< Yesaya 3 >

1 Taonani tsopano, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yuda zinthu pamodzi ndi thandizo; adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse,
Thi se, HERREN, Hærskarers HERRE, fratager Jerusalem og Juda støtte og Stav, hver Støtte af Brød og hver støtte af vand:
2 anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo, oweruza ndi aneneri, anthu olosera ndi akuluakulu,
Helt og Krigsmand, Dommer og Profet, Spåmand og Ældste,
3 atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka, aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera.
Halvhundredfører og Stormand, Rådsherre og, Håndværksmester og den, der er kyndig i Trolddom.
4 Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo; ana akhanda ndiwo adzawalamulire.
Jeg giver dem Drenge til Øverster, Drengekådhed skal herske over dem.
5 Anthu adzazunzana, munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake. Anthu wamba adzanyoza akuluakulu.
I Folket undertrykker den ene den anden, hver sin Næste; Dreng sætter sig op imod Olding, Usling mod Hædersmand.
6 Munthu adzagwira mʼbale wake mʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati, “Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu; lamulira malo opasuka ano!”
Når da en Mand tager fat på en anden i hans Fædrenehus og siger: "Du har en Kappe, du skal være vor Hersker, under dig skal dette faldefærdige Rige stå!"
7 Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti, “Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake. Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga; musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.”
så svarer han på hin Dag: "Jeg vil ikke være Sårlæge! Jeg har hverken Brød eller Klæder i Huset, gør ikke mig til Folkets Overhoved!"
8 Yerusalemu akudzandira, Yuda akugwa; zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova, sakulabadira ulemerero wa Mulungu.
Thi Jerusalem snubler, og Juda falder, fordi de med Tunge og Gerning er mod HERREN i Trods mod hans Herligheds Øjne.
9 Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa; amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu; salibisa tchimo lawolo. Tsoka kwa iwo odziputira okha mavuto.
Deres Ansigtsudtryk vidner imod dem; de kundgør deres Synd som Sodoma, dølger intet. Ve deres Sjæl, de styrted sig selv i Våde.
10 Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino, pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo.
Salige de retfærdige, dem går det godt, deres Gerningers frugt skal de nyde;
11 Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo! Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita.
ve den gudløse, ham går det ilde; han får, som hans Hænder har gjort.
12 Achinyamata akupondereza anthu anga, ndipo amene akuwalamulira ndi akazi. Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani; akukuchotsani pa njira yanu.
Mit, Folk har en Dreng ved Styret, og over det hersker Kvinder. Dine Ledere, mit Folk, leder, vild, gør Vejen, du, vandrer, vildsom.
13 Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu; wakonzeka kuti aweruze anthu ake.
Til Rettergang er HERREN trådt frem, han tår og vil dømme sit Folk.
14 Yehova akuwazenga milandu akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake: “Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa; nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi.
HERREN møder til Doms med de Ældste i sit Folk og dets Fyrster: "Det er jer, som gnaved Vingården af, I har Rov fra den arme til Huse.
15 Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga, nʼkudyera masuku pamutu amphawi?” Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
Hvor kan I træde på mit Folk og male de arme sønder?" så lyder det fra Herren, Hærskarers HERRE.
16 Yehova akunena kuti, “Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri, akuyenda atakweza makosi awo, akukopa amuna ndi maso awo akuyenda monyangʼama akuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo
HERREN siger: Eftersom Zions Døtre bryster sig og går med knejsende Nakke og kælne Blikke, går med trippende Gang og med raslende Ankelkæder -
17 Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo; Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.”
gør Herren issen skaldet på Zions Døtre og blotter deres Tindingers Lokker.
18 Tsiku limenelo Ambuye adzawachotsera zodzikongoletsera zawo: za mʼmiyendo, za ku mutu za mʼkhosi,
På hin Dag afriver Herren al deres Pynt: Ankelringe, Pandebånd, Halvmåner,
19 ndolo ndi zibangiri, nsalu zophimba pa nkhope,
Perler, Armbånd, Flor,
20 maduku, zigwinjiri za mʼmiyendo ndi malamba, mabotolo a zonunkhira ndi zithumwa,
Hovedsmykker, Ankelkæder, Bælter, Lugtedåser, Trylleringe,
21 mphete ndi zipini,
Fingerringe, Næseringe,
22 zovala za pa mphwando, zipewa ndi mwinjiro, zikwama,
Festklæder, Underdragter, Sjaler, Tasker,
23 magalasi oyangʼanira, zovala zosalala, nduwira ndiponso nsalu za mʼmapewa.
Spejle, Lin, Hovedbånd og Slør.
24 Mʼmalo mwa kununkhira azidzanunkha, mʼmalo mwa lamba, adzavala chingwe; mʼmalo mwa tsitsi lopesa bwino, adzakhala ndi dazi; mʼmalo mwa zovala zabwino, adzavala chiguduli; mʼmalo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.
For Vellugt kommer der Stank, i Stedet for Bælte Reb, for Fletninger skaldet Isse, for Stadsklæder Sæk om Hofte, for Skønhedsmærke Brændemærke.
25 Iwe Yerusalemu anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga, asilikali ako adzafera ku nkhondo.
Dine Mænd skal falde for Sværd, dit unge Mandskab i Strid.
26 Pa zipata za Ziyoni padzakhala kubuma ndi kulira; Iweyo udzasakazidwa nʼkukhala pansi, ukugubuduzika pa fumbi.
Hendes Porte skal sukke og klage og hun sidde ensom på Jorden.

< Yesaya 3 >