< Yesaya 3 >
1 Taonani tsopano, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yuda zinthu pamodzi ndi thandizo; adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse,
Albowiem oto panujący Pan zastępów odejmie od Jeruzalemu i od Judy łaskę, i podporę, wszelaką podporę chleba, i wszelaką podporę wody.
2 anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo, oweruza ndi aneneri, anthu olosera ndi akuluakulu,
Mocarza i męża walecznego, i sędziego, i proroka, i mędrca, i starca;
3 atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka, aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera.
Rotmistrza nad pięćdziesiąt, a męża poważnego, i radcę, i mądrego rzemieślnika, i krasomówcę.
4 Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo; ana akhanda ndiwo adzawalamulire.
I dam im dzieci za książęta; dzieci mówię panować będą nad nimi.
5 Anthu adzazunzana, munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake. Anthu wamba adzanyoza akuluakulu.
I będzie uciskał między ludem jeden drugiego, i bliźni bliźniego swego: powstanie dziecię przeciwko starcowi, a podły przeciwko zacnemu.
6 Munthu adzagwira mʼbale wake mʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati, “Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu; lamulira malo opasuka ano!”
A gdy się uchwyci każdy brata swego z domu ojca swego, i rzecze: Masz odzienie, bądźże książęciem naszym, a upadek ten zatrzymaj ręką swą:
7 Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti, “Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake. Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga; musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.”
Tedy on przysięże dnia onego, mówiąc: Nie będę zawiązywał tych ran: albowiem w domu moim niemasz chleba, ani odzienia; nie stanowcież mię książęciem nad ludem.
8 Yerusalemu akudzandira, Yuda akugwa; zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova, sakulabadira ulemerero wa Mulungu.
Bo Jeruzalem upada, a Juda się wali, dlatego, że język ich, i sprawy ich są przeciwko Panu, pobudzając do gniewu oczy majestatu jego.
9 Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa; amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu; salibisa tchimo lawolo. Tsoka kwa iwo odziputira okha mavuto.
Postawa oblicza ich świadczy przeciwko nim; grzech swój, jako Sodomczycy, opowiadają, a nie tają go. Biada duszy ich! albowiem sami na się złe przywodzą.
10 Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino, pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo.
Powiedzcie sprawiedliwemu, że mu dobrze będzie; bo owocu uczynków swoich pożywać będzie.
11 Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo! Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita.
Ale biada niepobożnemu! źle mu będzie; albowiem odpłata rąk jego dana mu będzie.
12 Achinyamata akupondereza anthu anga, ndipo amene akuwalamulira ndi akazi. Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani; akukuchotsani pa njira yanu.
Książęta ludu mego są dziećmi, a niewiasty panują nad nimi. O ludu mój! ci, którzy cię wodzą, zwodzą cię, a drogę ścieżek twoich ukrywają.
13 Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu; wakonzeka kuti aweruze anthu ake.
Powstał Pan, aby sądził, stoi, aby sądził lud.
14 Yehova akuwazenga milandu akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake: “Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa; nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi.
Pan przyjdzie na sąd przeciwko starszym ludu swego, i przeciwko książętom ich, a rzecze: Wyście spustoszyli winnicę moję, zdzierstwo z ubogiego w domach waszych.
15 Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga, nʼkudyera masuku pamutu amphawi?” Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
Przeczże trzecie lud mój, a oblicza ubogich bijecie? mówi Pan, Pan zastępów.
16 Yehova akunena kuti, “Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri, akuyenda atakweza makosi awo, akukopa amuna ndi maso awo akuyenda monyangʼama akuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo
I rzekł Pan: Iż się wynoszą córki Syońskie, a chodzą szyje wyciągnąwszy, i mrugając oczyma przechodzą się, a drobno postępując nogami swemi szelest czynią:
17 Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo; Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.”
Przetoż obłysi Pan wierzch głowy córek Syońskich, a Pan sromotę ich obnaży.
18 Tsiku limenelo Ambuye adzawachotsera zodzikongoletsera zawo: za mʼmiyendo, za ku mutu za mʼkhosi,
Dnia onego odejmie Pan ochędóstwo podwiązek, także czepce i zawieszenia,
19 ndolo ndi zibangiri, nsalu zophimba pa nkhope,
Piżmowe jabłka, i manele, i zatyczki,
20 maduku, zigwinjiri za mʼmiyendo ndi malamba, mabotolo a zonunkhira ndi zithumwa,
Bieretki, i zapony, i bindy, i przedniczki, i nausznice;
Pierścionki, i naczelniki,
22 zovala za pa mphwando, zipewa ndi mwinjiro, zikwama,
Odmienne szaty, i płaszczyki, i podwiki, i wacki,
23 magalasi oyangʼanira, zovala zosalala, nduwira ndiponso nsalu za mʼmapewa.
Zwierciadła, i rantuszki, i tkanki, i letniki.
24 Mʼmalo mwa kununkhira azidzanunkha, mʼmalo mwa lamba, adzavala chingwe; mʼmalo mwa tsitsi lopesa bwino, adzakhala ndi dazi; mʼmalo mwa zovala zabwino, adzavala chiguduli; mʼmalo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.
I będzie miasto wonnych rzeczy smród, a miasto pasa rozpasanie, a miasto utrefionych włosów łysina, a miasto szerokiej szaty opasanie worem, a miasto piękności ogorzelina.
25 Iwe Yerusalemu anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga, asilikali ako adzafera ku nkhondo.
Mężowie twoi od miecza upadną, a mocarze twoi w bitwie.
26 Pa zipata za Ziyoni padzakhala kubuma ndi kulira; Iweyo udzasakazidwa nʼkukhala pansi, ukugubuduzika pa fumbi.
I zasmucą się, a płakać będą bramy jego, a spustoszony na ziemi siedzieć będzie.