< Yesaya 27 >

1 Tsiku limenelo, Yehova ndi lupanga lake lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu, adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija, Leviyatani chinjoka chodzikulunga; adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
O gün RAB Livyatan'ı, o kaçan yılanı, Evet Livyatan'ı, o kıvrıla kıvrıla giden yılanı Acımasız, kocaman, güçlü kılıcıyla cezalandıracak, Denizdeki canavarı öldürecek.
2 Tsiku limenelo Yehova adzati, “Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
O gün RAB, “Sevdiğim bağ için ezgiler söyleyin” diyecek,
3 Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira; ndimawuthirira nthawi zonse. Ndimawulondera usana ndi usiku kuti wina angawononge.
“Ben RAB, bağın koruyucusuyum, Onu sürekli sularım. Kimse zarar vermesin diye Gece gündüz beklerim.
4 Ine sindinakwiye. Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo! Ndikachita nazo nkhondo; ndikanazitentha zonse ndi moto.
Kızgın değilim. Keşke karşıma dikenli çalılar çıksa! Onların üzerine yürür, Tümünü ateşe verirdim.
5 Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze; apangane nane za mtendere, ndithu, apangane nane za mtendere.”
Ya da koruyuculuğuma sarılsınlar, Barışsınlar benimle, Evet, benimle barışsınlar.”
6 Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu, Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa, ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
Yakup soyu gelecekte kök salacak, İsrail filizlenip çiçeklenecek, Yeryüzünü meyvesiyle dolduracak.
7 Kodi Yehova anakantha Israeli ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli? Kapena kodi Yehova anapha Israeli ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
RAB İsrailliler'i, kendilerini cezalandıranları cezalandırdığı gibi cezalandırdı mı? Ya da İsrailliler'i başkalarını öldürdüğü gibi öldürdü mü?
8 Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo, mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa, monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
RAB onları yargıladı, Kovup sürgüne gönderdi. Doğu rüzgarının estiği gün Onları şiddetli soluğuyla savurdu.
9 Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo. Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja, ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha. Sipadzapezekanso mafano a Asera kapena maguwa ofukiza lubani.
Böylece Yakup soyunun suçu bağışlanacak. Günahlarının kaldırılmasının sonucu şöyle olacak: Sunağın taşlarını tebeşir taşı gibi un ufak ettiklerinde Ne Aşera putu ne de buhur sunağı kalacak.
10 Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja, wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu; kumeneko amadyetselako ana angʼombe kumeneko zimapumulako ziweto ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
Surlu kent terk edildi, Çöl kadar ıssız, sahipsiz bir yurt oldu. Dana orada otlayıp uzanacak, Filizlerini yiyip bitirecek.
11 Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni. Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru; kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni, ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
Kuruyan dalları koparılacak, Kadınlar gelip bunları yakacaklar. Çünkü bu halk akıllı bir halk değil. Bu yüzden onları yaratan kendilerine acımayacak, Onlara biçim veren onları kayırmayacak.
12 Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
Ey İsrailoğulları, o gün RAB gürül gürül akan Fırat ile Mısır Vadisi arasında harman döver gibi, sizi birer birer toplayacak.
13 Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.
Evet, o gün büyük bir boru çalınacak; Asur'da yitenlerle Mısır'a sürgün edilenler gelip kutsal dağda, Yeruşalim'de RAB'be tapınacaklar.

< Yesaya 27 >