< Yesaya 32 >

1 Taonani, kudzakhala mfumu ina imene idzalamulira mwachilungamo, ndipo akalonga ake adzaweruza molungama.
Behold, a king shall reign in righteousness, and princes shall rule in judgment.
2 Munthu aliyense adzakhala ngati pothawirapo mphepo ndi malo obisalirapo namondwe, adzakhala ngati mitsinje ya mʼchipululu, ngati mthunzi wa thanthwe lalikulu la mʼdziko lowuma.
And a man shall be as a hiding-place from the wind, and a covert from the tempest; as streams of water in a dry place, as the shade of a great rock in a weary land.
3 Ndipo maso a anthu openya sadzakhalanso otseka, ndipo makutu a anthu akumva adzamvetsetsa.
And the eyes of them that see shall not be dim, and the ears of them that hear shall hearken.
4 Anthu a mtima wopupuluma adzadziwa ndi kuchita zinthu mofatsa, ndipo anthu ovutika kuyankhula adzayankhula mosadodoma ndi momveka.
The heart also of the rash shall understand knowledge, and the tongue of the stammerers shall be ready to speak plainly.
5 Chitsiru sichidzatchedwanso munthu waulemu wake ndipo munthu woyipa sadzalemekezedwa.
The vile person shall be no more called liberal, nor the churl said [to be] bountiful.
6 Pakuti munthu opusa amayankhula zauchitsiru, amaganiza kuchita zoyipa: Iye amachita zoyipira Mulungu, ndipo amafalitsa zolakwika zokhudza Yehova; anjala sawapatsa chakudya ndipo aludzu sawapatsa madzi.
For the vile person will speak villainy, and his heart will work iniquity, to practice hypocrisy, and to utter error against the LORD, to make empty the soul of the hungry; and he will cause the drink of the thirsty to fail.
7 Munthu woyipa njira zake ndi zoyipanso, iye kwake nʼkulingalira zinthu zoyipa. Amalingalira zakuti awononge anthu aumphawi ndi mabodza ake ngakhale kuti waumphawiyo akuyankhula zoona.
The instruments also of the churl [are] evil: he deviseth wicked devices to destroy the poor with lying words, even when the needy speaketh right.
8 Koma munthu wolemekezeka amalingaliranso kuchita zinthu zabwino, Iye amakhazikika pa zinthu zabwinozo.
But the liberal deviseth liberal things; and by liberal things shall he stand.
9 Khalani maso, inu akazi amene mukungokhala wopanda kulingalira kuti kunja kulinji ndipo imvani mawu anga. Inu akazi odzitama, imvani zimene ndikunena!
Rise up, ye women that are at ease; hear my voice, ye careless daughters; give ear to my speech.
10 Pakapita chaka ndi masiku pangʼono inu akazi amatama mudzanjenjemera; chifukwa mitengo ya mphesa idzakanika ndipo zipatso sizidzaoneka.
Many days and years shall ye be troubled, ye careless women: for the vintage shall fail, the gathering shall not come.
11 Nthunthumirani inu okhala mosatekesekanu; ndipo njenjemerani, inu akazi omadzikhulupirira nokhanu. Vulani zovala zanu, ndipo valani ziguduli mʼchiwuno mwanu.
Tremble, ye women that are at ease; be troubled, ye careless ones: strip ye, and make you bare, and gird [sackcloth] upon [your] loins.
12 Dzigugudeni pachifuwa mwachisoni chifukwa minda yachonde, ndi mphesa yawonongeka.
They shall lament for the breasts, for the pleasant fields, for the fruitful vine.
13 Mʼdziko la anthu anga mwamera minga ndi mkandankhuku. Zoona, mulilire nyumba zonse zachikondwerero ndi mzinda uno umene unali wachisangalalo.
Upon the land of my people shall come up thorns [and] briers; also, upon all the houses of joy [in] the joyous city:
14 Nyumba yaufumu idzasiyidwa, mzinda waphokoso udzakhala wopanda anthu; malinga ndi nsanja zidzasanduka chipululu mpaka muyaya. Abulu adzasangalalamo ndipo ziweto zidzapezamo msipu.
Because the palaces shall be forsaken; the multitude of the city shall be left; the forts and towers shall be for dens for ever, a joy of wild asses, a pasture of flocks;
15 Yehova adzatipatsa mzimu wake, ndipo dziko lachipululu lidzasanduka munda wachonde, ndipo munda wachonde udzakhala ngati nkhalango.
Until the spirit shall be poured upon us from on high, and the wilderness shall be a fruitful field, and the fruitful field shall be counted for a forest.
16 Tsono mʼchipululu mudzakhala chiweruzo cholungama ndipo mʼminda yachonde mudzakhala chilungamo.
Then judgment shall dwell in the wilderness, and righteousness remain in the fruitful field.
17 Mtendere udzakhala chipatso chachilungamo; zotsatira za chilungamo zidzakhala bata ndi kudzidalira mpaka muyaya.
And the work of righteousness shall be peace; and the effect of righteousness, quietness and assurance for ever.
18 Anthu anga adzakhala mʼmidzi yamtendere, mʼnyumba zodalirika, ndi malo osatekeseka a mpumulo.
And my people shall dwell in a peaceable habitation, and in sure dwellings, and in quiet resting-places;
19 Ngakhale nkhalango idzawonongedwa ndi matalala ndipo mzinda udzagwetsedwa mpaka pansi,
When it shall hail, coming down on the forest; and the city shall be low in a low place.
20 inutu mudzakhala odalitsika ndithu. Mudzadzala mbewu zanu mʼmbali mwa mtsinje uliwonse, ndipo ngʼombe zanu ndi abulu anu zidzadya paliponse.
Blessed [are] ye that sow beside all waters, that send forth [thither] the feet of the ox and the ass.

< Yesaya 32 >