< Yesaya 3 >

1 Taonani tsopano, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yuda zinthu pamodzi ndi thandizo; adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse,
Car voici que le Seigneur, Yahweh des armées, va retirer de Jérusalem et de Juda toute ressource et tout appui, toute ressource de pain et toute ressource d’eau,
2 anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo, oweruza ndi aneneri, anthu olosera ndi akuluakulu,
héros et homme de guerre, juge, prophète et devin, ancien,
3 atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka, aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera.
capitaine et notable, conseiller, ouvrier expert en son art et habile enchanteur.
4 Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo; ana akhanda ndiwo adzawalamulire.
Et je leur donnerai des jeunes gens pour princes, et des enfants domineront sur eux.
5 Anthu adzazunzana, munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake. Anthu wamba adzanyoza akuluakulu.
Et le peuple se ruera homme contre homme, chacun contre son voisin; ils se précipiteront, le jeune homme contre le vieillard, et l’homme de rien contre le plus illustre.
6 Munthu adzagwira mʼbale wake mʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati, “Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu; lamulira malo opasuka ano!”
Lorsqu’un homme prendra son frère dans la maison de son père, en disant: « Tu as un manteau, sois notre chef, et que cette ruine soit sous ta garde! »
7 Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti, “Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake. Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga; musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.”
Il se récriera en ce jour-là: « Je ne veux pas être le médecin: je n’ai dans ma maison ni pain ni manteau; ne me faites pas chef du peuple. »
8 Yerusalemu akudzandira, Yuda akugwa; zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova, sakulabadira ulemerero wa Mulungu.
Car Jérusalem chancelle et Juda s’écroule, parce que leurs paroles et leurs œuvres sont contre Yahweh, pour braver le regard de sa majesté.
9 Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa; amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu; salibisa tchimo lawolo. Tsoka kwa iwo odziputira okha mavuto.
L’air de leur visage dépose contre eux; comme Sodome, ils publient leur péché et ne s’en cachent point. Malheur à eux! car ils sont eux-mêmes les auteurs de leur perte.
10 Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino, pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo.
Dites au juste qu’il est heureux, car il mangera le fruit de ses œuvres.
11 Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo! Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita.
Malheur au méchant! mal lui arrivera, car ce que ses mains ont fait lui sera rendu.
12 Achinyamata akupondereza anthu anga, ndipo amene akuwalamulira ndi akazi. Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani; akukuchotsani pa njira yanu.
Mon peuple est opprimé par des enfants, et des femmes le gouvernent. Mon peuple, ceux qui te dirigent t’égarent, et ils ruinent le chemin où tu dois passer.
13 Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu; wakonzeka kuti aweruze anthu ake.
Yahweh s’est levé pour rendre la justice, et il est debout pour juger les peuples.
14 Yehova akuwazenga milandu akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake: “Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa; nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi.
Yahweh entre en jugement avec les anciens et les princes de son peuple: « Vous avez brouté la vigne; la dépouille du pauvre est dans vos maisons.
15 Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga, nʼkudyera masuku pamutu amphawi?” Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
De quel droit foulez-vous mon peuple, et écrasez-vous la face des malheureux? » — oracle du Seigneur Yahweh des armées.
16 Yehova akunena kuti, “Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri, akuyenda atakweza makosi awo, akukopa amuna ndi maso awo akuyenda monyangʼama akuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo
Yahweh a dit: Parce que les filles de Sion sont devenues orgueilleuses, qu’elles s’avancent la tête haute, lançant des regards, qu’elles vont à petits pas, et font sonner les anneaux de leurs pieds,
17 Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo; Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.”
le Seigneur rendra chauve le crâne des filles de Sion, et Yahweh découvrira leur nudité.
18 Tsiku limenelo Ambuye adzawachotsera zodzikongoletsera zawo: za mʼmiyendo, za ku mutu za mʼkhosi,
En ce jour-là, le Seigneur enlèvera le luxe des anneaux, les soleils et les croissants;
19 ndolo ndi zibangiri, nsalu zophimba pa nkhope,
les pendants d’oreille, les bracelets et les voiles;
20 maduku, zigwinjiri za mʼmiyendo ndi malamba, mabotolo a zonunkhira ndi zithumwa,
les diadèmes, les chaînettes des pieds et les ceintures;
21 mphete ndi zipini,
les boîtes à parfum et les amulettes, les bagues et les anneaux du nez;
22 zovala za pa mphwando, zipewa ndi mwinjiro, zikwama,
les robes de fête et les larges tuniques, les manteaux et les bourses;
23 magalasi oyangʼanira, zovala zosalala, nduwira ndiponso nsalu za mʼmapewa.
les miroirs et les mousselines, les turbans et les mantilles.
24 Mʼmalo mwa kununkhira azidzanunkha, mʼmalo mwa lamba, adzavala chingwe; mʼmalo mwa tsitsi lopesa bwino, adzakhala ndi dazi; mʼmalo mwa zovala zabwino, adzavala chiguduli; mʼmalo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.
Et, au lieu de parfum, il y aura la pourriture; au lieu de ceinture, une corde; au lieu de cheveux bouclés, une tête chauve; au lieu d’une ample robe, un sac; au lieu de beauté, la marque imprimée par le feu.
25 Iwe Yerusalemu anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga, asilikali ako adzafera ku nkhondo.
Tes guerriers tomberont par l’épée, et tes héros dans la bataille.
26 Pa zipata za Ziyoni padzakhala kubuma ndi kulira; Iweyo udzasakazidwa nʼkukhala pansi, ukugubuduzika pa fumbi.
Les portes de Sion gémiront et seront dans le deuil, et, désolée, elle sera assise dans la poussière.

< Yesaya 3 >