< Yesaya 30 >

1 Yehova akuti, “Tsoka kwa ana ondipandukira amene amachita zowakomera iwo okha osati Ine, nachita mgwirizano wawowawo koma osati motsogozedwa ndi Ine. Choncho amanka nachimwirachimwira.
Горе синам неслухня́ним, говорить Господь, що чинять наради, які не від Мене, і складають умови, — та без Духа Мого, щоб додати гріх на гріх,
2 Amapita ku Igupto kukapempha thandizo koma osandifunsa; amathawira kwa Farao kuti awateteze, ku Igupto amafuna malo opulumulira.
що йдуть, щоб зійти до Єгипту, але Моїх уст не питали, щоб за́хисту у фараона шукати, і щоб сховатися в тіні Єгипту!
3 Koma chitetezo cha Farao chidzakhala manyazi anu, malo a mthunzi a ku Igupto mudzachita nawo manyazi.
І стане вам соромом за́хист отой фараонів, а хова́ння у тіні Єгипту — за га́ньбу,
4 Ngakhale kuti nduna zawo zili ku Zowani, ndipo akazembe awo afika kale ku Hanesi,
бо в Цоані були його провідники́, і його посланці́ до Ханесу прийшли.
5 aliyense wa ku Yuda adzachita manyazi chifukwa cha anthu opanda nawo phindu, amene sabweretsa thandizo kapena phindu, koma manyazi ndi mnyozo.”
Вони посоро́млені будуть усі за наро́д, що не буде кори́сний для них, що не буде на поміч і не на пожи́ток, а на сором та га́ньбу.
6 Uthenga wonena za nyama za ku Negevi: Akazembe akuyenda mʼdziko lovuta ndi losautsa, mʼmene muli mikango yayimuna ndi yayikazi, mphiri ndi njoka zaululu. Iwo amasenzetsa abulu ndi ngamira chuma chawo, kupita nazo kwa mtundu wa anthu umene sungawathandize.
Пророцтво про Бегемота пі́вдня. В краю у́тиску та переслі́дування, звідки леви́ця та лев, гадюка й огни́стий летю́чий драко́н, носять багатство своє на хребті́ молодих ослюкі́в, і скарби свої на верблю́жім горбі́ до наро́ду, який не поможе.
7 Amapita ku Igupto amene thandizo lake ndi lachabechabe. Nʼchifukwa chake dzikolo ndalitcha Rahabe chirombo cholobodoka.
А Єгипет, — його поміч марна́ та пуста́, тому́ то я кликнув на теє: Рагав, сидіти спокійно!
8 Yehova anandiwuza kuti, “Tsopano pita, ukalembe zimenezi mʼbuku iwo akuona ndipo lidzakhala ngati umboni wosatha masiku a mʼtsogolo.
Тепер увійди, напиши на табли́ці для них, і в книжці спиши це, і нехай на пізніші часи́ воно буде і сві́дком навіки.
9 Amenewa ndi anthu owukira, onama ndi osafuna kumvera malangizo a Yehova.
Бо це неслухняний наро́д, це брехливі сини́, сини́, що не хочуть послухати науки Господньої,
10 Iwo amawuza alosi kuti, ‘Musationerenso masomphenya!’ Ndipo amanena kwa mneneri kuti, ‘Musatinenerenso zoona,’ mutiwuze zotikomera, munenere za mʼmutu mwanu.
що говорять прови́дцям: „Не бачте!“а пророкам: „Не пророкуйте правдивого нам, говоріть нам гладе́ньке, передба́чте ома́нливе,
11 Patukani pa njira ya Yehova, lekani kutsata njira ya Yehova; ndipo tisamvenso mawu a Woyerayo uja wa Israeli!”
уступіться з дороги, збо́чте з путі, заберіть з-перед нас Святого Ізраїлевого!“
12 Nʼchifukwa chake Woyerayo wa Israeli akunena kuti, “Popeza inu mwakana uthenga uwu, mumakhulupirira zopondereza anzanu ndipo mumadalira kuchita zoyipa,
Тому́ промовляє Святий Ізраїлів так: За те, що ви не́хтуєте оцим словом, і надію кладе́те на тиск та круті́йство, і на це опира́єтеся,
13 choncho tchimo linalo lidzakhala ngati mingʼalu pa khoma lalitali ndi lopendama limene linagwa mwadzidzidzi ndi mwamsangamsanga.
тому буде для вас ця прови́на, як ви́лім, що має впасти, що зя́є на мурі високім, що нагло, рапто́вно приходить руїна його!
14 Lidzaphwanyika ngati mbiya imene yanyenyekeratu, mwakuti pakati pake sipadzapezeka phale ngakhale lopalira moto mʼngʼanjo kapena lotungira madzi mʼchitsime.”
I Він поруйнує його, як руйнується по́суд ганча́рський, розбиваючи без милосердя його, і в ула́мках його не знайдеться ані черепка́, щоб із о́гнища взяти огню́ чи води зачерпну́ти з кринички.
15 Zimene Ambuye Yehova, Woyerayo wa Israeli ananena ndi izi: “Ngati mubwerera ndi kupuma mudzapulumuka, ngati mukhala chete ndi kukhulupirira mudzakhala amphamvu, koma inu munakana zimenezi.
Бо так промовляє Господь, Бог, Святий Ізраїлів: Коли ви наве́рнетесь та спочи́нете, то врято́вані будете, сила вам буде в ути́шенні та в сподіва́нні. Та ви не хотіли,
16 Inu mukuti, ‘Ayi ife tidzathawa, tidzakwera pa akavalo aliwiro.’ Zoonadi kuti mudzakwera pa akavalo aliwiro, koma okuthamangitsani adzakhalanso aliwiro.
і казали: „О ні, бо на ко́нях втечемо“, тому́ то втікати ви будете, „На баски́х ми поїдемо“, тому стануть баски́ми пого́ничі ваші!
17 Anthu 1,000 mwa inu adzathawa poona mdani mmodzi; poona adani asanu okha nonsenu mudzathawa. Otsala anu adzakhala ngati mbendera pa phiri, ndi ngati chizindikiro cha pa chulu.”
Від крику одно́го — поли́не одна тисяча, від крику п'ятьох — дремене́те ви всі, аж зоста́нетеся, немов що́гла ота на верше́чку гори, і немов пра́пор на взгі́р'ї!
18 Komatu Yehova akufunitsitsa kuti akukomereni mtima, iye ali wokonzeka kuti akuchitireni chifundo. Pakuti Yehova ndi Mulungu wachilungamo. Ndi odala onse amene amakhulupirira Iye!
І проте Господь буде чекати, щоб помилувати вас, і тому́ Він піді́йметься, щоб милосердя вчинити над вами. Бо Господи — то Бог правосу́ддя: блаженні всі ті, хто наді́ю на Нього кладе́!
19 Inu anthu a ku Ziyoni, amene mukhala mu Yerusalemu simudzaliranso. Mulungu adzakukomerani mtima pamene adzamva kulira kwanu kopempha thandizo! Ndipo akadzamva, adzakuyankhani.
Бо ти, о наро́де в Сіоні, що в Єрусалимі сидиш, плакати — не будеш ти плакати: милости́вим поправді Він буде до тебе на голос блага́ння твого, і як почує його, відповість Він тобі.
20 Ngakhale Ambuye adzakulowetseni mʼmasautso, aphunzitsi anu sadzakhala kakasi; inu mudzawaona ndi maso anuwo.
І дасть вам Господь хліба в у́тиску і воду в гноби́тельстві, та твої вчителі́ вже не бу́дуть хова́тись, і очі твої вчителі́в твоїх бачити бу́дуть.
21 Ngati mudzapatukira kumanja kapena kumanzere, mudzamva mawu kumbuyo kwanu woti, “Njira ndi iyi; yendani mʼmenemo.”
А коли ви відхи́литесь право́руч, чи пі́дете ліво́руч, то вуха твої будуть чути те слово, яке позад тебе казатиме: „Це та дорога, — просту́йте ви нею!“
22 Pamenepo mudzawononga mafano anu okutidwa ndi siliva ndiponso zifanizo zanu zokutidwa ndi golide; mudzawataya ngati zinthu zonyansa ndipo mudzati, “Zichoke zonsezi!”
І нечистим учините ви поволо́ку бовва́нів своїх із срібла́ й покриття́ на божка́ золотого свого, розпоро́шиш ти їх, як нечисте, і „геть" скажеш йому́.
23 Yehova adzakugwetseraninso mvula pa mbewu zanu zimene mukadzale mʼnthaka, ndipo chakudya chimene mudzakolole chidzakhala chabwino ndi chochuluka. Tsiku limenelo ngʼombe zanu zidzadya msipu wochuluka.
І Він пошле дощ на насіння твоє, яким бу́деш обсі́ювати землю, та хліб урожаю землі, — і пожи́вний та ситий він буде. Того дня на широкім пасо́виську па́стися буде твоя череда́,
24 Ngʼombe ndi abulu amene amalima mʼmunda adzadya chakudya chamchere, chopetedwa ndi foloko ndi fosholo.
а воли й віслюки́, що обро́блюють землю, будуть мі́шанку їсти солону, лопа́тою й ві́ялкою перечи́щену.
25 Pa tsiku limene adani anu adzaphedwa ndi nsanja zawo kugwa, mitsinje ya madzi idzayenda pa phiri lililonse lalikulu ndi pa phiri lililonse lalingʼono.
І на кожній високій горі та на кожному взгі́р'ї високому бу́дуть струмки́ та пото́ки води в день великого бо́ю, коли ба́шти попа́дають.
26 Mwezi udzawala ngati dzuwa, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzawonjezereka kasanu nʼkawiri, ngati kuwala kwa tsiku limodzi. Yehova adzamanga mabala a anthu ake ndi kupoletsa zilonda zimene Iye anachititsa polanga anthu ake.
І світло місяця стане, немов світло сонця, світло ж сонця усе́меро буде ясніше, як сімох днів, у той день, як Господь перев'я́же злама́ння народу Свого та заго́їть пора́нення вдару Свого!
27 Taonani, Yehova akubwera kuchokera kutali, ndipo mkwiyo wake ndiwonyeka ndi chiweruzo chake chidzakhala chopweteka. Iye wayankhula mwaukali kwambiri, ndipo mawu ake ali ngati moto wonyeka.
Ось Іме́ння Господнє прихо́дить здале́ка, палахкоти́ть Його гнів, і здійма́ється тя́жко: Його уста обу́рення повні, язик же Його, як жеру́щий огонь,
28 Mpweya wake uli ngati mtsinje wosefukira, wa madzi ofika mʼkhosi. Iye adzasefa anthu a mitundu ina ndi sefa wosakaza; Iye akuyika zitsulo mʼkamwa mwa anthu a mitundu ina ngati akavalo, kuti ziwasocheretse.
Його ж подих, як пото́п заливни́й, що до шиї сяга́є, щоб просі́яти люди на ситі погибелі. І буде на ще́лепах людів вузде́чка, що тя́гне до блу́ду.
29 Ndipo inu mudzayimba mokondwa monga mumachitira usiku pa chikondwerero chopatulika. Mudzasangalala ngati anthu oyimba zitoliro popita ku phiri la Yehova, thanthwe la Israeli.
Буде пісня для вас, як за но́чі освя́чення свята, і радість сердечна, мов у то́го, хто ходить з сопі́лкою, щоб вийти на го́ру Господню до Скелі Ізраїля.
30 Anthu adzamva liwu la ulemerero la Yehova ndipo adzaona dzanja lake likutsika pa iwo ndi mkwiyo woopsa, pamodzi ndi moto wonyeketsa, mphenzi, namondwe ndi matalala.
І Господь дасть почути велич голосу Свого, опуска́ння ж раме́на Свого покаже у гніві бурхли́вому та в огняно́му жеру́щому по́лум'ї, у бурі й дощі, та в камі́нному граді!
31 Asiriya adzaopa liwu la Yehova, ndipo Iye adzawakantha ndi ndodo.
Бо від голосу Господа буде лякатись Ашшу́р, що жезлом буде битий.
32 Yehova akamadzalanga adani ake ndi ndodo, anthu ake adzakhala akuvina nyimbo zoyimbira matambolini ndi azeze, Yehova ndiye ati adzamenyane ndi Asiriyawo.
І станеться, кожне уда́рення кия кара́ння Його, що на нього Господь покладе, буде з бу́бнами й а́рфою, і Він рухом Своєї руки воюватиме з ним у боя́х.
33 Malo otenthera zinthu akonzedwa kale; anakonzera mfumu ya ku Asiriya. Dzenje la motolo ndi lozama ndi lalikulu, ndipo muli nkhuni zambiri; mpweya wa Yehova, wangati mtsinje wa sulufule, udzayatsa motowo pa nkhunizo.
Бо давно пригото́влений То́фет, — пригото́влений він і для царя, глибоким, широким учи́нений; на бага́тті огню його й дров багате́нно, — запалить його подих Господній, немов би пото́ка сірча́ного!

< Yesaya 30 >