< Yesaya 27 >

1 Tsiku limenelo, Yehova ndi lupanga lake lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu, adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija, Leviyatani chinjoka chodzikulunga; adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
V ten den navštíví Hospodin mečem svým přísným, velikým a mocným Leviatana, hada dlouhého, a Leviatana, hada stočilého, a zabije draka, kterýž jest v moři.
2 Tsiku limenelo Yehova adzati, “Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
V ten den o vinici výborné víno vydávající zpívejte.
3 Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira; ndimawuthirira nthawi zonse. Ndimawulondera usana ndi usiku kuti wina angawononge.
Já Hospodin, kterýž ji ostříhám, každé chvilky budu ji svlažovati, a aby jí někdo neuškodil, v noci i ve dne ji ostříhati.
4 Ine sindinakwiye. Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo! Ndikachita nazo nkhondo; ndikanazitentha zonse ndi moto.
Prchlivosti při mně žádné není. Kdož mi dá bodlák a trn, abych proti ní válčil, a spálil ji docela?
5 Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze; apangane nane za mtendere, ndithu, apangane nane za mtendere.”
Zdali sváže sílu mou, aby učinil se mnou pokoj, aby pravím, učinil se mnou pokoj?
6 Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu, Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa, ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
Vždyť na to přijde, že se vkoření Jákob, zkvetne a zroste Izrael, a naplní okršlek zemský ovocem.
7 Kodi Yehova anakantha Israeli ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli? Kapena kodi Yehova anapha Israeli ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
Nebo zdaliž jej tak ubil, jako ubil nepřítele jeho? Zdali jej zamordoval, jako jsou jiní zmordováni od něho?
8 Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo, mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa, monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
Vedlé míry trestal jej i tehdáž, když jej zavesti dal, ješto nepřítele zachvátil větrem svým tuhým východním.
9 Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo. Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja, ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha. Sipadzapezekanso mafano a Asera kapena maguwa ofukiza lubani.
A protož tím způsobem očištěna bude nepravost Jákobova, a toť bude veliký užitek, že odejme hřích jeho, když rozmece všecko kamení oltáře jako kamení vápenné rozsypané, neostojí hájové, ani sluneční obrazové;
10 Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja, wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu; kumeneko amadyetselako ana angʼombe kumeneko zimapumulako ziweto ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
Když město hrazené zpustne, a bude příbytkem zavrženým a opuštěným jako poušť, tam pásti se bude tele, a tam léhati, a pokazí docela výstřelky jeho.
11 Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni. Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru; kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni, ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
Když počne zráti žeň jeho, potřína bude; ženy přijdouce, zapálí ji. Nebo ten lid nemá žádného rozumu; protož neslituje se nad ním učinitel jeho, a stvořitel jeho neučiní jemu milosti.
12 Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
I stane se v ten den, když pomstu uvoditi bude Hospodin od toku řeky až do potoka Egyptského, že vy, synové Izraelští, po jednom sebráni budete.
13 Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.
Stane se také v ten den, že troubeno bude trubou velikou, i přijdou, kteříž byli zahynuli v zemi Assyrské, a zahnáni byli do země Egyptské, a klaněti se budou Hospodinu na hoře svaté v Jeruzalémě.

< Yesaya 27 >