< Yesaya 31 >

1 Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo, amene amadalira akavalo, nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo, koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli, kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.
Woe [to] those going down to Egypt for help, And [who] lean on horses, And trust on chariots, because [they are] many, And on horsemen, because [they are] very strong, And have not looked on the Holy One of Israel, And have not sought YHWH.
2 Komatu Yehovayo ndi wanzeru ndipo angathe kuwononga, ndipo sasintha chimene wanena. Adzalimbana ndi anthu ochita zoyipa, komanso ndi amene amathandiza anthu ochita zoyipa.
And He [is] also wise, and brings in evil, And He has not turned aside His words, And He has risen against a house of evildoers, And against the help of workers of iniquity.
3 Aigupto ndi anthu chabe osati Mulungu; akavalo awo ndi nyama chabe osati mizimu. Yehova akangotambasula dzanja lake, amene amapereka chithandizo adzapunthwa, amene amalandira chithandizocho adzagwa; onsewo adzathera limodzi.
And the Egyptians [are men], and not God, And their horses [are] flesh, and not spirit, And YHWH stretches out His hand, And the helper has stumbled, And the helped one has fallen, And together all of them are consumed.
4 Zimene Yehova akunena kwa ine ndi izi: “Monga mkango kapena msona wamkango umabangula ukagwira nyama yake, ndipo suopsedwa kapena kusokonezeka ndi kufuwula kwa abusa amene akulimbana nayo, momwemonso palibe chingaletse Yehova Wamphamvuzonse kubwera kudzatchinjiriza phiri la Ziyoni ndi zitunda zake.
For thus said YHWH to me: “As the lion and the young lion growl over his prey, Against whom a multitude of shepherds is called, He is not frightened from their voice, And he is not humbled from their noise; So YHWH of Hosts comes down To war on Mount Zion, and on her height.
5 Monga mbalame zowuluka pamwamba pa zisa zake, Yehova Wamphamvuzonse adzatchinjiriza Yerusalemu; ndi kumupulumutsa, iye adzawupitirira ndi kuwulanditsa.”
As birds flying, so does YHWH of Hosts Cover over Jerusalem, covering and delivering, Passing over, and causing to escape.”
6 Inu Aisraeli, bwererani kwa Iye amene munamuwukira kwakukulu.
Turn back to Him from whom sons of Israel Have deepened apostasy.
7 Pakuti tsiku limenelo nonsenu mudzataya mafano anu a siliva ndi golide amene mumapanga ndi manja anu auchimo.
For in that day each despises His idols of silver, and his idols of gold, That your hands made to you—a sin.
8 “Aasiriya adzaphedwa ku nkhondo ndi mphamvu osati za munthu. Lupanga, osati la munthu, lidzawawononga. Adzathawa ku nkhondo ndipo anyamata awo adzagwira ntchito yathangata.
And Asshur has fallen by sword, not of the high, Indeed, a sword—not of the low, consumes him, And he has fled for himself from the face of a sword, And his young men become tributary.
9 Mfumu yawo idzamwalira ndi mantha, ndipo atsogoleri awo ankhondo adzathawa ndi mantha kusiya pambuyo mbendera yawo ya nkhondo.” Akutero Yehova, amene moto wake uli mu Ziyoni, ndipo ngʼanjo yake ili mu Yerusalemu.
And he passes on [to] his rock from fear, And his princes have been frightened by the ensign—a declaration of YHWH, Who has a light in Zion, And who has a furnace in Jerusalem!

< Yesaya 31 >