< Yesaya 28 >

1 Tsoka ufumu wonyada wa zidakwa za ku Efereimu. Tsoka kwa ulemerero wake wokongola umene ukufota ngati duwa limene lili pa mutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde.
Malheur, couronne fastueuse des buveurs d’Ephraïm, diadème éphémère dont se pare son orgueil, qui entoure des têtes brillantes de parfums, étourdies par le vin!
2 Taonani, ambuye ali naye wina wamphamvu ndi nyonga. Iye adzabwera ngati mkuntho wamatalala ndi namondwe wowononga, ngati madzi amphamvu osefukira a mvula yamkuntho; ndipo adzawagwetsa pansi mwankhanza.
Voici venir, violent et impétueux, lancé par l’Eternel comme l’irruption de la grêle, un ouragan meurtrier; comme l’irruption de grandes eaux qui submergent tout, il le fait peser sur le sol avec puissance.
3 Ulamuliro wa atsogoleri oledzera a ku Efereimu adzawuthetsa.
Elle sera foulée aux pieds, la couronne fastueuse des buveurs d’Ephraïm,
4 Ndipo ulemerero wokongola wa mzinda umene uli ngati duwa lofota pamutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde uja, udzakhala ngati nkhuyu yoyambirira kupsa imene munthu akangoyiona amayithyola nthawi yokolola isanakwane.
et il adviendra de ce diadème flétri qui pare son orgueil, qui couronne sa tête brillante de parfums, comme d’une primeur avant l’été, laquelle, à peine aperçue, à peine dans la main, est déjà dévorée.
5 Tsiku limenelo Yehova Wamphamvuzonse adzakhala ngati nkhata yaufumu, chipewa chokongola kwa anthu ake otsala.
En ce jour, l’Eternel-Cebaot sera une couronne de gloire et un splendide diadème pour le reste de son peuple,
6 Iye adzapereka mtima wachilungamo kwa oweruza, adzakhala chilimbikitso kwa amene amabweza adani pa zipata za mzinda.
et une inspiration de justice à ceux qui siègent pour la justice, de courage à ceux qui repoussent les attaques près des portes.
7 Nawonso awa ali dzandidzandi chifukwa cha vinyo ndipo akusochera chifukwa cha mowa: ansembe ndi aneneri akudzandira chifukwa cha mowa ndipo akusokonezeka chifukwa cha vinyo; akusochera chifukwa cha mowa, akudzandira pamene akuona masomphenya, kupunthwa pamene akupereka chigamulo.
Toutefois, eux aussi sont troublés par le vin, égarés par la boisson; prêtre et prophète trébuchent à cause de la boisson, sont étourdis par le vin, pris de vertige par suite d’ivresse; leur vision est devenue trouble et ils vacillent dans leurs jugements.
8 Pa matebulo onse pali masanzi okhaokha ndipo palibenso malo wopanda zonyansa.
En effet, toutes les tables sont couvertes de vomissures et d’immondices; pas un coin n’y échappe.
9 Iwo akuti, “Kodi munthu ameneyu akufuna aphunzitse ndani? Uthengawu akufuna kufotokozera yani? Ndi kwa ana amene aleka kuyamwa, kwa makanda ongowachotsa kumene ku bere?
"À qui donc veut-il enseigner la science? À qui inculquer des leçons? À des enfants qui viennent d’être sevrés, de quitter la mamelle.
10 Akuyesa kumatiphunzitsa pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Zonsezi akungoti apa pangʼono apa pangʼono.”
Ce n’est que loi sur loi, précepte sur précepte, règle sur règle, ordre sur ordre, une vétille par ci, une vétille par là!"
11 Mulungu adzayankhula kwa anthu ake kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo, ziyankhulo zosamveka bwino. Mulungu adzayankhula kwa anthu awa, amene
Sans doute c’est dans une langue barbare et dans un idiome étranger qu’il parlait à ce peuple,
12 anakuwuzani kuti, “Malo opumulira ndi ano, otopa apumule, malo owusira ndi ano.” Koma inu simunamvere.
lorsqu’il leur disait: "Ceci est la paix donnez du relâche à ceux qui sont Ias ceci est le repos!" Ils n’ont pas voulu écouter.
13 Choncho Yehova adzakuphunzitsani pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Kotero mudzayenda ndi kugwa chambuyo, adzapweteka ndi kukodwa mu msampha ndipo adzakutengani ku ukapolo.
Ils n’ont vu dans la parole du Seigneur que loi sur loi, précepte sur précepte, règle sur règle, ordre sur ordre, une vétille par ci, une vétille par là, de sorte qu’en marchant ils trébuchent en arrière et se brisent, s’engagent dans le piège et s’y embarrassent.
14 Nʼchifukwa chake imvani mawu a Yehova, inu anthu achipongwe amene mumalamulira anthu awa mu Yerusalemu.
En vérité, écoutez la parole de l’Eternel, ô gens de raillerie, vous qui dominez ce peuple dans Jérusalem.
15 Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa, ife tachita mgwirizano ndi manda. Pamene mliri woopsa ukadzafika sudzatikhudza ife, chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.” (Sheol h7585)
Vous avez dit: "Nous avons contracté une alliance—avec la mort, conclu un pacte avec le Cheol; lorsque passera le fléau dévastateur, il ne nous atteindra pas, car nous avons fait de la fraude notre abri et du mensonge notre refuge." (Sheol h7585)
16 Tsono zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi: “Taonani, ndikuyika mwala wovomerezeka ndi amisiri ngati maziko mu Ziyoni, mwala wapangodya, wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu; munthu amene awukhulupirira sadzagwedezeka.
Mais ainsi a parlé le Seigneur, l’Eternel: Voici, je vais, dans Sion, ériger une pierre de fondation, une pierre éprouvée, une précieuse pierre d’angle solidement fixée; quiconque s’y appuiera ne sera pas réduit à fuir.
17 Ntchito zolungama zidzakhala ngati chingwe choyezera maziko ake, ndipo chilungamo chidzakhala chowongolera mzere; matalala adzawononga malo anu othawirapo, amene ndi mabodza, ndipo madzi adzamiza malo anu obisalako.
J’Emploierai le droit comme cordeau et la justice comme fil à plomb; la grêle balayera l’abri de la fraude et les eaux entraîneront son refuge.
18 Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa; mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa. Pakuti mliri woopsa udzafika, ndipo udzakugonjetsani. (Sheol h7585)
Alors sera rompue votre alliance avec la mort, votre pacte avec le Cheol ne tiendra pas: lorsque s’avancera le fléau dévastateur, vous en serez écrasés. (Sheol h7585)
19 Ndipo ukadzangofika udzakutengani. Udzafika mmawa uliwonse, usiku ndi usana.” Anthu akadzamvetsetsa uthenga umenewu adzaopsedwa kwambiri.
Toutes les fois qu’il passera, il vous emportera; matin après matin il passera, le jour et la nuit, et rien que d’en percevoir le bruit sera un sujet d’épouvante.
20 Mudzakhala ngati munthu wogona pa bedi lalifupi kwambiri kuti sangathe kutambalitsapo miyendo; ndiponso mudzakhala ngati munthu amene wafunda bulangeti lochepa kwambiri kuti sangathe nʼkufunda komwe.
Trop courte sera la couche pour s’y étendre, et trop étroite la couverture pour s’y envelopper.
21 Yehova adzamenya nkhondo monga anachitira ku phiri la Perazimu adzakalipa monga anachitira ku chigwa cha Gibiyoni; adzagwira ntchito yake yooneka ngati yachilendo, ndipo zimene ati adzachite zidzakhala ngati zodabwitsa.
Car l’Eternel se lèvera comme sur la montagne de Peracim, et il manifestera sa colère comme dans la vallée de Gabaon, pour accomplir son œuvre étrange est son œuvre, et pour exécuter son labeur extraordinaire est son labeur.
22 Tsopano lekani kunyoza, mukapanda kutero maunyolo anu adzakuthinani kwambiri; Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse wandiwuza kuti, “Ndagamula kuti ndidzawononga dziko lapansi.”
Maintenant donc, trêve à vos railleries! Elles renforceraient vos chaînes; car c’est un arrêt de destruction que j’ai entendu prononcer par le Seigneur, l’Eternel-Cebaot, contre tout le pays.
23 Tcherani khutu ndipo mumve mawu anga; mvetserani ndipo mumve zimene ndikunena.
Prêtez l’oreille et écoutez ma voix, soyez attentifs et entendez mon discours.
24 Kodi mlimi wofuna kudzala mbewu amangokhalira kutipula kokhakokha? Kodi amangokhalira kugawula ndi kugalawuza kokhakokha?
Le laboureur passe-t-il tout son temps à labourer en vue de semer? À fendre le sol et à promener la herse dans son champ?
25 Pamene iye wasalaza mundawo, kodi samafesa mawere ndi chitowe? Kodi suja samadzala tirigu ndi barele mʼmizere yake, nadzala mchewere mʼphepete mwa mundawo?
N’Est-ce pas? Quand il en a égalisé la surface, il y répand de la vesce, y jette du cumin, sème le froment dans les sillons, l’orge aux endroits désignés et l’épeautre sur les bords.
26 Mulungu wake amamulangiza ndi kumuphunzitsa njira yabwino.
C’Est son Dieu qui lui a enseigné la règle à suivre, c’est lui qui l’a instruit.
27 Mawere sapunthira chopunthira cha galeta lopanda mikombero, kapena chitowe sapuntha popondetsapo mikombero ya galeta; mawere amapuntha ndi ndodo ndipo chitowe amapuntha ndi kamtengo.
De même ce n’est pas avec le rouleau tranchant que la vesce est battue, ce n’est pas la roue du chariot qu’on fait passer sur le cumin: la vesce est battue avec le bâton et le cumin avec la verge.
28 Tirigu ayenera kusinjidwa kuti apangire buledi, komabe munthu samangokhalira kupuntha tiriguyo osalekeza, kuopa kuti angatekedzeke. Ngakhale kuti amapuntha tiriguyo poyendetsapo mikombero ya galeta, koma akavalo ake satekedza tiriguyo.
Mais le blé dont on fait le pain doit être écrasé; il ne sert de rien de le battre indéfiniment, d’y faire passer avec force les roues du chariot et les chevaux, ce qui ne le réduit pas en poussière.
29 Izinso zimachokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, wa uphungu wodabwitsa ndi wa nzeru zopambana.
Cela aussi émane de l’Eternel-Cebaot: il conçoit des desseins merveilleux et déploie une haute sagesse.

< Yesaya 28 >