< Yesaya 31 >

1 Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo, amene amadalira akavalo, nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo, koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli, kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.
Горе тим, що в Єгипет по поміч ідуть, що на ко́ней спираються, і на колесни́ці надію свою́ покладають, — вони бо числе́нні! та на верхівці́в, — бо вони дуже сильні! але на Святого Ізраїлевого не дивляться, і до Господа не зверта́ються!
2 Komatu Yehovayo ndi wanzeru ndipo angathe kuwononga, ndipo sasintha chimene wanena. Adzalimbana ndi anthu ochita zoyipa, komanso ndi amene amathandiza anthu ochita zoyipa.
Та мудрий і Він, і спрова́дить лихе, і Своїх слів не відмінить, і піді́йметься Він проти дому безбожних, і проти помочі несправедливих.
3 Aigupto ndi anthu chabe osati Mulungu; akavalo awo ndi nyama chabe osati mizimu. Yehova akangotambasula dzanja lake, amene amapereka chithandizo adzapunthwa, amene amalandira chithandizocho adzagwa; onsewo adzathera limodzi.
А Єгипет — не Бог, а люди́на, а коні їхні — тіло, не дух: як простя́гне Господь Свою руку, то спіткне́ться пома́гач, впаде́ і підпома́ганий, — і ра́зом вони всі погинуть!
4 Zimene Yehova akunena kwa ine ndi izi: “Monga mkango kapena msona wamkango umabangula ukagwira nyama yake, ndipo suopsedwa kapena kusokonezeka ndi kufuwula kwa abusa amene akulimbana nayo, momwemonso palibe chingaletse Yehova Wamphamvuzonse kubwera kudzatchinjiriza phiri la Ziyoni ndi zitunda zake.
Бо до мене Господь сказав так: Як му́ркає лев чи левчу́к над своєю здоби́ччю, хоч покликана буде на нього юрба́ пастухів, він голосу їхнього не лякається, та не боїться їхнього крику, — так зі́йде Господь Саваот воюва́ти на Сіонській горі та на взгі́р'ї її!
5 Monga mbalame zowuluka pamwamba pa zisa zake, Yehova Wamphamvuzonse adzatchinjiriza Yerusalemu; ndi kumupulumutsa, iye adzawupitirira ndi kuwulanditsa.”
Як пта́хи летю́чі пташа́т, так Єрусалима Господь Саваот охоро́нить, охоро́нить літа́ючи, та збереже́, пощади́ть та врятує!
6 Inu Aisraeli, bwererani kwa Iye amene munamuwukira kwakukulu.
Верніться до Того, від Кого далеко відпа́ли, сино́ве Ізраїлеві!
7 Pakuti tsiku limenelo nonsenu mudzataya mafano anu a siliva ndi golide amene mumapanga ndi manja anu auchimo.
Бо дня того обри́дить собі чоловік божків срібних своїх та бовва́нів своїх золотих, що вам наробили на гріх руки ваші.
8 “Aasiriya adzaphedwa ku nkhondo ndi mphamvu osati za munthu. Lupanga, osati la munthu, lidzawawononga. Adzathawa ku nkhondo ndipo anyamata awo adzagwira ntchito yathangata.
І Ашшу́р упаде́ від меча не чоловіка, і його пожере́ меч не люди́ни; і він побіжить не перед мечем, і стануть його юнаки́ кріпака́ми.
9 Mfumu yawo idzamwalira ndi mantha, ndipo atsogoleri awo ankhondo adzathawa ndi mantha kusiya pambuyo mbendera yawo ya nkhondo.” Akutero Yehova, amene moto wake uli mu Ziyoni, ndipo ngʼanjo yake ili mu Yerusalemu.
А скеля його промине́ться від стра́ху, і владики його затриво́жаться перед прапором. Так говорить Господь, що має огонь на Сіоні, а в Єрусалимі у Нього горни́ло.

< Yesaya 31 >