< Yesaya 27 >

1 Tsiku limenelo, Yehova ndi lupanga lake lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu, adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija, Leviyatani chinjoka chodzikulunga; adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
Ngalolosuku iNkosi ngenkemba yayo elukhuni lenkulu lelamandla izajezisa uLeviyathani, inyoka ebalekayo, ngitsho uLeviyathani inyoka egoqanayo, ibulale umgobho oselwandle.
2 Tsiku limenelo Yehova adzati, “Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
Ngalolosuku hlabelelani ngaso isivini sewayini elibomvu.
3 Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira; ndimawuthirira nthawi zonse. Ndimawulondera usana ndi usiku kuti wina angawononge.
Mina Nkosi, ngiyasilondoloza, ngiyasithelela isikhathi sonke; hlezi kube khona osonayo ngisilondoloze ebusuku lemini.
4 Ine sindinakwiye. Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo! Ndikachita nazo nkhondo; ndikanazitentha zonse ndi moto.
Ukuthukuthela kakukho kimi. Ngubani ongabeka ukhula oluhlabayo lameva kumelane lami empini? Bengizamatsha ngidabule phakathi kwakho, ngikutshise kanyekanye.
5 Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze; apangane nane za mtendere, ndithu, apangane nane za mtendere.”
Kumbe kabambelele emandleni ami, enze ukuthula lami; uzakwenza ukuthula lami.
6 Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu, Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa, ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
Izakwenza abavela koJakobe bagxile, uIsrayeli uzahluma, akhahlele, agcwalise ubuso bomhlaba ngezithelo.
7 Kodi Yehova anakantha Israeli ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli? Kapena kodi Yehova anapha Israeli ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
Imtshayile yini njengokutshaya kwayo oyitshayayo? Ubulewe yini njengokubulawa kwababuleweyo bakhe?
8 Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo, mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa, monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
Ngesilinganiso ekukuxotsheni izaphikisana lakho; izakususa ngomoya wayo olukhuni ngosuku lomoya wempumalanga.
9 Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo. Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja, ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha. Sipadzapezekanso mafano a Asera kapena maguwa ofukiza lubani.
Ngakho ngalokhu isiphambeko sikaJakobe sizahlawulelwa; lalokhu kuyisithelo sonke sokususa isono sakhe, lapho esenza ukuthi wonke amatshe elathi abe njengamatshe ekalaga avuthuziweyo, izixuku lamalathi elanga kakuyikuma.
10 Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja, wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu; kumeneko amadyetselako ana angʼombe kumeneko zimapumulako ziweto ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
Ngoba umuzi obiyelweyo uzakuba wodwa, indawo yokuhlala ixotshwe, itshiywe njengenkangala; lapho ithole lizakudla khona, lilale khona, liqede izingatsha zawo.
11 Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni. Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru; kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni, ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
Lapho ingatsha zawo sezomile zizakwephulwa; abesifazana beze bazibase; ngoba kabasibantu abaqedisisayo; ngakho-ke lowo owabenzayo kayikubahawukela, lowababumbayo kayikubatshengisa umusa.
12 Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
Kuzakuthi-ke ngalolosuku iNkosi ibhule kusukela esifudlaneni somfula kuze kube semfuleni weGibhithe; lina-ke lizabuthwa ngamunye ngamunye, bantwana bakoIsrayeli.
13 Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.
Kuzakuthi-ke ngalolosuku kuvuthelwe uphondo olukhulu, lalabo ababebhubhe elizweni leAsiriya labaxotshelwe elizweni leGibhithe, bazabuya bayikhonze iNkosi entabeni engcwele eJerusalema.

< Yesaya 27 >