< Yesaya 29 >

1 Tsoka kwa iwe, Arieli, Arieli, mzinda umene Davide anakhazikitsamo zithando za nkhondo! Papite chaka chimodzi kapena ziwiri ndipo masiku a zikondwerero zanu azipitirirabe ndithu.
Malheur à Ariel, à Ariel, à la cité où David a dressé sa tente! Ajoutez année à année, que les solennités parcourent leur cycle,
2 Komatu Ine ndidzathira nkhondo Arieli ndipo kudzakhala kulira ndi kudandaula, mzindawo udzasanduka ngati ngʼanjo ya guwa lansembe.
et je serrerai de près Ariel, et il n’y aura que plaintes et gémissements! Mais elle sera pour moi comme Ariel
3 Ine ndidzamanga misasa ya nkhondo kulimbana ndi mzindawo; ndidzakuzungulira ndi nsanja za nkhondo ndi kumanga mitumbira yanga ya nkhondo kulimbana nawe.
je camperai tout autour de toi, je t’environnerai de postes armés, et j’établirai contre toi des retranchements.
4 Utagwetsedwa pansi, iwe udzayankhula kuchokera mʼnthaka, mawu ako adzatuluka uli mʼfumbi, adzamveka ngati a mzukwa. Mawu ako adzamveka ngati onongʼona kuchokera mʼfumbi.
Tu seras abaissée; c’est de la terre que s’élèvera ta voix, et de la poussière que se feront entendre tes sourds accents; ta voix sortira de terre, comme celle d’un spectre, et ta parole montera de la poussière comme un murmure. —
5 Koma chigulu cha adani ako chidzasanduka chifwirimbwiti. Chigulu cha ankhondo achilendo chidzabalalika ngati mungu wowuluzika ndi mphepo. Mwadzidzidzi ndi mosayembekezereka,
Et la multitude de tes ennemis sera comme une fine poussière, et la multitude des guerriers comme la paille qui s’envole.
6 Yehova Wamphamvuzonse adzabwera ndi mabingu ndi chivomerezi ndi phokoso lalikulu, kamvuluvulu ndi namondwe ndi malawi a moto wonyeketsa.
Et il arrivera que soudain, en un instant, tu seras visitée, par Yahweh des armées avec fracas, tonnerre et grand bruit, tourbillon, tempête et flamme de feu dévorant.
7 Tsono chigulu chankhondo cha mitundu ina yonse chimene chikulimbana ndi mzinda wa Arieli nʼkumathira nkhondo mzindawo, malinga ake ndi kuwuzinga, chigulu chonsecho chidzazimirira ngati maloto, gati zinthu zoziona mʼmasomphenya usiku.
Et il en sera comme d’un songe, vision de la nuit, de la multitude de toutes les nations qui combattront contre Ariel, et de tous ceux qui combattront contre elle et sa forteresse et la serreront de près.
8 Chidzakhala ngati munthu wanjala wolota akudya, koma podzuka ali nayobe njala; kapena ngati munthu waludzu wolota akumwa, koma podzuka, ali nalobe ludzu, kummero kwake kuli gwaa. Izi zidzachitika pamene chigulu cha nkhondo cha mitundu ina yonse chikunthira nkhondo Phiri la Ziyoni.
Comme celui qui a faim rêve qu’il mange, et, à son réveil, son âme est vide; et comme un homme qui a soif rêve qu’il boit, et, à son réveil, il est épuisé et toujours altéré; ainsi il en sera de la multitude de toutes les nations, qui marchent contre la montagne de Sion.
9 Pitirizani kuledzera ndipo mudzakhala opusa. Dzitsekeni mʼmaso ndipo mukhale osapenya, ledzerani, koma osati ndi vinyo, dzandirani, koma osati ndi mowa.
Etonnez-vous et soyez dans la stupeur! Aveuglez-vous et soyez aveuglés! Ils sont ivres, mais pas de vin; ils chancellent, mais pas de liqueurs fortes.
10 Yehova wakugonetsani tulo tofa nato. Watseka maso anu, inu aneneri; waphimba mitu yanu, inu alosi.
Car Yahweh a répandu sur vous un esprit de léthargie; il a fermé vos yeux — les prophètes; il a jeté un voile sur vos têtes — les voyants.
11 Kwa inu mawu onsewa ali ngati buku lotsekedwa, ndipo ngati lipatsidwa kwa wina wodziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde tawerengani bukuli,” iye adzati, “Sindingathe popeza ndi lomatidwa.”
Et toute vision est devenue pour vous comme les paroles d’un livre scellé. On le présente à un homme qui sait lire, en disant: « Lis cela! » et il dit: « Je ne puis, car ce livre est scellé. »
12 Kapena ngati lipatsidwa kwa amene sadziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde werenga bukuli,” iye adzayankha kuti, “Ine sindidziwa kuwerenga.”
On le présente à un homme qui ne sait pas lire, en disant: « Lis cela! » et il dit: « Je ne sais pas lire. »
13 Ambuye akuti, “Anthu awa amandipembedza Ine ndi pakamwa pawo, ndi kundilemekeza Ine ndi milomo yawo, koma mitima yawo ili kutali ndi Ine. Kundipembedza kwawo ndi kwa chiphamaso. Amandipembedza motsata malamulo a anthu amene anaphunzitsidwa.
Le Seigneur dit: Puisque ce peuple s’approche en paroles et m’honore des lèvres, tandis qu’il tient son cœur éloigné de moi, et que le culte qu’il me rend est un précepte appris des hommes,
14 Nʼchifukwa chakenso Ine ndidzapitirira kuwachitira ntchito zodabwitsa; nzeru za anthu anzeru zidzatha, luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
à cause de cela, je continuerai à user de prodiges, avec ce peuple, de prodiges étranges. Et la sagesse de ses sages périra, et l’intelligence de ses docteurs s’obscurcira.
15 Tsoka kwa amene amayesetsa kubisira Yehova maganizo awo, amene amachita ntchito zawo mu mdima nʼkumanena kuti, “Ndani amene akundiona kapena ndani akudziwa zimene ndikuchita?”
Malheur à ceux qui cachent profondément à Yahweh le secret de leurs desseins, dont l’œuvre s’accomplit dans les ténèbres, et qui disent: « Qui nous voit, qui nous connaît? »
16 Inu mumazondotsa zinthu ngati kuti dothi lasanduka wowumba mbiya. Kodi chinthu chopangidwa chingawuze wochipanga kuti “Sunandipange ndi iwe?” Kapena mʼphika kunena kwa amene anawuwumba kuti, “Iwe sudziwa chilichonse?”
Quelle folie! Le potier sera-t-il donc estimé pour de l’argile, que l’œuvre dise de l’ouvrier: « Il ne m’a pas faite; » et que le vase dise du potier: « Il n’y entend rien? »
17 Kodi Lebanoni posachedwapa sadzasanduka munda wachonde, ndipo kodi munda wachondewo ngati nkhalango?
Est-ce que dans un peu de temps, le Liban ne sera pas changé en verger, et le verger ne sera pas réputé une forêt?
18 Tsiku limenelo anthu osamva adzamva mawu a mʼbuku, ndipo anthu osaona amene ankakhala mu mdima adzapenya.
En ce jour-là, les sourds entendront les paroles du livre, et, sortant des ténèbres et de l’obscurité, les aveugles verront.
19 Anthu odzichepetsa adzakhalanso ndi chimwemwe mwa Yehova; ndipo anthu osowa adzakondwa chifukwa cha Woyerayo wa Israeli.
Les humbles se réjouiront de plus en plus en Yahweh, et les plus pauvres tressailliront dans le Saint d’Israël.
20 Koma anthu ankhanza adzazimirira, oseka anzawo sadzaonekanso, ndipo onse okopeka ndi zoyipa adzawonongedwa.
Car l’oppresseur aura disparu, et le moqueur aura péri, et tous ceux qui méditent l’iniquité seront exterminés,
21 Yehova adzalanga amene amasinjirira munthu kuti apezeke wolakwa, kapena kuphophonyetsa anthu ozenga mlandu ndi umboni wonama kuti osalakwa asaweruzidwe mwachilungamo.
ceux qui condamnent un homme pour un mot, qui tendent des pièges à celui qui les confond à la porte, et qui perdent le juste par leurs mensonges.
22 Choncho Yehova amene anawombola Abrahamu, akunena kwa zidzukulu za Yakobo kuti, “Anthu anga sadzachitanso manyazi; nkhope zawo sizidzagwanso ndi manyazi.
C’est pourquoi ainsi parle Yahweh à la maison de Jacob, lui qui a racheté Abraham: Jacob n’aura plus désormais à rougir, et son front désormais ne pâlira plus.
23 Akadzaona ana awo ndi ntchito ya manja anga pakati pawo, adzatamanda dzina langa loyera; adzazindikira kuyera kwa Woyerayo wa Yakobo, ndipo adzachita naye mantha Mulungu wa Israeli.
Car, lorsqu’il verra, lui et ses enfants, l’œuvre de mes mains au milieu d’eux, ils sanctifieront mon nom, ils sanctifieront le Saint de Jacob, et ils révéreront le Dieu d’Israël.
24 Anthu opusa adzapeza nzeru; onyinyirika adzalandira malangizo.”
Ceux qui avaient l’esprit égaré apprendront la sagesse, et ceux qui murmuraient recevront l’instruction.

< Yesaya 29 >