< Yesaya 28 >
1 Tsoka ufumu wonyada wa zidakwa za ku Efereimu. Tsoka kwa ulemerero wake wokongola umene ukufota ngati duwa limene lili pa mutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde.
Woe to the crown of pride, to the drunkards of Ephraim, and to the fading flower the glory of his joy, who were on the head of the fat valley, staggering with wine.
2 Taonani, ambuye ali naye wina wamphamvu ndi nyonga. Iye adzabwera ngati mkuntho wamatalala ndi namondwe wowononga, ngati madzi amphamvu osefukira a mvula yamkuntho; ndipo adzawagwetsa pansi mwankhanza.
Behold the Lord is mighty and strong, as a storm of hail: a destroying whirlwind, as the violence of many waters overflowing, and sent forth upon a spacious land.
3 Ulamuliro wa atsogoleri oledzera a ku Efereimu adzawuthetsa.
The crown of pride of the drunkards of Ephraim shall be trodden under feet.
4 Ndipo ulemerero wokongola wa mzinda umene uli ngati duwa lofota pamutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde uja, udzakhala ngati nkhuyu yoyambirira kupsa imene munthu akangoyiona amayithyola nthawi yokolola isanakwane.
And the fading flower the glory of his joy, who is on the head of the fat valley, shall be as a hasty fruit before the ripeness of autumn: which when he that seeth it shall behold, as soon as he taketh it in his hand, he will eat it up.
5 Tsiku limenelo Yehova Wamphamvuzonse adzakhala ngati nkhata yaufumu, chipewa chokongola kwa anthu ake otsala.
In that day the Lord of hosts shall be a crown of glory, and a garland of joy to the residue of his people:
6 Iye adzapereka mtima wachilungamo kwa oweruza, adzakhala chilimbikitso kwa amene amabweza adani pa zipata za mzinda.
And a spirit of judgment to him that sitteth in judgment, and strength to them that return out of the battle to the gate.
7 Nawonso awa ali dzandidzandi chifukwa cha vinyo ndipo akusochera chifukwa cha mowa: ansembe ndi aneneri akudzandira chifukwa cha mowa ndipo akusokonezeka chifukwa cha vinyo; akusochera chifukwa cha mowa, akudzandira pamene akuona masomphenya, kupunthwa pamene akupereka chigamulo.
But these also have been ignorant through wine, and through drunkenness have erred: the priest and the prophet have been ignorant through drunkenness, they are swallowed up with wine, they have gone astray in drunkenness, they have not known him that seeth, they have been ignorant of judgment.
8 Pa matebulo onse pali masanzi okhaokha ndipo palibenso malo wopanda zonyansa.
For all tables were full of vomit and filth, so that there was no more place.
9 Iwo akuti, “Kodi munthu ameneyu akufuna aphunzitse ndani? Uthengawu akufuna kufotokozera yani? Ndi kwa ana amene aleka kuyamwa, kwa makanda ongowachotsa kumene ku bere?
Whom shall he teach knowledge? and whom shall he make to understand the hearing? them that are weaned from the milk, that are drawn away from the breasts.
10 Akuyesa kumatiphunzitsa pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Zonsezi akungoti apa pangʼono apa pangʼono.”
For command, command again; command, command again; expect, expect again; expect, expect again: a little there, a little there.
11 Mulungu adzayankhula kwa anthu ake kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo, ziyankhulo zosamveka bwino. Mulungu adzayankhula kwa anthu awa, amene
For with the speech of lips, and with another tongue he will speak to this people.
12 anakuwuzani kuti, “Malo opumulira ndi ano, otopa apumule, malo owusira ndi ano.” Koma inu simunamvere.
To whom he said: This is my rest, refresh the weary, and this is my refreshing: and they would not hear.
13 Choncho Yehova adzakuphunzitsani pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Kotero mudzayenda ndi kugwa chambuyo, adzapweteka ndi kukodwa mu msampha ndipo adzakutengani ku ukapolo.
And the word of the Lord shall be to them: Command, command again; command, command again: expect, expect again; expect, expect again: a little there, a little there: that they may go, and fall backward, and be broken, and snared, and taken.
14 Nʼchifukwa chake imvani mawu a Yehova, inu anthu achipongwe amene mumalamulira anthu awa mu Yerusalemu.
Wherefore hear the word of the Lord, ye scornful men, who rule over my people that is in Jerusalem.
15 Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa, ife tachita mgwirizano ndi manda. Pamene mliri woopsa ukadzafika sudzatikhudza ife, chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.” (Sheol )
For you have said: We have entered into a league with death, and we have made a covenant with hell. When the overflowing scourge shall pass through, it shall not come upon us: for we have placed our hope in lies, and by falsehood we are protected. (Sheol )
16 Tsono zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi: “Taonani, ndikuyika mwala wovomerezeka ndi amisiri ngati maziko mu Ziyoni, mwala wapangodya, wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu; munthu amene awukhulupirira sadzagwedezeka.
Therefore thus saith the Lord God: Behold I will lay a stone in the foundations of Sion, a tried stone, a corner stone, a precious stone, founded in the foundation. He that believeth, let him not hasten.
17 Ntchito zolungama zidzakhala ngati chingwe choyezera maziko ake, ndipo chilungamo chidzakhala chowongolera mzere; matalala adzawononga malo anu othawirapo, amene ndi mabodza, ndipo madzi adzamiza malo anu obisalako.
And I will set judgment in weight, and justice in measure: and hail shall overturn the hope of falsehood: and waters shall overflow its protection.
18 Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa; mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa. Pakuti mliri woopsa udzafika, ndipo udzakugonjetsani. (Sheol )
And Sour league with death shall be abolished, and your covenant with hell shall not stand: when the overflowing scourge shall pass, you shall be trodden down by it. (Sheol )
19 Ndipo ukadzangofika udzakutengani. Udzafika mmawa uliwonse, usiku ndi usana.” Anthu akadzamvetsetsa uthenga umenewu adzaopsedwa kwambiri.
Whensoever it shall pass through, it shall take you away: because in the morning early it shall pass through, in the day and in the night, and vexation alone shall make you understand what you hear.
20 Mudzakhala ngati munthu wogona pa bedi lalifupi kwambiri kuti sangathe kutambalitsapo miyendo; ndiponso mudzakhala ngati munthu amene wafunda bulangeti lochepa kwambiri kuti sangathe nʼkufunda komwe.
For the bed is straitened, so that one must fall out, and a short covering cannot cover both.
21 Yehova adzamenya nkhondo monga anachitira ku phiri la Perazimu adzakalipa monga anachitira ku chigwa cha Gibiyoni; adzagwira ntchito yake yooneka ngati yachilendo, ndipo zimene ati adzachite zidzakhala ngati zodabwitsa.
For the Lord shall stand up as in the mountain of divisions: he shall be angry as in the valley which is in Gabaon: that he may do his work, his strange work: that he may perform his work, his work is strange to him.
22 Tsopano lekani kunyoza, mukapanda kutero maunyolo anu adzakuthinani kwambiri; Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse wandiwuza kuti, “Ndagamula kuti ndidzawononga dziko lapansi.”
And now do not mock, lest your bonds be tied strait. For I have heard of the Lord the God of hosts a consumption and a cutting short upon all the earth.
23 Tcherani khutu ndipo mumve mawu anga; mvetserani ndipo mumve zimene ndikunena.
Give ear, and hear my voice, hearken, and hear my speech.
24 Kodi mlimi wofuna kudzala mbewu amangokhalira kutipula kokhakokha? Kodi amangokhalira kugawula ndi kugalawuza kokhakokha?
Shall the ploughman plough all the day to sow, shall he open and harrow his ground?
25 Pamene iye wasalaza mundawo, kodi samafesa mawere ndi chitowe? Kodi suja samadzala tirigu ndi barele mʼmizere yake, nadzala mchewere mʼphepete mwa mundawo?
Will he not, when he hath made plain the surface thereof, sow gith, and scatter cummin, and put wheat in order, and barley, and millet, and vetches in their bounds?
26 Mulungu wake amamulangiza ndi kumuphunzitsa njira yabwino.
For he will instruct him in judgment: his God will teach him.
27 Mawere sapunthira chopunthira cha galeta lopanda mikombero, kapena chitowe sapuntha popondetsapo mikombero ya galeta; mawere amapuntha ndi ndodo ndipo chitowe amapuntha ndi kamtengo.
For gith shall not be thrashed with saws, neither shall the cart wheel turn about upon cummin: but gith shall be beaten out with a rod, and cummin with a staff.
28 Tirigu ayenera kusinjidwa kuti apangire buledi, komabe munthu samangokhalira kupuntha tiriguyo osalekeza, kuopa kuti angatekedzeke. Ngakhale kuti amapuntha tiriguyo poyendetsapo mikombero ya galeta, koma akavalo ake satekedza tiriguyo.
But bread corn shall be broken small: but the thrasher shall not thrash it for ever, neither shall the cart wheel hurt it, nor break it with its teeth.
29 Izinso zimachokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, wa uphungu wodabwitsa ndi wa nzeru zopambana.
This also is come forth from the Lord God of hosts, to make his counsel wonderful, and magnify justice.