< Yesaya 31 >

1 Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo, amene amadalira akavalo, nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo, koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli, kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.
Woe to them that go down to Egypt for help, and stay on horses; and trust in chariots, because they are many, and in horsemen, because they are very strong; but they look not unto the Holy One of Israel, neither seek the LORD!
2 Komatu Yehovayo ndi wanzeru ndipo angathe kuwononga, ndipo sasintha chimene wanena. Adzalimbana ndi anthu ochita zoyipa, komanso ndi amene amathandiza anthu ochita zoyipa.
Yet he also is wise, and will bring evil, and will not call back his words: but will arise against the house of the evil-doers, and against the help of them that work iniquity.
3 Aigupto ndi anthu chabe osati Mulungu; akavalo awo ndi nyama chabe osati mizimu. Yehova akangotambasula dzanja lake, amene amapereka chithandizo adzapunthwa, amene amalandira chithandizocho adzagwa; onsewo adzathera limodzi.
Now the Egyptians are men, and not God; and their horses flesh, and not spirit: and when the LORD shall stretch out his hand, both he that helpeth shall stumble, and he that is holpen shall fall, and they all shall fail together.
4 Zimene Yehova akunena kwa ine ndi izi: “Monga mkango kapena msona wamkango umabangula ukagwira nyama yake, ndipo suopsedwa kapena kusokonezeka ndi kufuwula kwa abusa amene akulimbana nayo, momwemonso palibe chingaletse Yehova Wamphamvuzonse kubwera kudzatchinjiriza phiri la Ziyoni ndi zitunda zake.
For thus saith the LORD unto me, Like as when the lion growleth and the young lion over his prey, if a multitude of shepherds be called forth against him, he will not be dismayed at their voice, nor abase himself for the noise of them: so shall the LORD of hosts come down to fight upon mount Zion, and upon the hill thereof.
5 Monga mbalame zowuluka pamwamba pa zisa zake, Yehova Wamphamvuzonse adzatchinjiriza Yerusalemu; ndi kumupulumutsa, iye adzawupitirira ndi kuwulanditsa.”
As birds flying, so will the LORD of hosts protect Jerusalem; he will protect and deliver [it], he will pass over and preserve [it].
6 Inu Aisraeli, bwererani kwa Iye amene munamuwukira kwakukulu.
Turn ye unto him from whom ye have deeply revolted, O children of Israel.
7 Pakuti tsiku limenelo nonsenu mudzataya mafano anu a siliva ndi golide amene mumapanga ndi manja anu auchimo.
For in that day they shall cast away every man his idols of silver, and his idols of gold, which your own hands have made unto you for a sin.
8 “Aasiriya adzaphedwa ku nkhondo ndi mphamvu osati za munthu. Lupanga, osati la munthu, lidzawawononga. Adzathawa ku nkhondo ndipo anyamata awo adzagwira ntchito yathangata.
Then shall the Assyrian fall with the sword, not of man; and the sword, not of men, shall devour him: and he shall flee from the sword, and his young men shall become tributary.
9 Mfumu yawo idzamwalira ndi mantha, ndipo atsogoleri awo ankhondo adzathawa ndi mantha kusiya pambuyo mbendera yawo ya nkhondo.” Akutero Yehova, amene moto wake uli mu Ziyoni, ndipo ngʼanjo yake ili mu Yerusalemu.
And his rock shall pass away by reason of terror, and his princes shall be dismayed at the ensign, saith the LORD, whose fire is in Zion, and his furnace in Jerusalem.

< Yesaya 31 >