< Yesaya 31 >

1 Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo, amene amadalira akavalo, nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo, koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli, kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.
Ay de los que bajan a Egipto en busca de ayuda, y dependen de los caballos, y confía en los carros porque son muchos, y en los jinetes porque son muy fuertes, pero no miran al Santo de Israel, y no buscan a Yahvé.
2 Komatu Yehovayo ndi wanzeru ndipo angathe kuwononga, ndipo sasintha chimene wanena. Adzalimbana ndi anthu ochita zoyipa, komanso ndi amene amathandiza anthu ochita zoyipa.
Pero él también es sabio, y traerá el desastre, y no retirará sus palabras, sino que se levantará contra la casa de los malhechores, y contra la ayuda de los que obran la iniquidad.
3 Aigupto ndi anthu chabe osati Mulungu; akavalo awo ndi nyama chabe osati mizimu. Yehova akangotambasula dzanja lake, amene amapereka chithandizo adzapunthwa, amene amalandira chithandizocho adzagwa; onsewo adzathera limodzi.
Los egipcios son hombres y no Dios; y sus caballos carne, y no espíritu. Cuando Yahvé extienda su mano, tanto el que ayuda como el que no, tropezará, y el que sea ayudado caerá, y todos ellos serán consumidos juntos.
4 Zimene Yehova akunena kwa ine ndi izi: “Monga mkango kapena msona wamkango umabangula ukagwira nyama yake, ndipo suopsedwa kapena kusokonezeka ndi kufuwula kwa abusa amene akulimbana nayo, momwemonso palibe chingaletse Yehova Wamphamvuzonse kubwera kudzatchinjiriza phiri la Ziyoni ndi zitunda zake.
Porque Yahvé me dice, “Como el león y el joven león gruñendo sobre su presa, si se convoca una multitud de pastores contra él, no se desanimará ante su voz, ni rebajarse por su ruido, por lo que Yahvé de los Ejércitos bajará a luchar en el monte Sión y en sus alturas.
5 Monga mbalame zowuluka pamwamba pa zisa zake, Yehova Wamphamvuzonse adzatchinjiriza Yerusalemu; ndi kumupulumutsa, iye adzawupitirira ndi kuwulanditsa.”
Como las aves que revolotean, así protegerá el Señor de los Ejércitos a Jerusalén. Él lo protegerá y lo entregará. Pasará por encima y lo preservará”.
6 Inu Aisraeli, bwererani kwa Iye amene munamuwukira kwakukulu.
Volved a aquel de quien os habéis rebelado profundamente, hijos de Israel.
7 Pakuti tsiku limenelo nonsenu mudzataya mafano anu a siliva ndi golide amene mumapanga ndi manja anu auchimo.
Porque en aquel día cada uno se deshará de sus ídolos de plata y de sus ídolos de oro, pecado que vuestras propias manos han hecho para vosotros.
8 “Aasiriya adzaphedwa ku nkhondo ndi mphamvu osati za munthu. Lupanga, osati la munthu, lidzawawononga. Adzathawa ku nkhondo ndipo anyamata awo adzagwira ntchito yathangata.
“El asirio caerá por la espada, no por el hombre; y la espada, no de la humanidad, lo devorará. Huirá de la espada, y sus jóvenes serán sometidos a trabajos forzados.
9 Mfumu yawo idzamwalira ndi mantha, ndipo atsogoleri awo ankhondo adzathawa ndi mantha kusiya pambuyo mbendera yawo ya nkhondo.” Akutero Yehova, amene moto wake uli mu Ziyoni, ndipo ngʼanjo yake ili mu Yerusalemu.
Su roca desaparecerá a causa del terror, y sus príncipes tendrán miedo del estandarte”. dice Yahvé, cuyo fuego está en Sión, y su horno en Jerusalén.

< Yesaya 31 >