< Yesaya 28 >
1 Tsoka ufumu wonyada wa zidakwa za ku Efereimu. Tsoka kwa ulemerero wake wokongola umene ukufota ngati duwa limene lili pa mutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde.
Malheur à la couronne d’orgueil, aux hommes ivres d’Ephraïm, à la fleur qui tombe, à la gloire de son exultation, à ceux qui étaient au haut de la vallée très grasse, chancelant par le vin.
2 Taonani, ambuye ali naye wina wamphamvu ndi nyonga. Iye adzabwera ngati mkuntho wamatalala ndi namondwe wowononga, ngati madzi amphamvu osefukira a mvula yamkuntho; ndipo adzawagwetsa pansi mwankhanza.
Voici que le Seigneur fort et puissant sera comme l’impétuosité de la grêle, comme un tourbillon qui brise, comme l’impétuosité des grandes eaux inondantes, et lâchées sur une terre spacieuse.
3 Ulamuliro wa atsogoleri oledzera a ku Efereimu adzawuthetsa.
Aux pieds sera foulée la couronne d’orgueil des hommes ivres d’Ephraïm.
4 Ndipo ulemerero wokongola wa mzinda umene uli ngati duwa lofota pamutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde uja, udzakhala ngati nkhuyu yoyambirira kupsa imene munthu akangoyiona amayithyola nthawi yokolola isanakwane.
Et elle tombera, la fleur de la gloire et de l’exultation de celui qui est au haut des vallées grasses, comme le fruit venant à temps avant l’automne; dès que quelqu’un le voyant l’aura regardé et pris de sa main, il le dévorera.
5 Tsiku limenelo Yehova Wamphamvuzonse adzakhala ngati nkhata yaufumu, chipewa chokongola kwa anthu ake otsala.
En ce jour-là, le Seigneur des armées sera une couronne de gloire, et un bouquet d’exultation pour le reste de son peuple;
6 Iye adzapereka mtima wachilungamo kwa oweruza, adzakhala chilimbikitso kwa amene amabweza adani pa zipata za mzinda.
Et un esprit de jugement pour celui qui sera assis sur le tribunal du jugement, et une force pour ceux qui retourneront de la guerre à la porte de la ville.
7 Nawonso awa ali dzandidzandi chifukwa cha vinyo ndipo akusochera chifukwa cha mowa: ansembe ndi aneneri akudzandira chifukwa cha mowa ndipo akusokonezeka chifukwa cha vinyo; akusochera chifukwa cha mowa, akudzandira pamene akuona masomphenya, kupunthwa pamene akupereka chigamulo.
Mais ceux-ci même ont manqué de connaissance par le vin, et par l’ivresse ils ont chancelé; le prêtre et le prophète ont manqué de connaissance par l’ivresse; absorbés par le vin, ils ont chancelé dans l’ivresse, ils n’ont pas connu le voyant, ils ont ignoré la justice.
8 Pa matebulo onse pali masanzi okhaokha ndipo palibenso malo wopanda zonyansa.
Car toutes les tables ont été remplies de vomissement et d’ordures, en sorte qu’il n’y avait plus un lieu sans souillure.
9 Iwo akuti, “Kodi munthu ameneyu akufuna aphunzitse ndani? Uthengawu akufuna kufotokozera yani? Ndi kwa ana amene aleka kuyamwa, kwa makanda ongowachotsa kumene ku bere?
À qui enseignera-t-il la science? à qui fera-t-il comprendre ce qui aura été entendu? à des enfants qu’on vient de sevrer, d’arracher aux mamelles.
10 Akuyesa kumatiphunzitsa pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Zonsezi akungoti apa pangʼono apa pangʼono.”
Parce qu’ils disent: Commande, commande encore, commande, commande encore, attends, attends encore, attends, attends encore, un peu là, un peu là.
11 Mulungu adzayankhula kwa anthu ake kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo, ziyankhulo zosamveka bwino. Mulungu adzayankhula kwa anthu awa, amene
Car dans un autre langage de lèvres et une autre langue, il parlera à ce peuple,
12 anakuwuzani kuti, “Malo opumulira ndi ano, otopa apumule, malo owusira ndi ano.” Koma inu simunamvere.
Auquel il avait dit: Voici mon repos, soulagez celui qui est fatigué, et voici mon rafraîchissement; et ils n’ont pas voulu entendre.
13 Choncho Yehova adzakuphunzitsani pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Kotero mudzayenda ndi kugwa chambuyo, adzapweteka ndi kukodwa mu msampha ndipo adzakutengani ku ukapolo.
Et telle sera la parole que le Seigneur leur adressera: Commande, commande encore, commande, commande encore, attends, attends encore, attends, attends encore, un peu là, un peu là; afin qu’ils aillent, et qu’ils tombent en arrière, et qu’ils soient brisés, qu’ils donnent dans le piège et qu’ils y soient pris.
14 Nʼchifukwa chake imvani mawu a Yehova, inu anthu achipongwe amene mumalamulira anthu awa mu Yerusalemu.
À cause de cela, écoutez la parole du Seigneur, hommes railleurs qui dominez sur mon peuple qui est à Jérusalem.
15 Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa, ife tachita mgwirizano ndi manda. Pamene mliri woopsa ukadzafika sudzatikhudza ife, chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.” (Sheol )
Car vous avez dit: Nous avons contracté une alliance avec la mort, et avec l’enfer nous avons fait un pacte. Le fléau débordant, lorsqu’il passera, ne viendra pas sur nous; parce que nous avons établi le mensonge notre espérance, et que par le mensonge nous avons été protégés. (Sheol )
16 Tsono zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi: “Taonani, ndikuyika mwala wovomerezeka ndi amisiri ngati maziko mu Ziyoni, mwala wapangodya, wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu; munthu amene awukhulupirira sadzagwedezeka.
C’est pourquoi le Seigneur Dieu dit ceci: Voici que moi je poserai dans les fondements de Sion une pierre, une pierre éprouvée, angulaire, précieuse, enfoncée dans le fondement; que celui qui croit, ne se hâte pas.
17 Ntchito zolungama zidzakhala ngati chingwe choyezera maziko ake, ndipo chilungamo chidzakhala chowongolera mzere; matalala adzawononga malo anu othawirapo, amene ndi mabodza, ndipo madzi adzamiza malo anu obisalako.
Et j’établirai avec un poids le jugement, et la justice avec mesure; et la grêle détruira l’espérance du mensonge; et la protection, les eaux l’inonderont.
18 Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa; mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa. Pakuti mliri woopsa udzafika, ndipo udzakugonjetsani. (Sheol )
Et votre alliance avec la mort sera détruite, votre pacte avec l’enfer ne subsistera pas; quant au fléau débordant, lorsqu’il passera, vous en serez accablés. (Sheol )
19 Ndipo ukadzangofika udzakutengani. Udzafika mmawa uliwonse, usiku ndi usana.” Anthu akadzamvetsetsa uthenga umenewu adzaopsedwa kwambiri.
Toutes les fois qu’il passera, il vous emportera; puisque dès le matin à l’aube, il passera pendant le jour et pendant la nuit; et il n’y aura seulement que le tourment qui donnera l’intelligence à l’ouïe.
20 Mudzakhala ngati munthu wogona pa bedi lalifupi kwambiri kuti sangathe kutambalitsapo miyendo; ndiponso mudzakhala ngati munthu amene wafunda bulangeti lochepa kwambiri kuti sangathe nʼkufunda komwe.
Car la couche a été resserrée, de manière que si deux s’y placent, l’un tombera; et la couverture étroite ne peut les couvrir l’un et l’autre.
21 Yehova adzamenya nkhondo monga anachitira ku phiri la Perazimu adzakalipa monga anachitira ku chigwa cha Gibiyoni; adzagwira ntchito yake yooneka ngati yachilendo, ndipo zimene ati adzachite zidzakhala ngati zodabwitsa.
Car comme sur la montagne des divisions, le Seigneur se lèvera; comme dans la vallée qui est en Gabaon, il se mettra en colère; afin de faire son œuvre, son œuvre étrangère; afin d’opérer son œuvre, son œuvre qui lui est est étrangère.
22 Tsopano lekani kunyoza, mukapanda kutero maunyolo anu adzakuthinani kwambiri; Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse wandiwuza kuti, “Ndagamula kuti ndidzawononga dziko lapansi.”
Et maintenant ne vous jouez point, de peur que vos liens ne se resserrent; car j’ai appris du Seigneur Dieu des armées la destruction et le retranchement qu’il va faire sur la terre tout entière.
23 Tcherani khutu ndipo mumve mawu anga; mvetserani ndipo mumve zimene ndikunena.
Prêtez l’oreille, et écoutez ma voix; soyez attentifs, et écoutez ma parole.
24 Kodi mlimi wofuna kudzala mbewu amangokhalira kutipula kokhakokha? Kodi amangokhalira kugawula ndi kugalawuza kokhakokha?
Est-ce que pendant tout le jour, le laboureur labourera afin de semer; fendra-t-il les mottes, et sarclera-t-il sa terre?
25 Pamene iye wasalaza mundawo, kodi samafesa mawere ndi chitowe? Kodi suja samadzala tirigu ndi barele mʼmizere yake, nadzala mchewere mʼphepete mwa mundawo?
Est-ce que, lorsqu’il en aura égalisé la surface, il ne sèmera pas de la nigelle et il ne répandra pas du cumin, et il ne mettra pas du blé par rangée, et de l’orge, et du millet, et de la vesce dans ses confins?
26 Mulungu wake amamulangiza ndi kumuphunzitsa njira yabwino.
Et son Dieu lui donnera le discernement; son Dieu l’instruira.
27 Mawere sapunthira chopunthira cha galeta lopanda mikombero, kapena chitowe sapuntha popondetsapo mikombero ya galeta; mawere amapuntha ndi ndodo ndipo chitowe amapuntha ndi kamtengo.
Car la nigelle ne sera pas triturée avec des traîneaux à pointes de fer, ni la roue du chariot ne circulera sur le cumin; mais avec une verge on battra la nigelle, et le cumin avec un fléau.
28 Tirigu ayenera kusinjidwa kuti apangire buledi, komabe munthu samangokhalira kupuntha tiriguyo osalekeza, kuopa kuti angatekedzeke. Ngakhale kuti amapuntha tiriguyo poyendetsapo mikombero ya galeta, koma akavalo ake satekedza tiriguyo.
Mais le pain sera brisé; cependant ce ne sera pas à perpétuité que celui qui le triture le triturera, et que la roue du chariot le pressera, et qu’avec ses ongles il le brisera.
29 Izinso zimachokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, wa uphungu wodabwitsa ndi wa nzeru zopambana.
Ceci est venu du Seigneur Dieu des armées, pour faire admirer ses conseils et signaler sa justice.