< Yesaya 27 >
1 Tsiku limenelo, Yehova ndi lupanga lake lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu, adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija, Leviyatani chinjoka chodzikulunga; adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
Na tisti dan bo Gospod s svojim bridkim, velikim in močnim mečem kaznoval leviatána in ostro kačo, celó leviatána, to sprijeno kačo in pokončal bo zmaja, ki je v morju.
2 Tsiku limenelo Yehova adzati, “Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
Na tisti dan ji pojte: »Vinograd rdečega vina.«
3 Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira; ndimawuthirira nthawi zonse. Ndimawulondera usana ndi usiku kuti wina angawononge.
Jaz, Gospod, ga varujem; vsak trenutek ga bom zalival. Da ga ne bi kdorkoli poškodoval, ga bom varoval noč in dan.
4 Ine sindinakwiye. Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo! Ndikachita nazo nkhondo; ndikanazitentha zonse ndi moto.
Razjarjenosti ni v meni. Kdo bi zoper mene v bitki postavil osat in trnje? Šel bi skoznje, skupaj bi jih požgal.
5 Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze; apangane nane za mtendere, ndithu, apangane nane za mtendere.”
Ali pa naj se oprime moje moči, da lahko sklene mir z menoj in sklenil bo mir z menoj.
6 Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu, Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa, ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
Tistim, ki pridejo iz Jakoba, bo povzročil, da se ukoreninijo. Izrael bo cvetel, brstel in obličje zemeljskega [kroga] bo napolnil s sadom.
7 Kodi Yehova anakantha Israeli ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli? Kapena kodi Yehova anapha Israeli ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
Mar ga je udaril, kakor je on udaril tiste, ki so ga udarili? Mar je umorjen glede na pokol tistih, ki so umorjeni po njem?
8 Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo, mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa, monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
Po meri, ko ta poganja naprej, boš razpravljal z njim. On ustavlja njegov oster veter na dan vzhodnika.
9 Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo. Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja, ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha. Sipadzapezekanso mafano a Asera kapena maguwa ofukiza lubani.
Torej s tem bo Jakobova krivičnost očiščena in to je ves sad, da odvzame njegov greh, ko vse oltarne kamne naredi kakor apnenčaste kamne, ki so raztreščeni narazen; ašere in podobe ne bodo obstale.
10 Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja, wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu; kumeneko amadyetselako ana angʼombe kumeneko zimapumulako ziweto ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
Vendar bo obrambno mesto opustelo in prebivališče zapuščeno in opuščeno kakor divjina. Tam se bo paslo tele in tam se bo uleglo in použilo njegove mladike.
11 Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni. Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru; kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni, ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
Ko njegove veje ovenijo, bodo odlomljene. Prišle bodo ženske in jih zažgale. Kajti to je ljudstvo brez razumevanja, zato tisti, ki jih je naredil, ne bo imel usmiljenja do njih in kdor jih je oblikoval, jim ne bo izkazal nobene naklonjenosti.
12 Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
Na tisti dan se bo zgodilo, da bo Gospod otepal od rečnega kanala do egiptovskega vodotoka in zbrani boste drug za drugim, oh vi, Izraelovi otroci.
13 Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.
Na tisti dan se bo zgodilo, da bo zatrobljeno na velik šofar in prišli bodo, ki so bili pripravljeni, da se pogubijo v asirski deželi in [ki so bili] pregnanci v egiptovski deželi in oboževali bodo Gospoda na sveti gori pri Jeruzalemu.