< Yesaya 3 >

1 Taonani tsopano, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yuda zinthu pamodzi ndi thandizo; adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse,
For, behold, the Lord, Jehovah of hosts, takes away from Jerusalem and from Judah support and staff, the whole support of bread, and the whole support of water,
2 anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo, oweruza ndi aneneri, anthu olosera ndi akuluakulu,
the mighty man, and the man of war, the judge, and the prophet, and the diviner, and the elder,
3 atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka, aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera.
the captain of fifty, and the honorable man, and the counselor, and the expert craftsman, and the skilful enchanter.
4 Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo; ana akhanda ndiwo adzawalamulire.
And I will give sons to be their rulers, and babes shall rule over them.
5 Anthu adzazunzana, munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake. Anthu wamba adzanyoza akuluakulu.
And the people shall be oppressed, every one by another, and every one by his neighbor. The child shall behave himself proudly against the old man, and the base against the honorable.
6 Munthu adzagwira mʼbale wake mʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati, “Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu; lamulira malo opasuka ano!”
When a man shall take hold of his brother in the house of his father, saying, Thou have clothing, be thou our ruler, and let this ruin be under thy hand,
7 Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti, “Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake. Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga; musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.”
in that day he shall lift up his voice, saying, I will not be a healer, for in my house is neither bread nor clothing. Ye shall not make me ruler of the people.
8 Yerusalemu akudzandira, Yuda akugwa; zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova, sakulabadira ulemerero wa Mulungu.
For Jerusalem is ruined, and Judah is fallen, because their tongue and their doings are against Jehovah, to provoke the eyes of his glory.
9 Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa; amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu; salibisa tchimo lawolo. Tsoka kwa iwo odziputira okha mavuto.
The show of their countenance witnesses against them, and they declare their sin as Sodom; they do not hide it. Woe to their soul! For they have done evil to themselves.
10 Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino, pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo.
Say ye of the righteous, that it is well, for they shall eat the fruit of their doings.
11 Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo! Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita.
Woe to the wicked! It is ill with him, for what his hands have done shall be done to him.
12 Achinyamata akupondereza anthu anga, ndipo amene akuwalamulira ndi akazi. Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani; akukuchotsani pa njira yanu.
As for my people, children are their oppressors, and women rule over them. O my people, those who lead thee cause thee to err, and destroy the way of thy paths.
13 Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu; wakonzeka kuti aweruze anthu ake.
Jehovah stands up to contend, and stands to judge the peoples.
14 Yehova akuwazenga milandu akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake: “Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa; nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi.
Jehovah will enter into judgment with the elders of his people, and the rulers of it. It is ye who have eaten up the vineyard; the spoil of a poor man is in your houses.
15 Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga, nʼkudyera masuku pamutu amphawi?” Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
What do ye mean that ye crush my people, and grind the face of the poor? says the Lord, Jehovah of hosts.
16 Yehova akunena kuti, “Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri, akuyenda atakweza makosi awo, akukopa amuna ndi maso awo akuyenda monyangʼama akuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo
Moreover Jehovah said, Because the daughters of Zion are haughty, and walk with outstretched necks and wanton eyes, walking and mincing as they go, and making a tinkling with their feet,
17 Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo; Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.”
therefore the Lord will smite with a scab the crown of the head of the daughters of Zion, and Jehovah will lay bare their secret parts.
18 Tsiku limenelo Ambuye adzawachotsera zodzikongoletsera zawo: za mʼmiyendo, za ku mutu za mʼkhosi,
In that day the Lord will take away the beauty of their anklets, and the hair nets, and the crescents,
19 ndolo ndi zibangiri, nsalu zophimba pa nkhope,
the pendants, and the bracelets, and the mufflers,
20 maduku, zigwinjiri za mʼmiyendo ndi malamba, mabotolo a zonunkhira ndi zithumwa,
the bonnets, and the ankle chains, and the sashes, and the perfume-boxes, and the amulets,
21 mphete ndi zipini,
the rings, and the nose-jewels,
22 zovala za pa mphwando, zipewa ndi mwinjiro, zikwama,
the festival robes, and the mantles, and the shawls, and the satchels,
23 magalasi oyangʼanira, zovala zosalala, nduwira ndiponso nsalu za mʼmapewa.
the hand-mirrors, and the fine linen, and the turbans, and the veils.
24 Mʼmalo mwa kununkhira azidzanunkha, mʼmalo mwa lamba, adzavala chingwe; mʼmalo mwa tsitsi lopesa bwino, adzakhala ndi dazi; mʼmalo mwa zovala zabwino, adzavala chiguduli; mʼmalo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.
And it shall come to pass, that instead of sweet spices there shall be rottenness, and instead of a girdle, a rope, and instead of well set hair, baldness, and instead of a robe, a girding of sackcloth, branding instead of beauty.
25 Iwe Yerusalemu anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga, asilikali ako adzafera ku nkhondo.
Thy men shall fall by the sword, and thy mighty in the war.
26 Pa zipata za Ziyoni padzakhala kubuma ndi kulira; Iweyo udzasakazidwa nʼkukhala pansi, ukugubuduzika pa fumbi.
And her gates shall lament and mourn, and she shall be desolate and sit upon the ground.

< Yesaya 3 >