< Yesaya 32 >

1 Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo, ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
Voilà qu’un roi régnera alors pour la justice et que des princes gouverneront pour le droit.
2 Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe, adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu, ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
Ils seront tous comme un refuge contre le vent et un abri contre l’orage, comme des cours d’eau dans des lieux arides, comme l’ombre d’un rocher puissant sur un sol altéré.
3 Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka, ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
Ceux qui voient n’auront plus les yeux troubles, ceux qui entendent prêteront une oreille attentive.
4 Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa, ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
L’Intelligence des gens légers apprendra à connaître, et la langue des bègues s’exprimera avec facilité et clarté.
5 Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
L’Homme pervers ne sera plus qualifié de noble et le fourbe ne passera plus pour généreux.
6 Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru, amaganiza kuchita zoyipa: Iye amachita zoyipira Mulungu, ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova; anjala sawapatsa chakudya ndipo aludzu sawapatsa madzi.
Car l’homme pervers débite des propos pervers, son cœur machine l’iniquité, pour accomplir des actions scélérates, proférer contre Dieu des faussetés, pour faire languir d’inanition celui qui a faim et priver de breuvage celui qui a soif.
7 Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso, iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa. Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
Le fourbe, ses armes sont mauvaises; il trame des projets perfides, afin de perdre les pauvres par des paroles de mensonge et l’indigent qui réclame son droit.
8 Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino, Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
L’Homme généreux, lui, ne conçoit que des desseins généreux, et il persévère dans sa noblesse.
9 Khalani maso, inu akazi amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji ndipo imvani mawu anga. Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
Femmes paisibles, levez-vous, entendez ma voix; et vous, filles insouciantes, écoutez mon discours.
10 Pakapita chaka ndi masiku pangʼono inu akazi amatama mudzanjenjemera; chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika ndipo zipatso sizidzaoneka.
Dans un an et des jours, vous serez troublées, vous qui vivez en pleine quiétude; car c’en est fini des vendanges, et de récolte, il n’en viendra plus.
11 Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu; ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu. Vulani zovala zanu, ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
Prenez peur, femmes paisibles, tremblez, filles insouciantes; dépouillez vos vêtements, mettez-vous à nu, qu’un cilice couvre vos reins!
12 Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde, ndi mphesa yawonongeka.
On se frappe la poitrine en pleurant les champs magnifiques, les vignes fertiles!
13 Mʼdziko la anthu anga mwamera minga ndi mkandankhuku. Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
Sur le sol de mon peuple poussent les ronces et les épines: elles envahissent même les maisons de plaisance, la ville joyeuse.
14 Nyumba yaufumu idzasiyidwa, mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu; malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya. Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
Car les palais sont délaissés, la cité bruyante est dans l’abandon; tour et château-fort sont devenus en permanence des cavernes, la joie des onagres, un pâturage pour les troupeaux,
15 Yehova adzatipatsa mzimu wake, ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde, ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
jusqu’au jour où se répandra sur nous un esprit d’en haut, où le désert redeviendra un verger et le verger sera considéré comme une forêt touffue.
16 Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
Alors le droit élira domicile dans le désert, et la justice aura son siège dans les jardins plantureux.
17 Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo; zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
Et l’œuvre de la justice sera la paix, et le fruit de la droiture sera le calme et la sécurité à tout jamais.
18 Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere, mʼnyumba zodalirika, ndi malo osatekeseka a mpumulo.
Mon peuple habitera dans un séjour de paix, dans des demeures bien protégées et dans des retraites tranquilles.
19 Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
Mais une grêle violente s’abattra sur la forêt, et la ville sera profondément abaissée.
20 inutu mudzakhala odalitsika ndithu. Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse, ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.
Heureux cependant, ô vous qui pourrez semer au bord de tous les cours d’eaux et laisser circuler librement le bœuf et l’âne!

< Yesaya 32 >