< Yesaya 31 >

1 Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo, amene amadalira akavalo, nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo, koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli, kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.
A UWE ka poe iho ilalo i Aigupita no ke kokuaia mai. Ka poe i paulele i na lio, a hilinai ma na kaakaua, No ka nui o ia mau mea; A ma na hololio hoi, no ko lakou ikaika nui: Aole hoi e nana aku i ka Mea Hemolele o ka Iseraela, Aole imi aku ma o Iehova la!
2 Komatu Yehovayo ndi wanzeru ndipo angathe kuwononga, ndipo sasintha chimene wanena. Adzalimbana ndi anthu ochita zoyipa, komanso ndi amene amathandiza anthu ochita zoyipa.
He akamai no hoi oia, A e hoopuka mai no ia i ka hewa, Aole ia e kapae i kana mau olelo; Aka, e ala mai no oia iluna e ku e i ka hale o ka poe hana hewa, E ku e hoi i ka poe kokua i na mea hana hewa.
3 Aigupto ndi anthu chabe osati Mulungu; akavalo awo ndi nyama chabe osati mizimu. Yehova akangotambasula dzanja lake, amene amapereka chithandizo adzapunthwa, amene amalandira chithandizocho adzagwa; onsewo adzathera limodzi.
No ka mea, he poe kanaka wale no ko Aigupita, aohe akua; He io no ko lakou mau lio, aohe uhane; E hohola mai no o Iehova i kona lima, A e kulanalana auanei ka mea kokua, E hina no hoi ka mea e kokuaia, A e make pu no lakou a pau.
4 Zimene Yehova akunena kwa ine ndi izi: “Monga mkango kapena msona wamkango umabangula ukagwira nyama yake, ndipo suopsedwa kapena kusokonezeka ndi kufuwula kwa abusa amene akulimbana nayo, momwemonso palibe chingaletse Yehova Wamphamvuzonse kubwera kudzatchinjiriza phiri la Ziyoni ndi zitunda zake.
No ka mea, penei i olelo mai ai o Iehova ia'u, E like me ka uwo ana o ka liona, A me ka liona hou hoi maluna o ka mea ana i pepehi ai, Ina i akoakoa na kahuhipa he nui loa, e ku e ia ia, Aole ia e makau i ko lakou leo, Aole hoi e kulou ilalo no ka lehulehu o lakou: Pela no o Iehova o na kaua e iho mai ai, E kaua mamuli o ka mauna o Ziona, Mamuli hoi o ko laila puu.
5 Monga mbalame zowuluka pamwamba pa zisa zake, Yehova Wamphamvuzonse adzatchinjiriza Yerusalemu; ndi kumupulumutsa, iye adzawupitirira ndi kuwulanditsa.”
E like me na manu lele, pela no o Iehova o na kaua e malama mai ai ia Ierusalema; I kona malama ana, e hoopakele no oia ia wahi, I kona hele ana ae, e hoola mai no oia.
6 Inu Aisraeli, bwererani kwa Iye amene munamuwukira kwakukulu.
E huli oukou i ka mea a ua mamo a Iseraela i haalele ino ai:
7 Pakuti tsiku limenelo nonsenu mudzataya mafano anu a siliva ndi golide amene mumapanga ndi manja anu auchimo.
No ka mea, i kela la, E kiola aku no ke kanaka i kona mau akuakii kala, A me kona mau akuakii gula, I na mea a ko oukou mau lima i hana hewa ai no oukou.
8 “Aasiriya adzaphedwa ku nkhondo ndi mphamvu osati za munthu. Lupanga, osati la munthu, lidzawawononga. Adzathawa ku nkhondo ndipo anyamata awo adzagwira ntchito yathangata.
A e haule no ko Asuria i ka pahikaua, aole nae i ko ke kanaka, E ai no ka pahikaua ia ia, aole nae o ko ke kanaka; E auhee no ia, mai ke alo aku o ka pahikaua, A e auhauia kona poe kanaka ui.
9 Mfumu yawo idzamwalira ndi mantha, ndipo atsogoleri awo ankhondo adzathawa ndi mantha kusiya pambuyo mbendera yawo ya nkhondo.” Akutero Yehova, amene moto wake uli mu Ziyoni, ndipo ngʼanjo yake ili mu Yerusalemu.
E hele aku no ia i kona pohaku, no ka makau. A e makau no kona poe alii no ka hae, Wahi a Iehova, ka mea nana ke ahi ma Ziona, A nana hoi ke kapuahi ma Ierusalema.

< Yesaya 31 >