< Yesaya 28 >

1 Tsoka ufumu wonyada wa zidakwa za ku Efereimu. Tsoka kwa ulemerero wake wokongola umene ukufota ngati duwa limene lili pa mutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde.
Malheur à la couronne d'orgueil, ô mercenaires d'Éphraïm; fleur qui tombe de sa gloire sur la cime de la montagne fertile; hommes ivres sans vin.
2 Taonani, ambuye ali naye wina wamphamvu ndi nyonga. Iye adzabwera ngati mkuntho wamatalala ndi namondwe wowononga, ngati madzi amphamvu osefukira a mvula yamkuntho; ndipo adzawagwetsa pansi mwankhanza.
Voilà que la colère du Seigneur est violente et terrible, comme la grêle tombant où il n'y a point d'abri, tombant avec force comme une inondation qui ravage une campagne; il donnera le repos à la terre. Sous les mains
3 Ulamuliro wa atsogoleri oledzera a ku Efereimu adzawuthetsa.
Et les pieds sera foulée votre couronne d'orgueil, ô mercenaires d'Éphraïm!
4 Ndipo ulemerero wokongola wa mzinda umene uli ngati duwa lofota pamutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde uja, udzakhala ngati nkhuyu yoyambirira kupsa imene munthu akangoyiona amayithyola nthawi yokolola isanakwane.
Et la fleur détachée de l'espérance de votre gloire, sur la cime de la haute montagne, sera comme le premier fruit mûr du figuier; celui qui l'aura vu, avant que sa main l'ait saisi, désirera le dévorer.
5 Tsiku limenelo Yehova Wamphamvuzonse adzakhala ngati nkhata yaufumu, chipewa chokongola kwa anthu ake otsala.
Ce jour-là, le Seigneur Dieu des armées sera une couronne d'espérance, et comme une guirlande de gloire, pour le reste de son peuple.
6 Iye adzapereka mtima wachilungamo kwa oweruza, adzakhala chilimbikitso kwa amene amabweza adani pa zipata za mzinda.
Ils seront restés en esprit de justice pour rendre la justice, et détruire les forces de ceux qui les entravent.
7 Nawonso awa ali dzandidzandi chifukwa cha vinyo ndipo akusochera chifukwa cha mowa: ansembe ndi aneneri akudzandira chifukwa cha mowa ndipo akusokonezeka chifukwa cha vinyo; akusochera chifukwa cha mowa, akudzandira pamene akuona masomphenya, kupunthwa pamene akupereka chigamulo.
Car ils ont été entraînés au péché par le vin; ils ont été égarés par les boissons fermentées; prêtres et prophètes ont perdu le sens, à cause des boissons fermentées; ils ont été absorbés par le vin; ils ont chancelé dans l'ivresse, ils ont erré: telle est ma vision.
8 Pa matebulo onse pali masanzi okhaokha ndipo palibenso malo wopanda zonyansa.
La malédiction consumera leurs conseils; car leurs conseils sont nés de la cupidité.
9 Iwo akuti, “Kodi munthu ameneyu akufuna aphunzitse ndani? Uthengawu akufuna kufotokozera yani? Ndi kwa ana amene aleka kuyamwa, kwa makanda ongowachotsa kumene ku bere?
A qui avons-nous prédit ces maux? à qui avons-nous porté ce message? A vous qui venez d'être sevrés, vous qu'on vient de retirer de la mamelle.
10 Akuyesa kumatiphunzitsa pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Zonsezi akungoti apa pangʼono apa pangʼono.”
Attendez affliction sur affliction, espérance sur espérance; encore un peu de temps, encore un peu de temps.
11 Mulungu adzayankhula kwa anthu ake kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo, ziyankhulo zosamveka bwino. Mulungu adzayankhula kwa anthu awa, amene
Avec des lèvres dédaigneuses, en une langue étrangère, Dieu parlera à ce peuple.
12 anakuwuzani kuti, “Malo opumulira ndi ano, otopa apumule, malo owusira ndi ano.” Koma inu simunamvere.
Il lui dira: Voici le repos de celui qui a faim, et voilà son affliction; et ils n'ont pas voulu écouter.
13 Choncho Yehova adzakuphunzitsani pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Kotero mudzayenda ndi kugwa chambuyo, adzapweteka ndi kukodwa mu msampha ndipo adzakutengani ku ukapolo.
Et la prédiction du Seigneur sera pour eux: affliction sur affliction, espérance sur espérance; encore un peu de temps, encore un peu de temps; afin qu'ils partent, et qu'ils tombent à la renverse; et ils seront broyés, et ils seront pris au piège, et ils périront.
14 Nʼchifukwa chake imvani mawu a Yehova, inu anthu achipongwe amene mumalamulira anthu awa mu Yerusalemu.
A cause de cela, écoutez la parole du Seigneur, hommes opprimés, et vous, princes de ce peuple qui est en Jérusalem.
15 Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa, ife tachita mgwirizano ndi manda. Pamene mliri woopsa ukadzafika sudzatikhudza ife, chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.” (Sheol h7585)
Vous disiez: Nous avons fait un pacte avec l'enfer, et des conventions avec la mort; s'il passe un tourbillon impétueux, il ne viendra pas sur nous; nous avons fait du mensonge notre espérance, nous serons abrités par le mensonge. (Sheol h7585)
16 Tsono zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi: “Taonani, ndikuyika mwala wovomerezeka ndi amisiri ngati maziko mu Ziyoni, mwala wapangodya, wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu; munthu amene awukhulupirira sadzagwedezeka.
A cause de cela, ainsi dit le Seigneur, voilà que je mets dans les fondations de Sion une pierre de grand prix, une pierre choisie et précieuse; c'est la pierre angulaire et honorable des fondations; et celui qui croira en elle ne sera point confondu.
17 Ntchito zolungama zidzakhala ngati chingwe choyezera maziko ake, ndipo chilungamo chidzakhala chowongolera mzere; matalala adzawononga malo anu othawirapo, amene ndi mabodza, ndipo madzi adzamiza malo anu obisalako.
Et je rendrai un jugement, pour qu'il soit une espérance; et ma miséricorde sera pesée avec mesure; et vainement ils seront appuyés sur le mensonge; si le tourbillon a passé près de vous,
18 Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa; mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa. Pakuti mliri woopsa udzafika, ndipo udzakugonjetsani. (Sheol h7585)
Est-ce parce que Dieu n'a pu rompre votre alliance avec la mort, ni l'espérance que vous placiez sur l'enfer? Si le tourbillon impétueux passe, il vous foulera aux pieds; (Sheol h7585)
19 Ndipo ukadzangofika udzakutengani. Udzafika mmawa uliwonse, usiku ndi usana.” Anthu akadzamvetsetsa uthenga umenewu adzaopsedwa kwambiri.
S'il passe, il vous prendra dès l'aurore; dès l'aurore il passera, et il durera tout le jour, et la nuit votre attente sera pire encore. Instruisez-vous à comprendre,
20 Mudzakhala ngati munthu wogona pa bedi lalifupi kwambiri kuti sangathe kutambalitsapo miyendo; ndiponso mudzakhala ngati munthu amene wafunda bulangeti lochepa kwambiri kuti sangathe nʼkufunda komwe.
O vous qui êtes tourmentés, vous dites: Nous ne pouvons combattre, nous sommes trop faibles pour nous rassembler.
21 Yehova adzamenya nkhondo monga anachitira ku phiri la Perazimu adzakalipa monga anachitira ku chigwa cha Gibiyoni; adzagwira ntchito yake yooneka ngati yachilendo, ndipo zimene ati adzachite zidzakhala ngati zodabwitsa.
Le Seigneur s'élèvera contre vous, comme contre la montagne des impies, et il se tiendra dans la vallée de Gabaon; et il fera ses œuvres avec colère, œuvres d'amertume; et il agira avec un courroux qui lui est étranger, et il vous frappera d'une plaie qui lui est étrangère
22 Tsopano lekani kunyoza, mukapanda kutero maunyolo anu adzakuthinani kwambiri; Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse wandiwuza kuti, “Ndagamula kuti ndidzawononga dziko lapansi.”
Gardez-vous de vous réjouir et de rendre plus forts vos liens; car j'ai appris du Seigneur Dieu des armées les œuvres accomplies et prochaines qu'il fera par toute la terre.
23 Tcherani khutu ndipo mumve mawu anga; mvetserani ndipo mumve zimene ndikunena.
Prêtez l'oreille, écoutez ma voix, soyez attentifs et recueillez mes paroles.
24 Kodi mlimi wofuna kudzala mbewu amangokhalira kutipula kokhakokha? Kodi amangokhalira kugawula ndi kugalawuza kokhakokha?
Est-ce que le laboureur laboure toute la journée? Ne prépare-t-il pas la semence avant de travailler à la terre?
25 Pamene iye wasalaza mundawo, kodi samafesa mawere ndi chitowe? Kodi suja samadzala tirigu ndi barele mʼmizere yake, nadzala mchewere mʼphepete mwa mundawo?
Après en avoir aplani la surface, ne sème-t-il pas de la poivrette et du cumin? Ne sème-t-il pas ensuite du froment, de l'orge, du millet, de l'épeautre, selon ses desseins?
26 Mulungu wake amamulangiza ndi kumuphunzitsa njira yabwino.
Or tu seras instruit par le jugement de ton Dieu, et tu te réjouiras.
27 Mawere sapunthira chopunthira cha galeta lopanda mikombero, kapena chitowe sapuntha popondetsapo mikombero ya galeta; mawere amapuntha ndi ndodo ndipo chitowe amapuntha ndi kamtengo.
Car la poivrette n'est point nettoyée durement; on ne fait point passer les roues d'un char sur le cumin, mais on bat la poivrette avec une verge;
28 Tirigu ayenera kusinjidwa kuti apangire buledi, komabe munthu samangokhalira kupuntha tiriguyo osalekeza, kuopa kuti angatekedzeke. Ngakhale kuti amapuntha tiriguyo poyendetsapo mikombero ya galeta, koma akavalo ake satekedza tiriguyo.
Et on mange le cumin avec du pain. Ainsi moi, je ne serai pas éternellement irrité contre vous, et la voix de mon amertume ne vous écrasera point toujours.
29 Izinso zimachokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, wa uphungu wodabwitsa ndi wa nzeru zopambana.
Tous ces signes viennent du Seigneur des armées; méditez-les, et rejetez toute vaine consolation.

< Yesaya 28 >