< Yesaya 27 >

1 Tsiku limenelo, Yehova ndi lupanga lake lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu, adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija, Leviyatani chinjoka chodzikulunga; adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
در آن روز خداوند به شمشیر سخت عظیم محکم خود آن مار تیز رو لویاتان را و آن مار پیچیده لویاتان را سزا خواهد داد و آن اژدها را که در دریا است خواهد کشت.۱
2 Tsiku limenelo Yehova adzati, “Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
در آن روز برای آن تاکستان شراب بسرایید.۲
3 Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira; ndimawuthirira nthawi zonse. Ndimawulondera usana ndi usiku kuti wina angawononge.
من که یهوه هستم آن را نگاه می‌دارم و هر دقیقه آن راآبیاری می‌نمایم. شب و روز آن را نگاهبانی می‌نمایم که مبادا احدی به آن ضرر برساند.۳
4 Ine sindinakwiye. Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo! Ndikachita nazo nkhondo; ndikanazitentha zonse ndi moto.
خشم ندارم. کاش که خس و خار با من به جنگ می‌آمدند تا بر آنها هجوم آورده، آنها را با هم می‌سوزانیدم.۴
5 Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze; apangane nane za mtendere, ndithu, apangane nane za mtendere.”
یا به قوت من متمسک می‌شد تا بامن صلح بکند و با من صلح می‌نمود.۵
6 Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu, Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa, ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
در ایام آینده یعقوب ریشه خواهد زد واسرائیل غنچه و شکوفه خواهد آورد. و ایشان روی ربع مسکون را از میوه پر خواهند ساخت.۶
7 Kodi Yehova anakantha Israeli ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli? Kapena kodi Yehova anapha Israeli ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
آیا او را زد بطوری که دیگران او را زدند؟ یاکشته شد بطوری که مقتولان وی کشته شدند؟۷
8 Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo, mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa, monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
چون او را دور ساختی به اندازه با وی معارضه نمودی. با باد سخت خویش او را در روز بادشرقی زایل ساختی.۸
9 Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo. Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja, ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha. Sipadzapezekanso mafano a Asera kapena maguwa ofukiza lubani.
بنابراین گناه یعقوب از این کفاره شده و رفع گناه او تمامی نتیجه آن است. چون تمامی سنگهای مذبح را مثل سنگهای آهک نرم شده می‌گرداند آنگاه اشیریم و بتهای آفتاب دیگر برپا نخواهد شد.۹
10 Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja, wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu; kumeneko amadyetselako ana angʼombe kumeneko zimapumulako ziweto ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
زیرا که آن شهرحصین منفرد خواهد شد و آن مسکن، مهجور ومثل بیابان واگذاشته خواهد شد. در آنجاگوساله‌ها خواهند چرید و در آن خوابیده، شاخه هایش را تلف خواهند کرد.۱۰
11 Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni. Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru; kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni, ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
چون شاخه هایش خشک شود شکسته خواهد شد. پس زنان آمده، آنها را خواهند سوزانید، زیرا که ایشان قوم بیفهم هستند. لهذا آفریننده ایشان برایشان ترحم نخواهد نمود و خالق ایشان بر ایشان شفقت نخواهد کرد.۱۱
12 Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
و در آن روز واقع خواهد شد که خداوند ازمسیل نهر (فرات ) تا وادی مصر غله را خواهدکوبید. و شما‌ای بنی‌اسرائیل یکی یکی جمع کرده خواهید شد.۱۲
13 Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.
و در آن روز واقع خواهدشد که کرنای بزرگ نواخته خواهد شد وگم شدگان زمین آشور و رانده شدگان زمین مصرخواهند آمد. و خداوند را در کوه مقدس یعنی دراورشلیم عبادت خواهند نمود.۱۳

< Yesaya 27 >