< Yesaya 30 >

1 Yehova akuti, “Tsoka kwa ana ondipandukira amene amachita zowakomera iwo okha osati Ine, nachita mgwirizano wawowawo koma osati motsogozedwa ndi Ine. Choncho amanka nachimwirachimwira.
Teško sinovima odmetničkim! - riječ je Jahvina. Oni provode osnove koje nisu moje, sklapaju saveze koji nisu po mom duhu i grijeh na grijeh gomilaju.
2 Amapita ku Igupto kukapempha thandizo koma osandifunsa; amathawira kwa Farao kuti awateteze, ku Igupto amafuna malo opulumulira.
Zaputiše se u Egipat, ne pitajući usta moja, da se uteku faraonovu zaklonu i da se zaštite u sjeni Egipta.
3 Koma chitetezo cha Farao chidzakhala manyazi anu, malo a mthunzi a ku Igupto mudzachita nawo manyazi.
Zaklon faraonov bit će na sramotu, i na ruglo zaštita u sjeni Egipta.
4 Ngakhale kuti nduna zawo zili ku Zowani, ndipo akazembe awo afika kale ku Hanesi,
Eno mu knezova već u Soanu, podanici stigoše u Hanes:
5 aliyense wa ku Yuda adzachita manyazi chifukwa cha anthu opanda nawo phindu, amene sabweretsa thandizo kapena phindu, koma manyazi ndi mnyozo.”
svi će se oni razočarati u narodu beskorisnom, neće im biti na pomoć ni na korist, već na sramotu i porugu.
6 Uthenga wonena za nyama za ku Negevi: Akazembe akuyenda mʼdziko lovuta ndi losautsa, mʼmene muli mikango yayimuna ndi yayikazi, mphiri ndi njoka zaululu. Iwo amasenzetsa abulu ndi ngamira chuma chawo, kupita nazo kwa mtundu wa anthu umene sungawathandize.
Proroštvo o negepskim životinjama. Kroza zemlju nevolje i bijede, lavice i lava koji riču, ljutice i zmaja krilatog, nose oni blago na leđima magaraca i bogatstvo na grbi deva, nose ga narodu beskorisnom.
7 Amapita ku Igupto amene thandizo lake ndi lachabechabe. Nʼchifukwa chake dzikolo ndalitcha Rahabe chirombo cholobodoka.
Jer prazna je i ništavna pomoć Egipta, zato ga i zovemo: Rahab - danguba.
8 Yehova anandiwuza kuti, “Tsopano pita, ukalembe zimenezi mʼbuku iwo akuona ndipo lidzakhala ngati umboni wosatha masiku a mʼtsogolo.
Ded napiši na ploču i zapiši u knjigu da vremenima budućim svjedočanstvo ostane.
9 Amenewa ndi anthu owukira, onama ndi osafuna kumvera malangizo a Yehova.
Ovo je narod odmetnički, sinovi lažljivi, sinovi koji neće da slušaju Zakon Jahvin.
10 Iwo amawuza alosi kuti, ‘Musationerenso masomphenya!’ Ndipo amanena kwa mneneri kuti, ‘Musatinenerenso zoona,’ mutiwuze zotikomera, munenere za mʼmutu mwanu.
Vidovitima oni govore: “Okanite se viđenja!” a vidiocima: “Ne prorokujte istinu! Govorite nam što je ugodno, opsjene nam prorokujte!
11 Patukani pa njira ya Yehova, lekani kutsata njira ya Yehova; ndipo tisamvenso mawu a Woyerayo uja wa Israeli!”
Skrenite s puta, zastranite sa staze, uklonite nam s očiju Sveca Izraelova!”
12 Nʼchifukwa chake Woyerayo wa Israeli akunena kuti, “Popeza inu mwakana uthenga uwu, mumakhulupirira zopondereza anzanu ndipo mumadalira kuchita zoyipa,
Stog' ovako zbori Svetac Izraelov: “Jer riječ ovu odbacujete, a uzdate se u opačinu i prijevaru i na njih se oslanjate,
13 choncho tchimo linalo lidzakhala ngati mingʼalu pa khoma lalitali ndi lopendama limene linagwa mwadzidzidzi ndi mwamsangamsanga.
grijeh će vam taj biti poput pukotine, visoko na zidu izbočene, koja prijeti rušenjem.
14 Lidzaphwanyika ngati mbiya imene yanyenyekeratu, mwakuti pakati pake sipadzapezeka phale ngakhale lopalira moto mʼngʼanjo kapena lotungira madzi mʼchitsime.”
Da se sruši k'o što se glinen sud razbije, slupan nemilice, te mu se među krhotinama ne nađe ni rbine, žerave da uzmeš s ognjišta il' zagrabiš vode iz studenca.”
15 Zimene Ambuye Yehova, Woyerayo wa Israeli ananena ndi izi: “Ngati mubwerera ndi kupuma mudzapulumuka, ngati mukhala chete ndi kukhulupirira mudzakhala amphamvu, koma inu munakana zimenezi.
Jer ovako govori Jahve Gospod, Svetac Izraelov: “Mir i obraćenje - spas vam je, u smirenu uzdanju snaga je vaša. Ali vi ne htjedoste.
16 Inu mukuti, ‘Ayi ife tidzathawa, tidzakwera pa akavalo aliwiro.’ Zoonadi kuti mudzakwera pa akavalo aliwiro, koma okuthamangitsani adzakhalanso aliwiro.
Rekoste: 'Ne! Pobjeći ćemo na konjima!' - i zato, bježat ćete! 'Na brzim ćemo konjima jahati!' - i zato, bit će brži vaši neprijatelji!”
17 Anthu 1,000 mwa inu adzathawa poona mdani mmodzi; poona adani asanu okha nonsenu mudzathawa. Otsala anu adzakhala ngati mbendera pa phiri, ndi ngati chizindikiro cha pa chulu.”
Pobjeći će vas tisuća kad jedan zaprijeti, zaprijete li petorica, u bijeg ćete nagnut' dok vas ne preostane k'o kopljača na vrhu gore il' na brijegu zastava.
18 Komatu Yehova akufunitsitsa kuti akukomereni mtima, iye ali wokonzeka kuti akuchitireni chifundo. Pakuti Yehova ndi Mulungu wachilungamo. Ndi odala onse amene amakhulupirira Iye!
Al' Jahve čeka čas da vam se smiluje, i stog izglÄedÄa da vam milost iskaže, jer Jahve je Bog pravedan - blago svima koji njega čekaju.
19 Inu anthu a ku Ziyoni, amene mukhala mu Yerusalemu simudzaliranso. Mulungu adzakukomerani mtima pamene adzamva kulira kwanu kopempha thandizo! Ndipo akadzamva, adzakuyankhani.
Da, puče sionski koji živiš u Jeruzalemu, više ne plači! Čim začuje vapaj tvoj, odmah će ti se smilovati; čim te čuje, uslišit će te.
20 Ngakhale Ambuye adzakulowetseni mʼmasautso, aphunzitsi anu sadzakhala kakasi; inu mudzawaona ndi maso anuwo.
Hranit će vas Gospod kruhom tjeskobe, pojiti vodom nevolje, al' se više neće kriti tvoj Učitelj - oči će ti gledati Učitelja tvoga.
21 Ngati mudzapatukira kumanja kapena kumanzere, mudzamva mawu kumbuyo kwanu woti, “Njira ndi iyi; yendani mʼmenemo.”
I uši će tvoje čuti riječ gdje iza tebe govori: “To je put, njime idite”, bilo da vam je krenuti nadesno ili nalijevo.
22 Pamenepo mudzawononga mafano anu okutidwa ndi siliva ndiponso zifanizo zanu zokutidwa ndi golide; mudzawataya ngati zinthu zonyansa ndipo mudzati, “Zichoke zonsezi!”
Smatrat ćeš nečistima svoje srebrne kumire i pozlatu svojih kipova; odbacit ćeš ih kao nečist i reći im: “Napolje!”
23 Yehova adzakugwetseraninso mvula pa mbewu zanu zimene mukadzale mʼnthaka, ndipo chakudya chimene mudzakolole chidzakhala chabwino ndi chochuluka. Tsiku limenelo ngʼombe zanu zidzadya msipu wochuluka.
A on će dati kišu tvojem sjemenu što ga posiješ u zemlju, i kruh kojim zemlja urodi bit će obilat i hranjiv. Stoka će tvoja pasti u onaj dan po prostranim pašnjacima.
24 Ngʼombe ndi abulu amene amalima mʼmunda adzadya chakudya chamchere, chopetedwa ndi foloko ndi fosholo.
Volovi i magarci što obrađuju zemlju jest će osoljenu krmu, ovijanu lopatom i vijačom.
25 Pa tsiku limene adani anu adzaphedwa ndi nsanja zawo kugwa, mitsinje ya madzi idzayenda pa phiri lililonse lalikulu ndi pa phiri lililonse lalingʼono.
I na svakoj gori i na svakome povišenom brijegu bit će potoka i rječica - u dan silnoga pokolja kad se kule budu rušile.
26 Mwezi udzawala ngati dzuwa, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzawonjezereka kasanu nʼkawiri, ngati kuwala kwa tsiku limodzi. Yehova adzamanga mabala a anthu ake ndi kupoletsa zilonda zimene Iye anachititsa polanga anthu ake.
Tada će svjetlost mjesečeva biti kao svjetlost sunčana, a svjetlost će sunčana postati sedam puta jača, kao svjetlost sedam dana - u dan kad Jahve iscijeli prijelom svojemu narodu, izliječi rane svojih udaraca.
27 Taonani, Yehova akubwera kuchokera kutali, ndipo mkwiyo wake ndiwonyeka ndi chiweruzo chake chidzakhala chopweteka. Iye wayankhula mwaukali kwambiri, ndipo mawu ake ali ngati moto wonyeka.
Gle, ime Jahve izdaleka dolazi, gnjev njegov gori, dim je neizdrživ. Usne su mu pune jarosti, jezik mu oganj što proždire.
28 Mpweya wake uli ngati mtsinje wosefukira, wa madzi ofika mʼkhosi. Iye adzasefa anthu a mitundu ina ndi sefa wosakaza; Iye akuyika zitsulo mʼkamwa mwa anthu a mitundu ina ngati akavalo, kuti ziwasocheretse.
Dah mu je kao potok nabujali što do grla seže. On dolazi da prosije narode rešetom zatornim, da stavi uzde zavodljive u čeljusti naroda.
29 Ndipo inu mudzayimba mokondwa monga mumachitira usiku pa chikondwerero chopatulika. Mudzasangalala ngati anthu oyimba zitoliro popita ku phiri la Yehova, thanthwe la Israeli.
Tad će vam pjesma biti kao u noćima blagdanskim, kad su srca vesela kao u onoga koji uza zvuke frule hodočasti na Goru Jahvinu, k Stijeni Izraelovoj.
30 Anthu adzamva liwu la ulemerero la Yehova ndipo adzaona dzanja lake likutsika pa iwo ndi mkwiyo woopsa, pamodzi ndi moto wonyeketsa, mphenzi, namondwe ndi matalala.
Jahve će zagrmjet glasom veličajnim i pokazat ruku svoju što udara u jarosnu gnjevu, sred ognja zatornog, iz olujna pljuska i krupÄe kamene.
31 Asiriya adzaopa liwu la Yehova, ndipo Iye adzawakantha ndi ndodo.
Od glasa Jahvina prepast će se Asur, šibom ošinut.
32 Yehova akamadzalanga adani ake ndi ndodo, anthu ake adzakhala akuvina nyimbo zoyimbira matambolini ndi azeze, Yehova ndiye ati adzamenyane ndi Asiriyawo.
I kad god ga udari šiba kaznena, kojom će ga Jahve išibati, nek' se oglase bubnjevi i citare - u sav jek boja on s njima ratuje!
33 Malo otenthera zinthu akonzedwa kale; anakonzera mfumu ya ku Asiriya. Dzenje la motolo ndi lozama ndi lalikulu, ndipo muli nkhuni zambiri; mpweya wa Yehova, wangati mtsinje wa sulufule, udzayatsa motowo pa nkhunizo.
Odavna je pripravljen Tofet za Moleka - lomača visoka, široka, mnogo ognja, mnogo drvlja. Dah gnjeva Jahvina, kao potok sumporni, njega će spaliti.

< Yesaya 30 >