lanxa isikhalazo sabaswelayo siqotho.
8 Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino, Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
Kodwa umuntu ohloniphekayo wenza amacebo ahloniphekayo, njalo uma ngezenzo ezihloniphekayo.
9 Khalani maso, inu akazi amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji ndipo imvani mawu anga. Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
Lina besifazane elingakhathazeki ngalutho, vukani lilalele kimi; lina madodakazi elizizwa livikelekile, lalelani engikutshoyo!
10 Pakapita chaka ndi masiku pangʼono inu akazi amatama mudzanjenjemera; chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika ndipo zipatso sizidzaoneka.
Ngesikhatshana nje esedlula umnyaka lina elizizwa livikelekile lizathuthumela; ukuvunwa kwevini akuyikuphumelela, lokuvunwa kwezithelo akuyikuba khona.
11 Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu; ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu. Vulani zovala zanu, ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
Thuthumelani lina madodakazi azizwa evikelekile; qhaqhazelani lina madodakazi azizwa evikelekile! Khululani izigqoko zenu, lithandele inkalo zenu ngamasaka.
12 Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde, ndi mphesa yawonongeka.
Zitshayeni izifuba zenu ngenxa yamasimu amahle, langenxa yezivini ezithela izithelo,
13 Mʼdziko la anthu anga mwamera minga ndi mkandankhuku. Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
langenxa yelizwe labantu bami, ilizwe eligcwele ukhula lameva, yebo, lilelani zonke izindlu zenjabulo ledolobho lokuzitika lentokozo.
14 Nyumba yaufumu idzasiyidwa, mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu; malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya. Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
Inqaba enkulu izatshiswa, idolobho elilomsindo lizatshiywa; inqaba lomphotshongo wokulinda kuzakuba ngumhlabathi ongatheli lutho kokuphela, kube yintokozo yabobabhemi lamadlelo emihlambi,
15 Yehova adzatipatsa mzimu wake, ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde, ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
umoya uze uthelwe phezu kwethu uvela phezulu, inkangala ibe ngumhlaba ovundileyo, umhlaba ovundileyo ube njengenhlabathi.
16 Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
Ukwahlulela kuhle kukaThixo kuzakuba khona enkangala, ukulunga kube khona emhlabeni ovundileyo.
17 Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo; zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
Izithelo zokulunga zizakuba yikuthula; okufaneleyo kuzaletha ukuthula zwi lethemba kuze kube nininini.
18 Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere, mʼnyumba zodalirika, ndi malo osatekeseka a mpumulo.
Abantu bami bazahlala ezindaweni ezilokuthula, emakhaya avikelekileyo, ezindaweni zokuphumula ezingelahlupho.
19 Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
Lanxa isiqhotho sitshabalalisa ihlathi ledolobho lidilizwe laphela nya,
20 inutu mudzakhala odalitsika ndithu. Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse, ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.
yeka ukubusiswa elizakuba yikho, lihlanyela inhlanyelo yenu emaceleni ezifula zonke, njalo liyekela inkomo zenu labobabhemi benu ukuba kusabalale.