< Yesaya 27 >

1 Tsiku limenelo, Yehova ndi lupanga lake lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu, adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija, Leviyatani chinjoka chodzikulunga; adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.
到那一天,上主要用他那厲害、巨大、猛烈的劍,來懲罰「里外雅堂」飛龍,和「里外雅堂」蜿蛇;並要擊殺海中的蛟龍。
2 Tsiku limenelo Yehova adzati, “Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
到那一天,你們要唱「那可愛的葡萄園」歌:「
3 Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira; ndimawuthirira nthawi zonse. Ndimawulondera usana ndi usiku kuti wina angawononge.
我,上主,親自作它的護守者,時加灌溉;我要日夜護守,免得受人侵害。
4 Ine sindinakwiye. Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo! Ndikachita nazo nkhondo; ndikanazitentha zonse ndi moto.
我再沒有怒氣;萬一有了荊棘和蒺藜,我必前去攻擊,將它完全焚毀;
5 Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze; apangane nane za mtendere, ndithu, apangane nane za mtendere.”
除非不求我保護,不與我講和,不與我和好...」
6 Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu, Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa, ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.
來自雅各伯將生根,以色列要發芽開花,她的果實要佈滿地面。
7 Kodi Yehova anakantha Israeli ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli? Kapena kodi Yehova anapha Israeli ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
上主打擊以色列,那裏像他打擊那些打擊以色列的人呢﹖上主擊殺以色列,那裏像他擊殺那些擊殺以色列的人呢﹖
8 Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo, mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa, monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
上主以離棄,以驅逐,懲罰了她;在吹東風的日子,藉巨風將她捲去。
9 Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo. Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja, ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha. Sipadzapezekanso mafano a Asera kapena maguwa ofukiza lubani.
惟其如此,雅各伯的罪過方得消除;她的罪孽得以赦免的代價,即在於她將祭壇所有的石塊,打得粉碎有如石灰,不在樹立「阿舍辣」和太陽柱。
10 Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja, wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu; kumeneko amadyetselako ana angʼombe kumeneko zimapumulako ziweto ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
的確,設防的城市已荒涼,成了被撇下和放棄的住宅,有如荒野。牛犢在那裏牧放,在那裏偃臥,吃盡了那裏的枝葉。
11 Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni. Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru; kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni, ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.
幾時樹枝枯萎,就自會斷落,婦女便來拿去燒火;她既不是個聰敏的民族,因此那創造她的,對她沒有憐憫;那形成她的,對她也不表恩情。
12 Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto.
到那一天,上主要從大河流域到埃及河畔收割果實,以色列子民啊!你們都要一個一個地被聚集起來。
13 Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.
到那一天,要吹起大號筒,凡是在亞述失迷的,在埃及地分散的,都要前來,在耶路撒冷聖山,朝拜上主。

< Yesaya 27 >