< Yesaya 29 >

1 Tsoka kwa iwe, Arieli, Arieli, mzinda umene Davide anakhazikitsamo zithando za nkhondo! Papite chaka chimodzi kapena ziwiri ndipo masiku a zikondwerero zanu azipitirirabe ndithu.
Biada Aryjelowi! Aryjelowi miastu, w którem mieszkał Dawid. Przydajcie rok do roku, niechaj rzeżą barany.
2 Komatu Ine ndidzathira nkhondo Arieli ndipo kudzakhala kulira ndi kudandaula, mzindawo udzasanduka ngati ngʼanjo ya guwa lansembe.
Jednak ucisnę Aryjela, i będzie smutek i żałość, bo mi będzie jako Aryjel.
3 Ine ndidzamanga misasa ya nkhondo kulimbana ndi mzindawo; ndidzakuzungulira ndi nsanja za nkhondo ndi kumanga mitumbira yanga ya nkhondo kulimbana nawe.
Położę się zaiste obozem w około przeciwko tobie, i ścisnę cię wałami, i wystawię przeciwko tobie baszty.
4 Utagwetsedwa pansi, iwe udzayankhula kuchokera mʼnthaka, mawu ako adzatuluka uli mʼfumbi, adzamveka ngati a mzukwa. Mawu ako adzamveka ngati onongʼona kuchokera mʼfumbi.
Tedy będąc zniżone, z ziemi mówić będziesz, i z prochu szeptać będzie mowa twoja; będzie mówił głos twój, jako wieszczka z ziemi, a z prochu mowa twoja szeptać będzie.
5 Koma chigulu cha adani ako chidzasanduka chifwirimbwiti. Chigulu cha ankhondo achilendo chidzabalalika ngati mungu wowuluzika ndi mphepo. Mwadzidzidzi ndi mosayembekezereka,
Bo mnóstwo nieprzyjaciół twoich będzie jako proszku drobnego, a zgraja okrutników jako plew latających; a to się nagle w okamgnieniu stanie.
6 Yehova Wamphamvuzonse adzabwera ndi mabingu ndi chivomerezi ndi phokoso lalikulu, kamvuluvulu ndi namondwe ndi malawi a moto wonyeketsa.
Od Pana zastępów nawiedzione będzie gromem i trzęsieniem ziemi, i głosem wielkim, wichrem i burzą, i płomieniem ognia pożerającego.
7 Tsono chigulu chankhondo cha mitundu ina yonse chimene chikulimbana ndi mzinda wa Arieli nʼkumathira nkhondo mzindawo, malinga ake ndi kuwuzinga, chigulu chonsecho chidzazimirira ngati maloto, gati zinthu zoziona mʼmasomphenya usiku.
Ale jako sen widzenia nocnego, tak będzie zgraja wszystkich narodów walczących przeciwko Aryjelowi, i wszystkich bojujących przeciwko niemu i twierdzom jego, i tych, którzy go uciskają.
8 Chidzakhala ngati munthu wanjala wolota akudya, koma podzuka ali nayobe njala; kapena ngati munthu waludzu wolota akumwa, koma podzuka, ali nalobe ludzu, kummero kwake kuli gwaa. Izi zidzachitika pamene chigulu cha nkhondo cha mitundu ina yonse chikunthira nkhondo Phiri la Ziyoni.
Będzie, mówię, jako gdy się śni głodnemu, jakoby jadł; ale gdy się ocuci, alić czczy żywot jego; i jako gdy się śni pragnącemu, jakoby pił, a gdy się ocuci, alić zemdlony zostaje, a dusza jego pragnie; tak będzie zgraja wszystkich narodów walczących przeciwko górze Syońskiej.
9 Pitirizani kuledzera ndipo mudzakhala opusa. Dzitsekeni mʼmaso ndipo mukhale osapenya, ledzerani, koma osati ndi vinyo, dzandirani, koma osati ndi mowa.
Jakoż tedy odwłaczacie, choćbyście się zdumiewać mieli; rozkoszujecie, choćbyście mieli na pomoc wołać. Opili się, ale nie winem; potaczają się, ale nie od mocnego napoju.
10 Yehova wakugonetsani tulo tofa nato. Watseka maso anu, inu aneneri; waphimba mitu yanu, inu alosi.
Bo was napełnił Pan duchem snu twardego, i zawarł oczy wasze; proroków i książąt waszych najopatrzniejszych oczy zasłonił.
11 Kwa inu mawu onsewa ali ngati buku lotsekedwa, ndipo ngati lipatsidwa kwa wina wodziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde tawerengani bukuli,” iye adzati, “Sindingathe popeza ndi lomatidwa.”
Przetoż wam wszelkie widzenie podobne jest słowom ksiąg zapieczętowanych, które danoliby temu, co zna pismo, a rzeczono: Czytaj to proszę, tedy odpowie: Nie mogę, bo są zapieczętowane.
12 Kapena ngati lipatsidwa kwa amene sadziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde werenga bukuli,” iye adzayankha kuti, “Ine sindidziwa kuwerenga.”
A danoliby księgi temu, co nie zna pisma, a rzeczono: Czytaj to proszę, tedy odpowie: Nie znam pisma.
13 Ambuye akuti, “Anthu awa amandipembedza Ine ndi pakamwa pawo, ndi kundilemekeza Ine ndi milomo yawo, koma mitima yawo ili kutali ndi Ine. Kundipembedza kwawo ndi kwa chiphamaso. Amandipembedza motsata malamulo a anthu amene anaphunzitsidwa.
Bo mówi Pan: Przeto, że ten lud przybliża się do mnie usty swemi, a serce jego dalekie jest odemnie, a bojaźni, którą się mnie boją, z przykazań ludzkich nauczyli się:
14 Nʼchifukwa chakenso Ine ndidzapitirira kuwachitira ntchito zodabwitsa; nzeru za anthu anzeru zidzatha, luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
Dlatego Ja też sobie dziwnie pocznę z tym ludem, dziwnie i cudownie, i zginie mądrość mądrych jego, a rozum roztropnych jego skryje się.
15 Tsoka kwa amene amayesetsa kubisira Yehova maganizo awo, amene amachita ntchito zawo mu mdima nʼkumanena kuti, “Ndani amene akundiona kapena ndani akudziwa zimene ndikuchita?”
Biada tym, którzy głęboko przed Panem ukrywają radę! których każda sprawa dzieje się w ciemności, i mówią: Któż widzi? Kto wie o nas?
16 Inu mumazondotsa zinthu ngati kuti dothi lasanduka wowumba mbiya. Kodi chinthu chopangidwa chingawuze wochipanga kuti “Sunandipange ndi iwe?” Kapena mʼphika kunena kwa amene anawuwumba kuti, “Iwe sudziwa chilichonse?”
Przewrotne myśli wasze są jako glina garncarska. Izali rzecze robota o tym, co ją urobił: Nie urobił mię? i ulepienie izali rzecze o tym, co je ulepił: Nie rozumiał?
17 Kodi Lebanoni posachedwapa sadzasanduka munda wachonde, ndipo kodi munda wachondewo ngati nkhalango?
Izali po maluczkim i króciuchnym czasie nie obróci się Liban w pole? a pole za las poczytane nie będzie?
18 Tsiku limenelo anthu osamva adzamva mawu a mʼbuku, ndipo anthu osaona amene ankakhala mu mdima adzapenya.
I usłyszą dnia onego głusi słowa ksiąg, a z mroku i z ciemności oczy ślepych patrzać będą.
19 Anthu odzichepetsa adzakhalanso ndi chimwemwe mwa Yehova; ndipo anthu osowa adzakondwa chifukwa cha Woyerayo wa Israeli.
Ale cisi nader się rozweselą w Panu, a ubodzy ludzie rozweselą się w Świętym Izraelskim.
20 Koma anthu ankhanza adzazimirira, oseka anzawo sadzaonekanso, ndipo onse okopeka ndi zoyipa adzawonongedwa.
Gdy ustanie okrutnik, a zniszczeje naśmiewca, wykorzenieni będą wszyscy, którzy pilnowali nieprawości;
21 Yehova adzalanga amene amasinjirira munthu kuti apezeke wolakwa, kapena kuphophonyetsa anthu ozenga mlandu ndi umboni wonama kuti osalakwa asaweruzidwe mwachilungamo.
Którzy winują człowieka dla słowa, a na tego, który ich strofuje, w bramie sidła stawiają, i bez przyczyny do upadku przywodzą sprawiedliwego.
22 Choncho Yehova amene anawombola Abrahamu, akunena kwa zidzukulu za Yakobo kuti, “Anthu anga sadzachitanso manyazi; nkhope zawo sizidzagwanso ndi manyazi.
Przetoż tak mówi o domu Jakóbowym Pan, który odkupił Abrahama: Już dalej nie będzie zawstydzony Jakób, ani więcej twarz jego zblednie.
23 Akadzaona ana awo ndi ntchito ya manja anga pakati pawo, adzatamanda dzina langa loyera; adzazindikira kuyera kwa Woyerayo wa Yakobo, ndipo adzachita naye mantha Mulungu wa Israeli.
Albowiem gdy ujrzy synów swoich, dzieło rąk moich, w pośrodku siebie, poświęcających imię moje; tedy będą poświęcać Świętego Jakóbowego, a Boga Izraelskiego bać się będą.
24 Anthu opusa adzapeza nzeru; onyinyirika adzalandira malangizo.”
I staną się rozumnymi błądzący duchem, a szemracze nauczą się umiejętności.

< Yesaya 29 >