< Yesaya 31 >
1 Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo, amene amadalira akavalo, nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo, koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli, kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.
Biada tym, którzy zstępują do Egiptu po pomoc, polegają na koniach i ufają rydwanom, bo jest ich wiele, i jeźdźcom, bo są bardzo silni, a nie patrzą na Świętego Izraela i nie szukają PANA!
2 Komatu Yehovayo ndi wanzeru ndipo angathe kuwononga, ndipo sasintha chimene wanena. Adzalimbana ndi anthu ochita zoyipa, komanso ndi amene amathandiza anthu ochita zoyipa.
Ale on też jest mądry, dlatego sprowadzi zło, a swoich słów nie cofnie. Lecz powstanie przeciw domowi złoczyńców i przeciwko pomocy tych, którzy czynią nieprawość.
3 Aigupto ndi anthu chabe osati Mulungu; akavalo awo ndi nyama chabe osati mizimu. Yehova akangotambasula dzanja lake, amene amapereka chithandizo adzapunthwa, amene amalandira chithandizocho adzagwa; onsewo adzathera limodzi.
Przecież Egipcjanie są ludźmi, a nie Bogiem, ich konie są ciałem, a nie duchem. Gdy więc PAN wyciągnie swą rękę, padnie i ten, co pomaga, padnie i ten, któremu on pomaga, i tak wszyscy razem zginą.
4 Zimene Yehova akunena kwa ine ndi izi: “Monga mkango kapena msona wamkango umabangula ukagwira nyama yake, ndipo suopsedwa kapena kusokonezeka ndi kufuwula kwa abusa amene akulimbana nayo, momwemonso palibe chingaletse Yehova Wamphamvuzonse kubwera kudzatchinjiriza phiri la Ziyoni ndi zitunda zake.
Tak bowiem PAN powiedział do mnie: Jak ryczy lew lub lwiątko nad swym łupem, choć zwoła się przeciwko niemu gromadę pasterzy i nie lęka się ich wrzasku ani nie kuli się przed ich hałasem, tak zstąpi PAN zastępów, aby walczyć o górę Syjon i o jej pagórek.
5 Monga mbalame zowuluka pamwamba pa zisa zake, Yehova Wamphamvuzonse adzatchinjiriza Yerusalemu; ndi kumupulumutsa, iye adzawupitirira ndi kuwulanditsa.”
Jak ptaki latają [koło swego gniazda], tak PAN zastępów obroni Jerozolimę; [owszem], obroni i wybawi, a przechodząc, zachowa.
6 Inu Aisraeli, bwererani kwa Iye amene munamuwukira kwakukulu.
Nawróćcie się do tego, od którego synowie Izraela mocno odstąpili.
7 Pakuti tsiku limenelo nonsenu mudzataya mafano anu a siliva ndi golide amene mumapanga ndi manja anu auchimo.
Tego dnia bowiem każdy porzuci swoje bożki ze srebra i swoje bożki ze złota, które wasze ręce uczyniły wam na grzech.
8 “Aasiriya adzaphedwa ku nkhondo ndi mphamvu osati za munthu. Lupanga, osati la munthu, lidzawawononga. Adzathawa ku nkhondo ndipo anyamata awo adzagwira ntchito yathangata.
Wtedy Asyryjczyk padnie od miecza, lecz nie [człowieka] walecznego, a miecz nieludzki pochłonie go. I ucieknie przed mieczem, a jego młodzieńcy będą podbici.
9 Mfumu yawo idzamwalira ndi mantha, ndipo atsogoleri awo ankhondo adzathawa ndi mantha kusiya pambuyo mbendera yawo ya nkhondo.” Akutero Yehova, amene moto wake uli mu Ziyoni, ndipo ngʼanjo yake ili mu Yerusalemu.
Swoją twierdzę ominie ze strachu, a jego książęta ulękną się sztandaru, mówi PAN, którego ogień jest na Syjonie, a jego piec – w Jerozolimie.