< Yesaya 29 >
1 Tsoka kwa iwe, Arieli, Arieli, mzinda umene Davide anakhazikitsamo zithando za nkhondo! Papite chaka chimodzi kapena ziwiri ndipo masiku a zikondwerero zanu azipitirirabe ndithu.
Горе Аріїлу, Аріїлу, місту, що Давид у нім таборува́в! Рік до року додайте, хай свя́та закі́нчать свій круг!
2 Komatu Ine ndidzathira nkhondo Arieli ndipo kudzakhala kulira ndi kudandaula, mzindawo udzasanduka ngati ngʼanjo ya guwa lansembe.
І прити́сну Аріїла, і станеться ле́мент та плач, і він стане на мене, як о́гнище Боже.
3 Ine ndidzamanga misasa ya nkhondo kulimbana ndi mzindawo; ndidzakuzungulira ndi nsanja za nkhondo ndi kumanga mitumbira yanga ya nkhondo kulimbana nawe.
І ота́борюся проти тебе навко́ло, і сторо́жею сти́сну тебе, і ба́шти поставлю на тебе.
4 Utagwetsedwa pansi, iwe udzayankhula kuchokera mʼnthaka, mawu ako adzatuluka uli mʼfumbi, adzamveka ngati a mzukwa. Mawu ako adzamveka ngati onongʼona kuchokera mʼfumbi.
І ти будеш пони́жений, і будеш з землі говорити, і приглу́шено буде звучати твоє слово. І стане твій голос з землі, мов померлого дух, і шепоті́тиме з пороху слово твоє.
5 Koma chigulu cha adani ako chidzasanduka chifwirimbwiti. Chigulu cha ankhondo achilendo chidzabalalika ngati mungu wowuluzika ndi mphepo. Mwadzidzidzi ndi mosayembekezereka,
І буде юрба́ ворогів твоїх, мов тонкий пил, юрба ж насильників — мов поло́ва зникли́ва, і це станеться нагло, рапто́вно.
6 Yehova Wamphamvuzonse adzabwera ndi mabingu ndi chivomerezi ndi phokoso lalikulu, kamvuluvulu ndi namondwe ndi malawi a moto wonyeketsa.
Господь Саваот тебе громом та трусом наві́дає, і шумом великим, вихром та бурею, та огняни́м їдким по́лум'ям.
7 Tsono chigulu chankhondo cha mitundu ina yonse chimene chikulimbana ndi mzinda wa Arieli nʼkumathira nkhondo mzindawo, malinga ake ndi kuwuzinga, chigulu chonsecho chidzazimirira ngati maloto, gati zinthu zoziona mʼmasomphenya usiku.
І буде, як сон, як виді́ння нічне́ та юрба́ всіх народів, що на Аріїла воюють, і всі, хто воює на нього, і проти тверди́ні його, і хто йому докучає.
8 Chidzakhala ngati munthu wanjala wolota akudya, koma podzuka ali nayobe njala; kapena ngati munthu waludzu wolota akumwa, koma podzuka, ali nalobe ludzu, kummero kwake kuli gwaa. Izi zidzachitika pamene chigulu cha nkhondo cha mitundu ina yonse chikunthira nkhondo Phiri la Ziyoni.
І буде, мов бачить голодний у сні, ніби їсть, а прокинеться він — і порожня душа його, і мов спра́гнений бачить у сні, ніби п'є, а прокинеться він — і ось змучений, а душа його спра́гнена! Та́к буде на́товпові всіх наро́дів, що пі́дуть війною на го́ру Сіон.
9 Pitirizani kuledzera ndipo mudzakhala opusa. Dzitsekeni mʼmaso ndipo mukhale osapenya, ledzerani, koma osati ndi vinyo, dzandirani, koma osati ndi mowa.
Одубі́йте й дивуйтесь, заліпіть собі очі й ослі́пніть! Вони повпива́лися, та не вином, захитались, та не від п'янко́го напо́ю,
10 Yehova wakugonetsani tulo tofa nato. Watseka maso anu, inu aneneri; waphimba mitu yanu, inu alosi.
бо вилив Господь на вас духа глибокого сну та закрив ваші очі, затьма́рив пророків і ваших голів та прови́дців!
11 Kwa inu mawu onsewa ali ngati buku lotsekedwa, ndipo ngati lipatsidwa kwa wina wodziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde tawerengani bukuli,” iye adzati, “Sindingathe popeza ndi lomatidwa.”
І буде вам кожне видіння, немов би слова запеча́таної книжки, що дають її тому́, хто вміє читати, та кажуть: „Читай но оце“, та відказує той: „Не мо́жу, — вона ж запеча́тана“.
12 Kapena ngati lipatsidwa kwa amene sadziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde werenga bukuli,” iye adzayankha kuti, “Ine sindidziwa kuwerenga.”
І дають оту книжку тому, хто не вміє читати, та кажуть: „Читай но оце“, та відказує той: „Я не вмію читати“.
13 Ambuye akuti, “Anthu awa amandipembedza Ine ndi pakamwa pawo, ndi kundilemekeza Ine ndi milomo yawo, koma mitima yawo ili kutali ndi Ine. Kundipembedza kwawo ndi kwa chiphamaso. Amandipembedza motsata malamulo a anthu amene anaphunzitsidwa.
І промовив Господь: За те, що наро́д цей уста́ми своїми набли́жується, і губами своїми шанує Мене, але серце своє віддалив він від Мене, а страх їхній до Мене — заучена заповідь лю́дська,
14 Nʼchifukwa chakenso Ine ndidzapitirira kuwachitira ntchito zodabwitsa; nzeru za anthu anzeru zidzatha, luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
тому Я ось ізно́ву предивне вчиню́ з цим наро́дом, вчиню чудо й диво, і загине мудрість премудрих його, а розум розумних його заховається.
15 Tsoka kwa amene amayesetsa kubisira Yehova maganizo awo, amene amachita ntchito zawo mu mdima nʼkumanena kuti, “Ndani amene akundiona kapena ndani akudziwa zimene ndikuchita?”
Горе тим, що гли́боко за́дум ховають від Господа, і чиняться в те́мряві їхні діла, і що говорять вони: „Хто нас бачить, і хто про нас знає?“
16 Inu mumazondotsa zinthu ngati kuti dothi lasanduka wowumba mbiya. Kodi chinthu chopangidwa chingawuze wochipanga kuti “Sunandipange ndi iwe?” Kapena mʼphika kunena kwa amene anawuwumba kuti, “Iwe sudziwa chilichonse?”
О, ваша фальшивосте! Чи ганча́р уважається рівним до глини? Чи зро́блене скаже про майстра свого: „Він мене не зробив“, а твір про свого творця́ говоритиме: „Він не розуміє цього “?
17 Kodi Lebanoni posachedwapa sadzasanduka munda wachonde, ndipo kodi munda wachondewo ngati nkhalango?
Хіба за короткого ча́су Ліван на садка не обе́рнеться, а садок порахо́ваний буде за ліс?
18 Tsiku limenelo anthu osamva adzamva mawu a mʼbuku, ndipo anthu osaona amene ankakhala mu mdima adzapenya.
І в той день слова книжки почують глухі, а очі сліпих із темно́ти та з те́мряви бачити будуть,
19 Anthu odzichepetsa adzakhalanso ndi chimwemwe mwa Yehova; ndipo anthu osowa adzakondwa chifukwa cha Woyerayo wa Israeli.
і суми́рні побі́льшать у Господі радість свою, а люди убогі в Святому Ізраїля ті́шитись будуть!
20 Koma anthu ankhanza adzazimirira, oseka anzawo sadzaonekanso, ndipo onse okopeka ndi zoyipa adzawonongedwa.
Бо скінчи́вся наси́льник, і минувся насмі́шник, і пони́щені всі ті, хто дба́є про кривду,
21 Yehova adzalanga amene amasinjirira munthu kuti apezeke wolakwa, kapena kuphophonyetsa anthu ozenga mlandu ndi umboni wonama kuti osalakwa asaweruzidwe mwachilungamo.
хто судить люди́ну за слово одне, на того ж, хто судить у брамі, вони ставлять па́стку, і праведного випиха́ють обма́ною.
22 Choncho Yehova amene anawombola Abrahamu, akunena kwa zidzukulu za Yakobo kuti, “Anthu anga sadzachitanso manyazi; nkhope zawo sizidzagwanso ndi manyazi.
Тому́ то Господь, що викупив Авраама, сказав домові Якова так: Не буде тепер засоро́млений Яків, й обличчя його не поблі́дне тепер,
23 Akadzaona ana awo ndi ntchito ya manja anga pakati pawo, adzatamanda dzina langa loyera; adzazindikira kuyera kwa Woyerayo wa Yakobo, ndipo adzachita naye mantha Mulungu wa Israeli.
бо як він серед себе побачить діте́й своїх, чин Моїх рук, вони будуть святи́ти Моє Ймення, і посвятять Святого Якового, і будуть боятися Бога Ізраїля!
24 Anthu opusa adzapeza nzeru; onyinyirika adzalandira malangizo.”
Тоді́ то хто блу́дить у дусі, ті розум пізна́ють, а хто ре́мствує, ті поу́ки навча́ться!