< Yesaya 3 >

1 Taonani tsopano, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yuda zinthu pamodzi ndi thandizo; adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse,
Car voici, le Seigneur, l'Éternel des armées, va ôter de Jérusalem et de Juda tout appui et toute ressource, toute ressource de pain et toute ressource d'eau;
2 anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo, oweruza ndi aneneri, anthu olosera ndi akuluakulu,
L'homme fort et l'homme de guerre, le juge et le prophète, le devin et l'ancien,
3 atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka, aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera.
Le chef de cinquantaines et l'homme considéré, le conseiller, l'artisan habile et celui qui s'entend à la magie.
4 Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo; ana akhanda ndiwo adzawalamulire.
Et je leur donnerai des jeunes gens pour chefs, et des enfants domineront sur eux.
5 Anthu adzazunzana, munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake. Anthu wamba adzanyoza akuluakulu.
Le peuple sera opprimé; l'un s'élèvera contre l'autre, et chacun contre son prochain; le jeune homme attaquera le vieillard, et l'homme de rien celui qui est honoré.
6 Munthu adzagwira mʼbale wake mʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati, “Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu; lamulira malo opasuka ano!”
Alors un homme saisira son frère dans la maison paternelle: Tu as un manteau, sois notre chef, et prends en main ces ruines!
7 Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti, “Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake. Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga; musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.”
Mais, en ce jour-là, celui-ci répondra, disant: Je n'y saurais porter remède; il n'y a dans ma maison ni pain ni manteau; ne m'établissez pas chef du peuple.
8 Yerusalemu akudzandira, Yuda akugwa; zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova, sakulabadira ulemerero wa Mulungu.
Car Jérusalem s'écroule, et Juda tombe, parce que leurs paroles et leurs actions sont contre l'Éternel, pour braver les regards de sa majesté.
9 Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa; amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu; salibisa tchimo lawolo. Tsoka kwa iwo odziputira okha mavuto.
L'impudence de leurs visages témoigne contre eux; comme Sodome, ils publient leur péché, et ne le dissimulent point. Malheur à leur âme! Car elle se prépare des maux.
10 Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino, pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo.
Dites les justes heureux; car ils mangeront le fruit de leurs œuvres.
11 Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo! Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita.
Malheur au méchant, malheur! Car il recueillera l'œuvre de ses mains.
12 Achinyamata akupondereza anthu anga, ndipo amene akuwalamulira ndi akazi. Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani; akukuchotsani pa njira yanu.
Mon peuple a des enfants pour oppresseurs, et des femmes dominent sur lui. Mon peuple, tes guides t'égarent et t'ont fait perdre le chemin que tu dois suivre.
13 Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu; wakonzeka kuti aweruze anthu ake.
L'Éternel se présente pour plaider; il est debout pour juger les peuples.
14 Yehova akuwazenga milandu akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake: “Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa; nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi.
L'Éternel entre en jugement avec les anciens de son peuple, et avec ses princes: c'est vous qui avez dévoré la vigne! La dépouille du pauvre est dans vos maisons!
15 Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga, nʼkudyera masuku pamutu amphawi?” Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
De quel droit foulez-vous mon peuple et écrasez-vous la face des pauvres, dit le Seigneur, l'Éternel des armées?
16 Yehova akunena kuti, “Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri, akuyenda atakweza makosi awo, akukopa amuna ndi maso awo akuyenda monyangʼama akuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo
L'Éternel dit encore: Parce que les filles de Sion sont orgueilleuses, qu'elles marchent le cou tendu en faisant des signes des yeux, et qu'elles marchent à petits pas, faisant résonner les boucles de leurs pieds,
17 Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo; Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.”
Le Seigneur rendra chauve la tête des filles de Sion, l'Éternel découvrira leur nudité.
18 Tsiku limenelo Ambuye adzawachotsera zodzikongoletsera zawo: za mʼmiyendo, za ku mutu za mʼkhosi,
En ce jour-là, le Seigneur ôtera les anneaux dont elles se parent, les filets et les croissants;
19 ndolo ndi zibangiri, nsalu zophimba pa nkhope,
Les pendants d'oreille, les bracelets et les voiles;
20 maduku, zigwinjiri za mʼmiyendo ndi malamba, mabotolo a zonunkhira ndi zithumwa,
Les diadèmes, les chaînettes des pieds, les ceintures, les boîtes de senteur et les amulettes;
21 mphete ndi zipini,
Les bagues et les anneaux pour le nez;
22 zovala za pa mphwando, zipewa ndi mwinjiro, zikwama,
Les robes de fête, les larges tuniques, les manteaux, les sachets;
23 magalasi oyangʼanira, zovala zosalala, nduwira ndiponso nsalu za mʼmapewa.
Les miroirs, les chemises, les tiares et les mantilles.
24 Mʼmalo mwa kununkhira azidzanunkha, mʼmalo mwa lamba, adzavala chingwe; mʼmalo mwa tsitsi lopesa bwino, adzakhala ndi dazi; mʼmalo mwa zovala zabwino, adzavala chiguduli; mʼmalo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.
Au lieu de parfum, il y aura de l'infection; au lieu de ceintures, des cordes; au lieu de cheveux frisés, des têtes chauves; au lieu de robes flottantes, des sacs étroits; des cicatrices, au lieu de beauté.
25 Iwe Yerusalemu anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga, asilikali ako adzafera ku nkhondo.
Tes hommes tomberont par l'épée, et tes héros par la guerre.
26 Pa zipata za Ziyoni padzakhala kubuma ndi kulira; Iweyo udzasakazidwa nʼkukhala pansi, ukugubuduzika pa fumbi.
Les portes de Sion gémiront et seront dans le deuil; désolée, elle s'assiéra à terre.

< Yesaya 3 >