< Yesaya 31 >

1 Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo, amene amadalira akavalo, nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo, koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli, kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.
Cursed are those who go down to Egypt for help, and who put their faith in horses; looking to war-carriages for salvation, because of their numbers; and to horsemen, because they are very strong; but they are not looking to the Holy One of Israel, or turning their hearts to the Lord;
2 Komatu Yehovayo ndi wanzeru ndipo angathe kuwononga, ndipo sasintha chimene wanena. Adzalimbana ndi anthu ochita zoyipa, komanso ndi amene amathandiza anthu ochita zoyipa.
Though he is wise, and able to send evil, and his purpose will not be changed; but he will go against the house of the evil-doers, and against those to whom they are looking for help.
3 Aigupto ndi anthu chabe osati Mulungu; akavalo awo ndi nyama chabe osati mizimu. Yehova akangotambasula dzanja lake, amene amapereka chithandizo adzapunthwa, amene amalandira chithandizocho adzagwa; onsewo adzathera limodzi.
For the Egyptians are men, and not God; and their horses are flesh, and not spirit: and when the Lord's hand is stretched out, the helper and he who is helped will come down together.
4 Zimene Yehova akunena kwa ine ndi izi: “Monga mkango kapena msona wamkango umabangula ukagwira nyama yake, ndipo suopsedwa kapena kusokonezeka ndi kufuwula kwa abusa amene akulimbana nayo, momwemonso palibe chingaletse Yehova Wamphamvuzonse kubwera kudzatchinjiriza phiri la Ziyoni ndi zitunda zake.
For the Lord has said to me, As a lion, or a young lion, makes an angry noise over his food, and if a band of herdsmen come out against him, he will not be in fear of their voices, or give up his food for their noise: so the Lord of armies will come down to make war against Mount Zion and its hill.
5 Monga mbalame zowuluka pamwamba pa zisa zake, Yehova Wamphamvuzonse adzatchinjiriza Yerusalemu; ndi kumupulumutsa, iye adzawupitirira ndi kuwulanditsa.”
Like birds with outstretched wings, so will the Lord of armies be a cover to Jerusalem; he will be a cover and salvation for it, going over it he will keep it from danger.
6 Inu Aisraeli, bwererani kwa Iye amene munamuwukira kwakukulu.
Come back to him who has been so deeply sinned against by the children of Israel.
7 Pakuti tsiku limenelo nonsenu mudzataya mafano anu a siliva ndi golide amene mumapanga ndi manja anu auchimo.
For in that day they will all give up their images of silver and of gold, the sin which they made for themselves.
8 “Aasiriya adzaphedwa ku nkhondo ndi mphamvu osati za munthu. Lupanga, osati la munthu, lidzawawononga. Adzathawa ku nkhondo ndipo anyamata awo adzagwira ntchito yathangata.
Then the Assyrian will come down by the sword, but not of man; the sword, not of men, will be the cause of his destruction: and he will go in flight from the sword, and his young men will be put to forced work.
9 Mfumu yawo idzamwalira ndi mantha, ndipo atsogoleri awo ankhondo adzathawa ndi mantha kusiya pambuyo mbendera yawo ya nkhondo.” Akutero Yehova, amene moto wake uli mu Ziyoni, ndipo ngʼanjo yake ili mu Yerusalemu.
And his rock will come to nothing because of fear, and his chiefs will go in flight from the flag, says the Lord, whose fire is in Zion, and his altar in Jerusalem.

< Yesaya 31 >