< Yesaya 32 >

1 Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo, ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
Sie len ac fah oasr sie tokosra su leumi mwet lal ke suwoswos, ac mwet kol fulat saya lun mutunfacl sac ac fah oru nununku suwohs.
2 Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe, adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu, ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
Kais sie selos ac fah oana sie acn in wikla liki eng upa ac paka. Elos ac fah oana infacl srisrik su sororror ke acn mwesis, oana lulin sie eot lulap in acn turangang.
3 Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka, ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
Mutun mwet su ku in liye fah tia ohkla, ac sren mwet su ku in lohng ac fah porongo.
4 Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa, ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
Elos ac tia sifil semuteng, ac elos ac orekma ke etauk, ac elos ac fahk kalem ma elos nunku uh.
5 Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
Wangin mwet ac nunku mu fal in akfulatyeyuk sie mwet lalfon, ku fahk mu sie mwet sesuwos el wo.
6 Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru, amaganiza kuchita zoyipa: Iye amachita zoyipira Mulungu, ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova; anjala sawapatsa chakudya ndipo aludzu sawapatsa madzi.
Sie mwet lalfon el kaskas lalfon, ac el nunkauk ma koluk elan oru. El kikiap lain LEUM GOD in ma el oru ac ma el fahk. El tia wi kite mwet masrinsral, ku sang ma nimen mwet malu.
7 Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso, iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa. Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
Sie mwet kutasrik el koluk ac el suk in oru ma koluk. El orek pwapa koluk in akkolukye mwet sukasrup ke kas kikiap, ac kosralosla liki suwohs lalos.
8 Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino, Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
A sie mwet suwohs el oru ma suwohs, ac el tu na ku ke ma pwaye.
9 Khalani maso, inu akazi amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji ndipo imvani mawu anga. Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
Kowos mutan su moulkin moul fisrasr, ac wangin mwe akfosrngaye kowos, porongo ma nga ac fahk uh.
10 Pakapita chaka ndi masiku pangʼono inu akazi amatama mudzanjenjemera; chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika ndipo zipatso sizidzaoneka.
Sahp kowos insewowo inge, tusruktu pacl se inge ke yac fahsru kowos ac fah sun ma upa, mweyen ac wangin grape kowos in kosrani.
11 Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu; ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu. Vulani zovala zanu, ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
Moul lowos finne fisrasr ac wangin mwe sensen, tusruktu inge kowos in sangeng ac rarrar! Sarukla nuknuk lowos ac kapriya infulwowos ke nuknuk yohk eoa.
12 Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde, ndi mphesa yawonongeka.
Puok iniwowos ke asor, mweyen ima wo fahko ac ima in grape kunanula.
13 Mʼdziko la anthu anga mwamera minga ndi mkandankhuku. Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
Inge kokul ac mah fakfuk kapak fin acn lun mwet luk. Tungi lohm nukewa ma mwet we uh tuh engan, oayapa ke siti se ma tuh arulana warongrong meet.
14 Nyumba yaufumu idzasiyidwa, mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu; malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya. Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
Finne inkul sel tokosra ac fah wanginla mwet we, ac siti fulat sac fah mwesisla. Lohm sin mwet, ac pot ku ma karinganulos ac fah sruala oan nwe tok. Donkey lemnak fah forfor we, ac sheep fah konauk acn in mongo lalos we.
15 Yehova adzatipatsa mzimu wake, ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde, ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
Tusruktu God El ac sifilpa okoama ngun lal nu facsr. Acn mwesisla ac fah folokyak wo fohk we, ac ima uh fah oswe fahko na wowo.
16 Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
Ma pwaye ac suwohs ac fah orek acn nukewa in facl se inge.
17 Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo; zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
Ke sripen mwet nukewa ac oru ma suwohs, ac fah oasr misla ac wangin mwe sensen nwe tok.
18 Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere, mʼnyumba zodalirika, ndi malo osatekeseka a mpumulo.
Mwet lun God fah tia enenu in fosrnga, ac lohm selos ac fah misla ac okak.
19 Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
(Tusruktu af yohk kosra ac fah kahki nu fin sak insak uh, ac siti uh ac kunausyukla.)
20 inutu mudzakhala odalitsika ndithu. Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse, ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.
Fuka lupan engan lun mwet nukewa ke yohk kof nu ke ima lalos, ac pus mah yen nukewa nun donkey ac cow uh.

< Yesaya 32 >